< Провербеле 3 >

1 Фиуле, ну уйта ынвэцэтуриле меле ши пэстрязэ ын инима та сфатуриле меле!
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Кэч еле ыць вор лунӂи зилеле ши аний веций тале ши-ць вор адуче мултэ паче.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Сэ ну те пэрэсяскэ бунэтатя ши крединчошия: лягэ-ци-ле ла гыт, скрие-ле пе тэблица инимий тале!
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Ши, астфел, вей кэпэта тречере ши минте сэнэтоасэ ынаинтя луй Думнезеу ши ынаинтя оаменилор.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Ынкреде-те ын Домнул дин тоатэ инима та ши ну те бизуи пе ынцелепчуня та!
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Рекуноаште-Л ын тоате кэиле тале, ши Ел ыць ва нетези кэрэриле.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Ну те сокоти сингур ынцелепт; теме-те де Домнул ши абате-те де ла рэу!
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Ачаста ва адуче сэнэтате трупулуй тэу ши рэкорире оаселор тале.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Чинстеште пе Домнул ку авериле тале ши ку челе динтый роаде дин тот венитул тэу,
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 кэч атунч грынареле ыць вор фи плине де белшуг ши тяскуриле тале вор ӂеме де муст.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Фиуле, ну диспрецуи мустраря Домнулуй ши ну те мыхни де педепселе Луй!
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Кэч Домнул мустрэ пе чине юбеште, ка ун пэринте пе копилул пе каре-л юбеште!
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Фериче де омул каре гэсеште ынцелепчуня ши де омул каре капэтэ причепере!
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Кэч кыштигул пе каре-л адуче еа есте май бун декыт ал арӂинтулуй, ши венитул адус де еа есте май де прец декыт аурул;
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 еа есте май де прец декыт мэргэритареле ши тоате комориле тале ну се пот асемуи ку еа.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Ын дряпта ей есте о вяцэ лунгэ; ын стынга ей, богэцие ши славэ.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Кэиле ей сунт ниште кэй плэкуте ши тоате кэрэриле ей сунт ниште кэрэрь пашниче.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Еа есте ун пом де вяцэ пентру чей че о апукэ, ши чей че о ау сунт феричиць.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Прин ынцелепчуне а ынтемеят Домнул пэмынтул ши прин причепере а ынтэрит Ел черуриле;
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 прин штиинца Луй с-ау дескис адынкуриле ши стрекоарэ норий роуа.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Фиуле, сэ ну се депэртезе ынвэцэтуриле ачестя де окий тэй: пэстрязэ ынцелепчуня ши кибзуинца,
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 кэч еле вор фи вяца суфлетулуй тэу ши подоаба гытулуй тэу!
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Атунч вей мерӂе ку ынкредере пе друмул тэу, ши пичорул ну ци се ва потикни.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Кынд те вей кулка, вей фи фэрэ тямэ, ши кынд вей дорми, сомнул ыць ва фи дулче.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Ну те теме нич де спаймэ нэпрасникэ, нич де о нэвэлире дин партя челор рэй,
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 кэч Домнул ва фи нэдеждя та ши Ел ыць ва пэзи пичорул де кэдере.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Ну опри о бинефачере челуй че аре невое де еа, кынд поць с-о фачь.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Ну зиче апроапелуй тэу: „Ду-те ши вино ярэшь; ыць вой да мыне”, кынд ай де унде сэ дай!
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ну гынди рэу ымпотрива апроапелуй тэу, кынд локуеште лиништит лынгэ тине!
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Ну те черта фэрэ причинэ ку чинева, кынд ну ць-а фэкут ничун рэу!
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Ну пизмуи пе омул асупритор ши ну алеӂе ничуна дин кэиле луй!
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Кэч Домнул урэште пе оамений стрикаць, дар есте приетен ку чей фэрэ приханэ.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Блестемул Домнулуй есте ын каса челуй рэу, дар локуинца челор неприхэниць о бинекувынтязэ.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Кынд аре а фаче ку чей батжокориторь, Ышь бате жок де ей, дар челор смериць ле дэ хар.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Ынцелепций вор моштени слава, дар партя челор небунь есте рушиня.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Провербеле 3 >