< Романь 10 >
1 Фрацилор, доринца инимий меле, ши ругэчуня мя кэтре Думнезеу, пентру исраелиць есте сэ фие мынтуиць.
Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe.
2 Ле мэртурисеск кэ ей ау рывнэ пентру Думнезеу, дар фэрэ причепере,
Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso.
3 пентру кэ, ынтрукыт н-ау куноскут неприхэниря пе каре о дэ Думнезеу, ау кэутат сэ-шь пунэ ынаинте о неприхэнире а лор ыншишь ши ну с-ау супус астфел неприхэнирий пе каре о дэ Думнезеу.
Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu.
4 Кэч Христос есте сфыршитул Леӂий, пентру ка орьчине креде ын Ел сэ поатэ кэпэта неприхэниря.
Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.
5 Ын адевэр, Мойсе скрие кэ омул каре ымплинеште неприхэниря пе каре о дэ Леӂя ва трэи прин еа.
Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
6 Пе кынд ятэ кум ворбеште неприхэниря пе каре о дэ крединца: „Сэ ну зичь ын инима та: ‘Чине се ва суи ын чер?’ (Сэ кобоаре адикэ пе Христос дин чер)
Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’” (ndiko, kukatsitsa Khristu)
7 сау: ‘Чине се ва коборы ын адынк?’ (Сэ скоале адикэ пе Христос дин морць.)” (Abyssos )
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos )
8 Че зиче еа деч? „Кувынтул есте апроапе де тине: ын гура та ши ын инима та.” Ши кувынтул ачеста есте кувынтул крединцей, пе каре-л проповэдуим ной.
Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira,
9 Дакэ мэртурисешть деч ку гура та пе Исус ка Домн ши дакэ крезь ын инима та кэ Думнезеу Л-а ынвият дин морць, вей фи мынтуит.
kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
10 Кэч прин крединца дин инимэ се капэтэ неприхэниря ши прин мэртурисиря ку гура се ажунӂе ла мынтуире,
Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa.
11 дупэ кум зиче Скриптура: „Орьчине креде ын Ел ну ва фи дат де рушине.”
Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.”
12 Ын адевэр, ну есте ничо деосебире ынтре иудеу ши грек, кэч тоць ау ачелашь Домн, каре есте богат ын ындураре пентру тоць чей че-Л кямэ.
Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye
13 Фииндкэ орьчине ва кема Нумеле Домнулуй ва фи мынтуит.
pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”
14 Дар кум вор кема пе Ачела ын каре н-ау крезут? Ши кум вор креде ын Ачела деспре каре н-ау аузит? Ши кум вор аузи деспре Ел фэрэ проповэдуитор?
Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo?
15 Ши кум вор проповэдуи, дакэ ну сунт тримишь? Дупэ кум есте скрис: „Кыт де фрумоасе сунт пичоареле челор че вестеск пачя, але челор че вестеск Евангелия!”
Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”
16 Дар ну тоць ау аскултат де Евангелие. Кэч Исая зиче: „Доамне, чине а крезут проповэдуиря ноастрэ?”
Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?”
17 Астфел, крединца вине ын урма аузирий, яр аузиря вине прин Кувынтул луй Христос.
Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu.
18 Дар еу ынтреб: „Н-ау аузит ей?” Ба да, кэч „гласул лор а рэсунат прин тот пэмынтул ши кувинтеле лор ау ажунс пынэ ла марӂиниле лумий”.
Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti, “Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi. Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”
19 Дар ынтреб ярэшь: „Н-а штиут Исраел лукрул ачеста?” Ба да, кэч Мойсе, чел динтый, зиче: „Вэ вой ынтэрыта ла пизмэ прин чея че ну есте ням, вэ вой ацыца мыния принтр-ун ням фэрэ причепере.”
Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti, “Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake. Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”
20 Ши Исая мерӂе ку ындрэзняла пынэ аколо кэ зиче: „Ам фост гэсит де чей че ну Мэ кэутау; М-ам фэкут куноскут челор че ну ынтребау де Мине.”
Ndipo Yesaya molimba mtima akuti, “Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna. Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”
21 Пе кынд, деспре Исраел зиче: „Тоатэ зиуа Мь-ам ынтинс мыниле спре ун нород рэзврэтит ши ымпотривитор ла ворбэ.”
Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti, “Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga kwa anthu osandimvera ndi okanika.”