< Псалмул 74 >
1 Пентру че, Думнезеуле, не лепезь пентру тотдяуна? Пентру че Те мыний пе турма пэшуний Тале?
Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Аду-Ць аминте де попорул Тэу пе каре л-ай кыштигат одиниоарэ, пе каре л-ай рэскумпэрат ка семинцие а моштенирий Тале! Аду-Ць аминте де мунтеле Сионулуй, унде Ыць авяй локуинца;
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 ындряптэ-Ць паший спре ачесте локурь пустиите фэрэ курмаре! Врэжмашул а пустиит тотул ын Локашул Тэу чел Сфынт.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Потривничий Тэй ау муӂит ын мижлокул Темплулуй Тэу; шь-ау пус семнеле лор дрепт семне.
Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 Паркэ ерау ниште оамень каре ридикэ топорул ынтр-о пэдуре дясэ:
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 ын курынд, ау сфэрымат тоате подоабеле сэпате, ку ловитурь де секурь ши чокане.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
7 Ау пус фок Сфынтулуй Тэу Локаш; ау дэрымат ши ау пынгэрит локуинца Нумелуй Тэу.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 Ей зичяу ын инима лор: „Сэ-й прэпэдим пе тоць!” Ау арс тоате локуриле сфинте дин царэ.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 Семнеле ноастре ну ле май ведем; ну май есте ничун пророк ши ну май есте нимень принтре ной каре сэ штие пынэ кынд…
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 Пынэ кынд, Думнезеуле, ва батжокори асуприторул ши ва несокоти врэжмашул фэрэ курмаре Нумеле Тэу?
Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Пентру че Ыць траӂь ынапой мына ши дряпта Та? Скоате-о дин сын ши нимичеште-й!
Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 Тотушь Думнезеу есте Ымпэратул меу, каре дин времурь стрэвекь дэ избэвирь ын мижлокул ачестей цэрь.
Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Ту ай деспэрцит маря ку путеря Та, ай сфэрымат капетеле балаурилор дин апе;
Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 ай здробит капул левиатанулуй, л-ай дат сэ-л мэнынче фяреле дин пустиу.
Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Ай фэкут сэ цышняскэ извоаре ын пырае, ай ускат рыурь каре ну сякэ.
Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 А Та есте зиуа, а Та есте ши ноаптя; Ту ай ашезат лумина ши соареле.
Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Ту ай статорничит тоате хотареле пэмынтулуй, Ту ай рындуит вара ши ярна.
Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Аду-Ць аминте, Доамне, кэ врэжмашул Те батжокореште ши ун попор некибзуит хулеште Нумеле Тэу!
Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Ну лэса прадэ фярелор суфлетул туртурелей Тале ши ну уйта пе вечие вяца ненорочицилор Тэй!
Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Ай ын ведере легэмынтул! Кэч локуриле досниче дин царэ сунт плине де бырлогурь де тылхарь.
Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Сэ ну се ынтоаркэ рушинат чел апэсат, чи ненорочитул ши сэракул сэ лауде Нумеле Тэу!
Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Скоалэ-Те, Думнезеуле, апэрэ-Ць причина! Аду-Ць аминте де окэриле пе каре Ци ле арункэ ын фиекаре зи чел фэрэ минте!
Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Ну уйта стригэтеле потривничилор Тэй, зарва каре креште некурмат а челор че се ридикэ ымпотрива Та!
Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.