< Псалмул 72 >
1 Думнезеуле, дэ жудекэциле Тале ымпэратулуй ши дэ дрептатя Та фиулуй ымпэратулуй!
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 Ши ел ва жудека пе попорул Тэу ку дрептате ши пе ненорочиций Тэй ку непэртинире.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Мунций вор адуче паче попорулуй ши дялуриле, де асеменя, ка урмаре а дрептэций Тале.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 Ел ва фаче дрептате ненорочицилор попорулуй, ва скэпа пе копиий сэракулуй ши ва здроби пе асупритор.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 Аша кэ се вор теме де Тине кыт ва фи соареле ши кыт се ва арэта луна, дин ням ын ням;
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 ва фи ка о плоае каре каде пе ун пэмынт косит, ка о плоае репеде каре удэ кымпия.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 Ын зилеле луй ва ынфлори чел неприхэнит ши ва фи белшуг де паче пынэ ну ва май фи лунэ.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 Ел ва стэпыни де ла о маре ла алта ши де ла рыу пынэ ла марӂиниле пэмынтулуй.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Локуиторий пустиулуй ышь вор плека ӂенункюл ынаинтя луй ши врэжмаший вор линӂе цэрына.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Ымпэраций Тарсисулуй ши ай остроавелор вор плэти бирурь, ымпэраций Себей ши Сабей вор адуче дарурь.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Да, тоць ымпэраций се вор ынкина ынаинтя луй, тоате нямуриле ый вор служи.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 Кэч ел ва избэви пе сэракул каре стригэ ши пе ненорочитул каре н-аре ажутор.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Ва авя милэ де чел ненорочит ши де чел липсит ши ва скэпа вяца сэрачилор;
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 ый ва избэви де апэсаре ши де силэ ши сынӂеле лор ва фи скумп ынаинтя луй.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 Ей вор трэи ши-й вор да аур дин Себа; се вор руга неынчетат пентру ел ши-л вор бинекувынта ын фиекаре зи.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Ва фи белшуг де грыу ын царэ пынэ ын вырфул мунцилор ши спичеле лор се вор клэтина ка ши копачий дин Либан; оамений вор ынфлори ын четэць ка ярба пэмынтулуй.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Нумеле луй ва дэйнуи пе вечие: кыт соареле ый ва цине нумеле. Ку ел се вор бинекувынта уний пе алций, ши тоате нямуриле ыл вор нуми феричит.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Бинекувынтат сэ фие Домнул Думнезеул луй Исраел, сингурул каре фаче минунь!
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 Бинекувынтат сэ фие ын вечь слэвитул Луй Нуме! Тот пэмынтул сэ се умпле де слава Луй! Амин! Амин!
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 Сфыршитул ругэчунилор луй Давид, фиул луй Исай.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.