< Псалмул 49 >

1 Аскултаць лукрул ачеста, тоате попоареле, луаць аминте, тоць локуиторий лумий:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 мичь ши марь, богаць ши сэрачь!
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 Гура мя ва ворби кувинте ынцелепте ши инима мя аре гындурь плине де жудекатэ.
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 Еу ымь плек урекя ла пилделе каре ымь сунт инсуфлате, ымь ынчеп кынтаря ын сунетул харпей.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Пентру че сэ мэ тем ын зилеле ненорочирий, кынд мэ ынконжоарэ нелеӂюиря потривничилор мей?
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 Ей се ынкред ын авуцииле лор ши се фэлеск ку богэция лор чя маре.
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 Дар ну пот сэ се рэскумпере унул пе алтул, нич сэ дя луй Думнезеу прецул рэскумпэрэрий.
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 Рэскумпэраря суфлетулуй лор есте аша де скумпэ, кэ ну се ва фаче ничодатэ.
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 Ну вор трэи пе вечие, ну пот сэ ну вадэ мормынтул.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 Да, ыл вор ведя: кэч ынцелепций мор, небунул ши простул деопотривэ пер ши ласэ алтора авуцииле лор.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Ей ышь ынкипуе кэ вешниче ле вор фи каселе, кэ локуинцеле лор вор дэйнуи дин вяк ын вяк, ей, каре дау нумеле лор ла цэрь ынтреӂь.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 Дар омул пус ын чинсте ну дэйнуеште, чи есте ка добитоачеле каре се тае.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 Ятэ че соартэ ау ей, чей плинь де атыта ынкредере, прекум ши чей че ый урмязэ, кэрора ле плак кувинтеле лор.
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Сунт душь ка о турмэ ын Локуинца морцилор, ый паште моартя ши, ын курынд, оамений фэрэ приханэ ый калкэ ын пичоаре: ли се дуче фрумусеця ши Локуинца морцилор ле есте локашул. (Sheol h7585)
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
15 Дар мие Думнезеу ымь ва скэпа суфлетул дин Локуинца морцилор, кэч мэ ва луа суб окротиря Луй. (Sheol h7585)
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
16 Ну те теме кынд се ымбогэцеште чинева ши кынд и се ынмулцеск вистиерииле касей,
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 кэч ну я нимик ку ел кынд моаре: вистиерииле луй ну се кобоарэ дупэ ел.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Сэ се тот крядэ омул феричит ын вяцэ, сэ се тот лауде ку букурииле пе каре ши ле фаче,
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 кэч тот ын локуинца пэринцилор сэй ва мерӂе ши ну ва май ведя лумина ничодатэ.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 Омул пус ын чинсте ши фэрэ причепере есте ка добитоачеле пе каре ле тай.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< Псалмул 49 >