< Апокалипса 13 >

1 Апой ам стат пе нисипул мэрий. Ши ам вэзут ридикынду-се дин маре о фярэ ку зече коарне ши шапте капете; пе коарне авя зече кунунь ымпэрэтешть ши пе капете авя нуме де хулэ.
Kenaka ndinaona chinjokacho chitayima mʼmbali mwa nyanja. Ndipo ndinaona chirombo chikutuluka mʼnyanja. Chinali ndi nyanga khumi ndi mitu isanu ndi iwiri. Pa nyanga iliyonse chinavala chipewa chaufumu, ndipo pa mutu uliwonse panali dzina lonyoza Mulungu.
2 Фяра пе каре ам вэзут-о семэна ку ун леопард, авя лабе ка де урс ши гурэ ка о гурэ де леу. Балаурул й-а дат путеря луй, скаунул луй де домние ши о стэпынире маре.
Chirombo chimene ndinachionacho chinali ngati kambuku, mapazi ake ngati chimbalangondo, kukamwa kwake ngati kwa mkango. Chinjoka chija chinapatsa chirombocho mphamvu zake, mpando wake waufumu ndiponso ulamuliro waukulu.
3 Унул дин капетеле ей пэря рэнит де моарте, дар рана де моарте фусесе виндекатэ. Ши тот пэмынтул се мира дупэ фярэ.
Umodzi wa mitu wa chirombocho unkaoneka ngati uli ndi bala losati nʼkupola, koma nʼkuti balalo litapola. Dziko lonse linadabwa ndipo linatsatira chirombocho.
4 Ши ау ынчепут сэ се ынкине балаурулуй, пентру кэ дэдусе путеря луй фярей. Ши ау ынчепут сэ се ынкине фярей, зикынд: „Чине се поате асемэна ку фяра ши чине се поате лупта ку еа?”
Anthu anapembedza chinjoka chija chifukwa chinapereka ulamuliro wake kwa chirombocho. Nachonso chirombo chija anachipembedza nʼkumafunsa kuti, “Ndani angafanane ndi chirombochi? Ndani angachite nacho nkhondo?”
5 И с-а дат о гурэ каре ростя ворбе марь ши хуле. Ши и с-а дат путере сэ лукрезе патрузечь ши доуэ де лунь.
Chirombo chija chinaloledwa kuyankhula mawu onyada ndi achipongwe kwa Mulungu. Chinapatsidwa mphamvu zolamulira pa miyezi 42.
6 Еа шь-а дескис гура ши а ынчепут сэ ростяскэ хуле ымпотрива луй Думнезеу, сэ-Й хуляскэ Нумеле, кортул ши пе чей че локуеск ын чер.
Ndipo chinayamba kuyankhula mawu achipongwe onyoza Mulungu, dzina lake, malo okhalamo ndi onse amene amakhala kumwamba.
7 И с-а дат сэ факэ рэзбой ку сфинций ши сэ-й бируе. Ши и с-а дат стэпынире песте орьче семинцие, песте орьче нород, песте орьче лимбэ ши песте орьче ням.
Chinaloledwa kuchita nkhondo ndi oyera mtima ndi kuwagonjetsa. Ndipo chinapatsidwanso mphamvu zolamulira anthu a fuko lililonse, mtundu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse.
8 Ши тоць локуиторий пэмынтулуй и се вор ынкина, тоць ачея ал кэрор нуме н-а фост скрис де ла ынтемееря лумий ын картя веций Мелулуй, каре а фост ынжунгият.
Anthu onse okhala pa dziko lapansi adzapembedza chirombocho, aliyense amene chilengedwere cha dziko lapansi dzina lake silinalembedwe mʼbuku la amoyo la Mwana Wankhosa anaphedwa uja.
9 Чине аре урекь, сэ аудэ!
Iye amene ali ndi makutu, amve.
10 Чине дуче пе алций ын робие ва мерӂе ши ел ын робие. Чине учиде ку сабия требуе сэ фие учис ку сабие. Аич есте рэбдаря ши крединца сфинцилор.
“Woyenera kupita ku ukapolo, adzapita ku ukapolo. Woyenera kufa ndi lupanga, adzafa ndi lupanga.” Pamenepa kwa anthu a Mulungu pakufunika kupirira ndi kukhulupirika.
11 Апой ам вэзут ридикынду-се дин пэмынт о алтэ фярэ, каре авя доуэ коарне ка але унуй мел ши ворбя ка ун балаур.
Kenaka ndinaona chirombo china chikutuluka mʼnthaka. Chinali ndi nyanga ziwiri ngati mwana wankhosa koma kuyankhula kwake ngati chinjoka.
12 Еа лукра ку тоатэ путеря фярей динтый ынаинтя ей ши фэчя ка пэмынтул ши локуиторий луй сэ се ынкине фярей динтый, а кэрей ранэ де моарте фусесе виндекатэ.
Chinalamulira ndi mphamvu zonse za chirombo choyamba chija, ndipo chinachititsa kuti dziko lapansi ndi anthu okhalamo alambire chirombo choyamba chija, chimene bala lake losati nʼkupola linali litapola.
13 Сэвыршя семне марь, пынэ аколо кэ фэчя кяр сэ се кобоаре фок дин чер пе пэмынт, ын фаца оаменилор.
Ndipo chinachita zizindikiro zazikulu zodabwitsa, mpaka kumagwetsa moto pa dziko lapansi kuchokera kumwamba anthu akuona.
14 Ши амэӂя пе локуиторий пэмынтулуй прин семнеле пе каре и се дэдусе сэ ле факэ ын фаца фярей. Еа а зис локуиторилор пэмынтулуй сэ факэ о икоанэ фярей, каре авя рана де сабие ши трэя.
Chifukwa cha zizindikiro zimene chinaloledwa kuchita mʼmalo mwa chirombo choyamba chija, chimene bala lake linapola, chinanyenga anthu okhala pa dziko lapansi. Chinalamula anthu kuti apange fano mopereka ulemu kwa chirombo chimene chinavulazidwa ndi lupanga, koma nʼkukhalabe ndi moyo.
15 И с-а дат путере сэ дя суфларе икоаней фярей, ка икоана фярей сэ ворбяскэ ши сэ факэ сэ фие оморыць тоць чей че ну се вор ынкина икоаней фярей.
Chirombo cha chiwirichi chinapatsidwa mphamvu zakupereka mpweya kwa fano la chirombo choyamba chija kuti liyankhule ndi kuphetsa aliyense wokana kupembedza fanolo.
16 Ши а фэкут ка тоць: мичь ши марь, богаць ши сэрачь, слобозь ши робь, сэ примяскэ ун семн пе мына дряптэ сау пе фрунте
Chinakakamiza aliyense, wamngʼono, wamkulu, wolemera, wosauka, mfulu ndi kapolo kuti alembedwe chizindikiro pa dzanja lamanja kapena pa mphumi.
17 ши нимень сэ ну поатэ кумпэра сау винде фэрэ сэ айбэ семнул ачеста, адикэ нумеле фярей, сау нумэрул нумелуй ей.
Chinkachita zimenezi kuti wina aliyense asaloledwe kugula kapena kugulitsa kanthu ngati alibe chizindikiro chimenechi, chimene ndi dzina la chirombocho kapena nambala yotanthauza dzina lake.
18 Аич е ынцелепчуня. Чине аре причепере, сэ сокотяскэ нумэрул фярей. Кэч есте ун нумэр де ом. Ши нумэрул ей есте шасе суте шайзечь ши шасе.
Pano pafunika nzeru. Munthu amene ali ndi nzeru atanthauze nambala ya chirombocho, pakuti nambalayo ikutanthauza munthu. Nambala yake ndi 666.

< Апокалипса 13 >