< Псалмул 102 >
1 Доамне, аскултэ-мь ругэчуня ши с-ажунгэ стригэтул меу пынэ ла Тине!
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Ну-мь аскунде Фаца Та ын зиуа неказулуй меу! Плякэ-Ць урекя спре мине кынд стриг! Аскултэ-мэ деграбэ!
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Кэч зилеле меле пер ка фумул ши оаселе ымь ард ка ун тэчуне.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Инима ымь есте ловитэ ши ми се усукэ ынтокмай ка ярба; пынэ ши пыня уйт сэ мь-о мэнынк.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Аша де марь ымь сунт ӂеметеле, кэ ми се липеск оаселе де карне.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Семэн ку пеликанул дин пустиу, сунт ка о кукувя дин дэрымэтурь;
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 ну май пот дорми ши сунт ка пасэря сингуратикэ пе ун акопериш.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Ын фиекаре зи мэ батжокореск врэжмаший мей ши потривничий мей журэ пе мине ын мыния лор.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Мэнынк цэрынэ ын лок де пыне ши ымь аместек лакримиле ку бэутура
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 дин причина мынией ши урӂией Тале, кэч Ту м-ай ридикат ши м-ай арункат департе.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Зилеле меле сунт ка о умбрэ гата сэ трякэ ши мэ усук ка ярба.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Дар Ту, Доамне, Ту ымпэрэцешть пе вечие ши помениря Та цине дин ням ын ням.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Ту Те вей скула ши вей авя милэ де Сион; кэч есте время сэ те ындурь де ел, а венит время хотэрытэ пентру ел.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Кэч робий Тэй юбеск петреле Сионулуй ши ле е милэ де цэрына луй.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Атунч се вор теме нямуриле де Нумеле Домнулуй ши тоць ымпэраций пэмынтулуй де слава Та.
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Да, Домнул ва зиди ярэшь Сионул ши Се ва арэта ын слава Са.
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Ел я аминте ла ругэчуня невояшулуй ши ну-й несокотеште ругэчуня.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Сэ се скрие лукрул ачеста пентру нямул де оамень каре ва вени, ши попорул каре се ва наште сэ лауде пе Домнул!
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 Кэч Ел привеште дин ынэлцимя сфинценией Луй; Домнул привеште дин черурь пе пэмынт,
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 ка сэ аудэ ӂеметеле приншилор де рэзбой ши сэ избэвяскэ пе чей че сунт пе моарте;
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 пентру ка ей сэ вестяскэ ын Сион Нумеле Домнулуй ши лауделе Луй ын Иерусалим,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 кынд се вор стрынӂе тоате попоареле ши тоате ымпэрэцииле ка сэ служяскэ Домнулуй.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Ел мь-а фрынт путеря ын друм ши мь-а скуртат зилеле.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Еу зик: „Думнезеуле, ну мэ луа ла жумэтатя зилелор меле, Ту, ай кэруй ань цин вешник!”
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Ту ай ынтемеят ын векиме пэмынтул ши черуриле сунт лукраря мынилор Тале.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Еле вор пери, дар Ту вей рэмыне; тоате се вор ынвеки ка о хайнэ; ле вей скимба ка пе ун вешмынт ши се вор скимба.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Дар Ту рэмый Ачелашь ши аний Тэй ну се вор сфырши.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Фиий робилор Тэй ышь вор локуи цара ши сэмынца лор ва рэмыне ынаинтя Та.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”