< Псалмул 20 >

1 Сэ те аскулте Домнул ын зиуа неказулуй, сэ те окротяскэ Нумеле Думнезеулуй луй Иаков,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 сэ-ць тримитэ ажутор дин локашул Сэу чел Сфынт ши сэ те сприжине дин Сион!
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Сэ-Шь адукэ аминте де тоате даруриле тале де мынкаре ши сэ-ць примяскэ ардериле-де-тот!
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Сэ-ць дя че-ць дореште инима ши сэ-ць ымплиняскэ тоате плануриле тале!
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Атунч ной не вом букура де бируинца та ши вом флутура стягул ын Нумеле Думнезеулуй ностру. Домнул сэ-ць аскулте тоате доринцеле тале!
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Штиу де акум кэ Домнул скапэ пе унсул Сэу ши-й ва рэспунде дин черурь, дин Локашул Луй чел Сфынт, прин ажуторул атотпутерник ал дрептей Луй.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Уний се бизуе пе кареле лор, алций, пе каий лор, дар ной не бизуим пе Нумеле Домнулуй Думнезеулуй ностру.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Ей се ындоае ши кад, дар ной не ридикэм ши рэмынем ын пичоаре.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Скапэ, Доамне, пе ымпэратул ши аскултэ-не кынд Те кемэм!
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Псалмул 20 >