< Псалмул 119 >

1 Фериче де чей фэрэ приханэ ын каля лор, каре умблэ ынтотдяуна дупэ Леӂя Домнулуй!
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Фериче де чей че пэзеск порунчиле Луй, каре-Л каутэ дин тоатэ инима лор,
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 каре ну сэвыршеск ничо нелеӂюире ши умблэ ын кэиле Луй!
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Ту ай дат порунчиле Тале ка сэ фие пэзите ку сфинцение.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 О, де ар цинти кэиле меле ла пэзиря орындуирилор Тале!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Атунч ну вой роши де рушине ла ведеря тутурор порунчилор Тале!
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Те вой лэуда ку инимэ неприхэнитэ кынд вой ынвэца леӂиле дрептэций Тале.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Вряу сэ пэзеск орындуириле Тале: ну мэ пэрэси де тот!
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Кум ышь ва цине тынэрул куратэ кэраря? Ындрептынду-се дупэ Кувынтул Тэу.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Те каут дин тоатэ инима мя; ну мэ лэса сэ мэ абат де ла порунчиле Тале.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Стрынг Кувынтул Тэу ын инима мя, ка сэ ну пэкэтуеск ымпотрива Та!
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Бинекувынтат сэ фий Ту, Доамне! Ынвацэ-мэ орындуириле Тале!
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Ку бузеле меле вестеск тоате хотэрыриле гурий Тале.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Кынд урмез ынвэцэтуриле Тале, мэ букур де парк-аш авя тоате комориле.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Мэ гындеск адынк ла порунчиле Тале ши кэрэриле Тале ле ам суб окь.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Мэ десфэтез ын орындуириле Тале ши ну уйт Кувынтул Тэу.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Фэ бине робулуй Тэу, ка сэ трэеск ши сэ пэзеск Кувынтул Тэу!
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Дескиде-мь окий, ка сэ вэд лукруриле минунате але Леӂий Тале!
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Сунт ун стрэин пе пэмынт: ну-мь аскунде порунчиле Тале!
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Тотдяуна ми се топеште суфлетул де дор дупэ Леӂиле Тале.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Ту мустри пе чей ынгымфаць, пе блестемаций ачештя каре се рэтэческ де ла порунчиле Тале.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Ридикэ де пе мине окара ши диспрецул, кэч пэзеск ынвэцэтуриле Тале!
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Сэ тот стя воевозий ши сэ ворбяскэ ымпотрива мя: робул Тэу куӂетэ адынк ла орындуириле Тале.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Ынвэцэтуриле Тале сунт десфэтаря мя ши сфэтуиторий мей.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Суфлетул меу есте липит де цэрынэ: ынвиорязэ-мэ дупэ фэгэдуинца Та!
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Еу ымь историсеск кэиле ши Ту мэ аскулць: ынвацэ-мэ орындуириле Тале!
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Фэ-мэ сэ причеп каля порунчилор Тале ши вой куӂета ла лукруриле Тале челе минунате!
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Ымь плынӂе суфлетул де дурере: ридикэ-мэ, дупэ Кувынтул Тэу!
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Депэртязэ-мэ де каля некрединчошией кэтре Тине ши дэ-мь ындураря Та, ка сэ урмез Леӂя Та!
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Алег каля адевэрулуй, пун леӂиле Тале суб окий мей.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Мэ цин де ынвэцэтуриле Тале, Доамне, ну мэ лэса де рушине!
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Алерг пе каля порунчилор Тале, кэч ымь скоць инима ла ларг.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Ынвацэ-мэ, Доамне, каля орындуирилор Тале, ка с-о цин пынэ ла сфыршит!
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Дэ-мь причепере, ка сэ пэзеск Леӂя Та ши с-о цин дин тоатэ инима мя!
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Повэцуеште-мэ пе кэраря порунчилор Тале, кэч ымь плаче де еа!
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Плякэ-мь инима спре ынвэцэтуриле Тале, ши ну спре кыштиг!
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Абате-мь окий де ла ведеря лукрурилор дешарте, ынвиорязэ-мэ ын каля Та!
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Ымплинеште-Ць фэгэдуинца фацэ де робул Тэу, фэгэдуинца фэкутэ пентру чей че се тем де Тине!
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Депэртязэ де ла мине окара де каре мэ тем! Кэч жудекэциле Тале сунт плине де бунэтате.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Ятэ, дореск сэ ымплинеск порунчиле Тале: фэ-мэ сэ трэеск ын неприхэниря черутэ де Тине!
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Сэ винэ, Доамне, ындураря Та песте мине, мынтуиря Та, дупэ фэгэдуинца Та!
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Ши атунч вой путя рэспунде челуй че мэ батжокореште, кэч мэ ынкред ын Кувынтул Тэу.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Ну луа де тот дин гура мя кувынтул адевэрулуй! Кэч нэдэждуеск ын жудекэциле Тале.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Вой пэзи Леӂя Та некурмат, тотдяуна ши пе вечие.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Вой умбла ын лок ларг, кэч каут порунчиле Тале.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Вой ворби деспре ынвэцэтуриле Тале ынаинтя ымпэрацилор ши ну-мь ва роши образул.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Мэ десфэтез ын порунчиле Тале, кэч ле юбеск.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Ымь ынтинд мыниле спре порунчиле Тале, пе каре ле юбеск, ши вряу сэ мэ гындеск адынк ла орындуириле Тале.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Аду-Ць аминте де фэгэдуинца датэ робулуй Тэу, ын каре м-ай фэкут сэ-мь пун нэдеждя!
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Ачаста есте мынгыеря мя ын неказул меу: кэ фэгэдуинца Та ымь дэ ярэшь вяцэ.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Ниште ынгымфаць мь-арункэ батжокурь, тотушь еу ну мэ абат де ла Леӂя Та.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Мэ гындеск ла жудекэциле Тале де одиниоарэ, Доамне, ши мэ мынгый.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 М-апукэ о мыние апринсэ ла ведеря челор рэй, каре пэрэсеск Леӂя Та.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Орындуириле Тале сунт прилежул кынтэрилор меле ын каса прибеӂией меле.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Ноаптя ымь адук аминте де Нумеле Тэу, Доамне, ши пэзеск Леӂя Та.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Аша ми се кувине, кэч пэзеск порунчиле Тале.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Партя мя, Доамне, о спун, есте сэ пэзеск кувинтеле Тале.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Те рог дин тоатэ инима мя: ай милэ де мине, дупэ фэгэдуинца Та!
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Мэ гындеск ла кэиле меле ши ымь ындрепт пичоареле спре ынвэцэтуриле Тале.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Мэ грэбеск ши ну преӂет сэ пэзеск порунчиле Тале.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Курселе челор рэй мэ ынконжоарэ, дар ну уйт Леӂя Та.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Мэ скол ла мезул нопций сэ Те лауд пентру жудекэциле Тале челе дрепте.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Сунт приетен ку тоць чей че се тем де Тине ши ку чей че пэзеск порунчиле Тале.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Пэмынтул, Доамне, есте плин де бунэтатя Та; ынвацэ-мэ орындуириле Тале!
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Ту фачь бине робулуй Тэу, Доамне, дупэ фэгэдуинца Та.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Ынвацэ-мэ сэ ам ынцелеӂере ши причепере, кэч кред ын порунчиле Тале!
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Пынэ че ам фост смерит, рэтэчям; дар акум пэзеск Кувынтул Тэу.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Ту ешть бун ши бинефэкэтор: ынвацэ-мэ орындуириле Тале!
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Ниште ынгымфаць урзеск неадевэрурь ымпотрива мя; дар еу пэзеск дин тоатэ инима мя порунчиле Тале.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Инима лор есте несимцитоаре ка грэсимя, дар еу мэ десфэтез ын Леӂя Та.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Есте спре бинеле меу кэ м-ай смерит, ка сэ ынвэц орындуириле Тале.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Май мулт прецуеште пентру мине леӂя гурий Тале декыт о мие де лукрурь де аур ши де арӂинт.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Мыниле Тале м-ау фэкут ши м-ау ынтокмит; дэ-мь причепере, ка сэ ынвэц порунчиле Тале!
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Чей че се тем де Тине мэ вэд ши се букурэ, кэч нэдэждуеск ын фэгэдуинцеле Тале.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Штиу, Доамне, кэ жудекэциле Тале сунт дрепте: дин крединчошие м-ай смерит.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Фэ ка бунэтатя Та сэ-мь фие мынгыере, кум ай фэгэдуит робулуй Тэу!
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Сэ винэ песте мине ындурэриле Тале, ка сэ трэеск, кэч Леӂя Та есте десфэтаря мя.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Сэ фие ынфрунтаць ынгымфаций каре мэ асупреск фэрэ темей! Кэч еу мэ гындеск адынк ла порунчиле Тале.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Сэ се ынтоаркэ ла мине чей че се тем де Тине ши чей че куноск ынвэцэтуриле Тале!
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Инима сэ-мь фие неымпэрцитэ ын орындуириле Тале, ка сэ ну фиу дат де рушине!
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Ымь тынжеште суфлетул дупэ мынтуиря Та: нэдэждуеск ын фэгэдуинца Та.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Ми се топеск окий дупэ фэгэдуинца Та ши зик: „Кынд мэ вей мынгыя?”
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Кэч ам ажунс ка ун бурдуф пус ын фум, тотушь ну уйт орындуириле Тале.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Каре есте нумэрул зилелор робулуй Тэу? Кынд вей педепси пе чей че мэ пригонеск?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Ниште ынгымфаць сапэ гропь ынаинтя мя; ну лукрязэ дупэ Леӂя Та.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Тоате порунчиле Тале ну сунт декыт крединчошие; ей мэ пригонеск фэрэ темей: ажутэ-мэ!
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Гата, гата сэ мэ добоаре ши сэ мэ прэпэдяскэ, дар еу ну пэрэсеск порунчиле Тале.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Ынвиорязэ-мэ дупэ бунэтатя Та, ка сэ пэзеск ынвэцэтуриле гурий Тале!
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Кувынтул Тэу, Доамне, дэйнуеште ын вечь ын черурь.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Крединчошия Та цине дин ням ын ням; Ту ай ынтемеят пэмынтул, ши ел рэмыне таре.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Дупэ леӂиле Тале стэ ын пичоаре тотул астэзь, кэч тоате лукруриле Ыць сунт супусе.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Дакэ н-ар фи фост Леӂя Та десфэтаря мя, аш фи перит ын тикэлошия мя.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Ничодатэ ну вой уйта порунчиле Тале, кэч прин еле мэ ынвиорезь.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Ал Тэу сунт: мынтуеште-мэ, кэч каут порунчиле Тале!
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Ниште рэй мэ аштяптэ ка сэ мэ пярдэ, дар еу яу аминте ла ынвэцэтуриле Тале.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Вэд кэ тот че есте десэвыршит аре марӂинь, порунчиле Тале ынсэ сунт фэрэ марӂинь.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Кыт де мулт юбеск Леӂя Та! Тоатэ зиуа мэ гындеск ла еа.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Порунчиле Тале мэ фак май ынцелепт декыт врэжмаший мей, кэч тотдяуна ле ам ку мине.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Сунт май ынвэцат декыт тоць ынвэцэторий мей, кэч мэ гындеск ла ынвэцэтуриле Тале.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Ам май мултэ причепере декыт бэтрыний, кэч пэзеск порунчиле Тале.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Ымь цин пичорул департе де орьче друм рэу, ка сэ пэзеск Кувынтул Тэу.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Ну мэ депэртез де леӂиле Тале, кэч Ту мэ ынвець.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Че дулчь сунт кувинтеле Тале пентру черул гурий меле! Май дулчь декыт мьеря ын гура мя!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Прин порунчиле Тале мэ фак май причепут, де ачея урэск орьче кале а минчуний.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Кувынтул Тэу есте о канделэ пентру пичоареле меле ши о луминэ пе кэраря мя.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Жур, ши мэ вой цине де журэмынт, кэ вой пэзи леӂиле Тале челе дрепте.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Сунт фоарте амэрыт: ынвиорязэ-мэ, Доамне, дупэ Кувынтул Тэу!
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Примеште, Доамне, симцэминтеле пе каре ле спуне гура мя ши ынвацэ-мэ леӂиле Тале!
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Вяца ымь есте некурмат ын примеждие, ши тотушь ну уйт Леӂя Та.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Ниште рэй ымь ынтинд курсе, дар еу ну мэ рэтэческ де ла порунчиле Тале.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Ынвэцэтуриле Тале сунт моштениря мя де вечь, кэч еле сунт букурия инимий меле.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Ымь плек инима сэ ымплинеск орындуириле Тале, тотдяуна ши пынэ ла сфыршит.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Урэск пе оамений нехотэрыць, дар юбеск Леӂя Та.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Ту ешть адэпостул ши скутул меу; еу нэдэждуеск ын фэгэдуинца Та.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Депэртаци-вэ де мине, рэилор, ка сэ пэзеск порунчиле Думнезеулуй меу!
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Сприжинэ-мэ, дупэ фэгэдуинца Та, ка сэ трэеск ши ну мэ лэса де рушине ын нэдеждя мя!
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Фий сприжинул меу, ка сэ фиу скэпат ши сэ мэ веселеск неынчетат де орындуириле Тале!
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Ту диспрецуешть пе тоць чей че се депэртязэ де орындуириле Тале, кэч ыншелэтория лор есте задарникэ.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Ка спума ей пе тоць чей рэй де пе пэмынт, де ачея еу юбеск ынвэцэтуриле Тале.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Ми се ынфиоарэ карня де фрика Та ши мэ тем де жудекэциле Тале.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Пэзеск леӂя ши дрептатя: ну мэ лэса ын воя асуприторилор мей!
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Я суб окротиря Та бинеле робулуй Тэу ши ну мэ лэса апэсат де ниште ынгымфаць!
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Ми се топеск окий дупэ мынтуиря Та ши дупэ фэгэдуинца Та чя дряптэ.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Поартэ-Те ку робул Тэу дупэ бунэтатя Та ши ынвацэ-мэ орындуириле Тале!
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Еу сунт робул Тэу; дэ-мь причепере, ка сэ куноск ынвэцэтуриле Тале!
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Есте время ка Домнул сэ лукрезе, кэч ей калкэ Леӂя Та.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Де ачея, еу юбеск порунчиле Тале май мулт декыт аурул, да, май мулт декыт аурул курат.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Де ачея, гэсеск дрепте тоате порунчиле Тале ши урэск орьче кале а минчуний.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Ынвэцэтуриле Тале сунт минунате, де ачея ле пэзеште суфлетул меу.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Дескопериря кувинтелор Тале дэ луминэ, дэ причепере челор фэрэ рэутате.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Дескид гура ши офтез, кэч сунт лаком дупэ порунчиле Тале.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Ынтоарче-Ць Фаца спре мине ши ай милэ де мине, дупэ обичеюл Тэу фацэ де чей че юбеск Нумеле Тэу!
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Ынтэреште-мь паший ын Кувынтул Тэу ши ну лэса ничо нелеӂюире сэ стэпыняскэ песте мине!
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Избэвеште-мэ де асуприря оаменилор, ка сэ пэзеск порунчиле Тале!
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Фэ сэ стрэлучяскэ Фаца Та песте робул Тэу ши ынвацэ-мэ орындуириле Тале!
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Окий ымь варсэ широае де апе, пентру кэ Леӂя Та ну есте пэзитэ.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Ту ешть дрепт, Доамне, ши жудекэциле Тале сунт фэрэ приханэ.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Ту Ыць ынтемеезь ынвэцэтуриле пе дрептате ши пе чя май маре крединчошие.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Рывна мя мэ мэнынкэ, пентру кэ потривничий мей уйтэ кувинтеле Тале.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Кувынтул Тэу есте ку тотул ынчеркат, ши робул Тэу ыл юбеште.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Сунт мик ши диспрецуит, дар ну уйт порунчиле Тале.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Дрептатя Та есте о дрептате вешникэ ши Леӂя Та есте адевэрул.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Неказул ши стрымтораря мэ ажунг, дар порунчиле Тале сунт десфэтаря мя.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Ынвэцэтуриле Тале сунт дрепте пе вечие: дэ-мь причепере, ка сэ трэеск!
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Те кем дин тоатэ инима мя: аскултэ-мэ, Доамне, ка сэ пэзеск орындуириле Тале!
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Те кем: мынтуеште-мэ, ка сэ пэзеск ынвэцэтуриле Тале!
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 О яу ынаинтя зорилор ши стриг; нэдэждуеск ын фэгэдуинцеле Тале.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 О яу ынаинтя стрэжилор де ноапте ши дескид окий, ка сэ мэ гындеск адынк ла Кувынтул Тэу.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Аскултэ-мь гласул, дупэ бунэтатя Та, ынвиорязэ-мэ, Доамне, дупэ жудеката Та!
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Се апропие чей че урмэреск мишелия ши се депэртязэ де Леӂя Та.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Дар Ту ешть апроапе, Доамне, ши тоате порунчиле Тале сунт адевэрул.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Де мултэ време штиу, дин ынвэцэтуриле Тале, кэ ле-ай ашезат пентру тотдяуна.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Вези-мь тикэлошия ши избэвеште-мэ, кэч ну уйт Леӂя Та!
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Апэрэ-мь причина ши рэскумпэрэ-мэ, ынвиорязэ-мэ, дупэ фэгэдуинца Та!
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Мынтуиря есте департе де чей рэй, кэч ей ну каутэ орындуириле Тале.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Марь сунт ындурэриле Тале, Доамне! Ынвиорязэ-мэ дупэ жудекэциле Тале!
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Мулць сунт пригониторий ши потривничий мей, дар ну мэ депэртез де ынвэцэтуриле Тале.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Вэд ку скырбэ пе чей некрединчошь Цие, каре ну пэзеск Кувынтул Тэу.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Везь кыт де мулт юбеск еу порунчиле Тале: ынвиорязэ-мэ, Доамне, дупэ бунэтатя Та!
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Темелия Кувынтулуй Тэу есте адевэрул ши тоате леӂиле Тале челе дрепте сунт вешниче.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Ниште воевозь мэ пригонеск фэрэ темей, дар инима мя ну тремурэ декыт де кувинтеле Тале.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Мэ букур де Кувынтул Тэу ка чел че гэсеште о маре прадэ.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Урэск ши ну пот суфери минчуна, дар юбеск Леӂя Та.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Де шапте орь пе зи Те лауд дин причина леӂилор Тале челор дрепте.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Мултэ паче ау чей че юбеск Леӂя Та ши ну ли се ынтымплэ ничо ненорочире.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Еу нэдэждуеск ын мынтуиря Та, Доамне, ши ымплинеск порунчиле Тале.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Суфлетул меу цине ынвэцэтуриле Тале ши ле юбеск мулт де тот!
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Пэзеск порунчиле ши ынвэцэтуриле Тале, кэч тоате кэиле меле сунт ынаинтя Та.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Сэ ажунгэ стригэтул меу пынэ ла Тине, Доамне! Дэ-мь причепере, дупэ фэгэдуинца Та!
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Сэ ажунгэ череря мя пынэ ла Тине! Избэвеште-мэ, дупэ фэгэдуинца Та!
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Бузеле меле сэ вестяскэ лауда Та, кэч Ту мэ ынвець орындуириле Тале!
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Сэ кынте лимба мя Кувынтул Тэу, кэч тоате порунчиле Тале сунт дрепте!
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Мына Та сэ-мь фие ынтр-ажутор, кэч ам алес порунчиле Тале!
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Суспин дупэ мынтуиря Та, Доамне, ши Леӂя Та есте десфэтаря мя.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Сэ-мь трэяскэ суфлетул ши сэ Те лауде, ши жудекэциле Тале сэ мэ сприжине!
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Рэтэческ ка о оае пердутэ: каутэ пе робул Тэу, кэч ну уйт порунчиле Тале!
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Псалмул 119 >