< Псалмул 32 >

1 Фериче де чел ку фэрэделеӂя ертатэ ши де чел ку пэкатул акоперит!
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Фериче де омул кэруя ну-й цине ын сямэ Домнул нелеӂюиря ши ын духул кэруя ну есте викление!
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Кытэ време ам тэкут, ми се топяу оаселе де ӂеметеле меле некурмате,
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 кэч зи ши ноапте мына Та апэса асупра мя; ми се уска влага кум се усукэ пэмынтул де сечета верий.
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Атунч Ць-ам мэртурисит пэкатул меу ши ну мь-ам аскунс фэрэделеӂя. Ам зис: „Ымь вой мэртуриси Домнулуй фэрэделеӂиле!” Ши Ту ай ертат вина пэкатулуй меу.
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 Де ачея орьче ом евлавиос сэ се роаӂе Цие ла време потривитэ! Ши кяр де с-ар вэрса апе марь, пе ел ну-л вор атинӂе делок.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Ту ешть окротиря мя, Ту мэ скоць дин неказ, Ту мэ ынконжорь ку кынтэрь де избэвире.
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 „Еу, зиче Домнул, те вой ынвэца ши-ць вой арэта каля пе каре требуе с-о урмезь, те вой сфэтуи ши вой авя привиря ындрептатэ асупра та.”
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Ну фиць ка ун кал сау ка ун катыр фэрэ причепере, пе каре-л струнешть ку ун фрыу ши о зэбалэ ку каре-л леӂь ка сэ ну се апропие де тине!
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Де мулте дурерь аре парте чел рэу, дар чел че се ынкреде ын Домнул есте ынконжурат ку ындураря Луй.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Неприхэницилор, букураци-вэ ын Домнул ши веселици-вэ! Скоатець стригэте де букурие, тоць чей ку инима фэрэ приханэ!
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Псалмул 32 >