< ЗАХАРИЯ 13 >
1 Ын зиуа ачея, се ва дескиде касей луй Давид ши локуиторилор Иерусалимулуй ун извор пентру пэкат ши некурэцие.
“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 Ын зиуа ачея”, зиче Домнул оштирилор, „вой стырпи дин царэ нумеле идолилор, ка нимень сэ ну-шь май адукэ аминте де ей; вой скоате, де асеменя, дин царэ пе пророчий минчиношь ши духул некурат.
“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
3 Ши, дакэ ва май пророчь чинева, атунч татэл сэу ши мама са, ыншишь пэринций луй, ый вор зиче: ‘Ту ну вей трэи, кэч ай спус минчунь ын Нумеле Домнулуй’; ши татэл сэу ши мама са, чей каре л-ау нэскут, ыл вор стрэпунӂе кынд ва пророчь.
Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 Ын зиуа ачея, пророчий се вор рушина, фиекаре, де веденииле лор кынд вор пророчь ши ну се вор май ымбрэка ынтр-о манта де пэр ка сэ минтэ пе оамень.
“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
5 Чи фиекаре дин ей ва зиче: ‘Еу ну сунт пророк, чи сунт плугар, кэч ам фост кумпэрат дин тинереця мя!’
Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
6 Ши дакэ-л ва ынтреба чинева: ‘Де унде вин ачесте рэнь пе каре ле ай ла мынь?’, ел ва рэспунде: ‘Ын каса челор че мэ юбяу ле-ам примит.’
Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
7 Скоалэ-те, сабие, асупра пэсторулуй Меу ши асупра омулуй каре ымь есте товарэш!”, зиче Домнул оштирилор. „Ловеште пе пэстор ши се вор рисипи оиле! Ши Ымь вой ынтоарче мына спре чей мичь.
“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 Ын тоатэ цара”, зиче Домнул, „доуэ треимь вор фи нимичите, вор пери, яр чялалтэ треиме ва рэмыне.
Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 Дар треимя ачаста дин урмэ о вой пуне ын фок ши о вой курэци кум се курэцеште арӂинтул, о вой лэмури кум се лэмуреште аурул. Ей вор кема Нумеле Меу ши ый вой аскулта; Еу вой зиче: ‘Ачеста есте попорул Меу!’ Ши ей вор зиче: ‘Домнул есте Думнезеул меу!’”
Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”