< Провербеле 27 >
1 Ну те фэли ку зиуа де мыне, кэч ну штий че поате адуче о зи!
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Сэ те лауде алтул, ну гура та, ун стрэин, ну бузеле тале!
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Пятра есте гря ши нисипул есте греу, дар супэраря пе каре о причинуеште небунул есте май гря декыт амындоуэ.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Фурия есте фэрэ милэ ши мыния, нэвалникэ, дар чине поате ста ымпотрива ӂелозией?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Май бине о мустраре пе фацэ декыт о приетение аскунсэ.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 Рэниле фэкуте де ун приетен доведеск крединчошия луй, дар сэрутэриле унуй врэжмаш сунт минчиноасе.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 Сэтулул калкэ ын пичоаре фагуреле де мьере, дар пентру чел флэмынд тоате амэрэчуниле сунт дулчь.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Ка пасэря плекатэ дин куйбул ей, аша есте омул плекат дин локул сэу.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Кум ынвеселеск унтделемнул ши тэмыя инима, аша де дулчь сунт сфатуриле плине де драгосте але унуй приетен.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Ну пэрэси пе приетенул тэу ши пе приетенул татэлуй тэу, дар ну интра ын каса фрателуй тэу ын зиуа неказулуй тэу: май бине ун вечин апроапе декыт ун фрате департе.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Фиуле, фий ынцелепт ши ынвеселеште-мь инима, ши атунч вой путя рэспунде челуй че мэ батжокореште!
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 Омул кибзуит веде рэул ши се аскунде, дар проштий мерг спре ел ши сунт педепсиць.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Я-й хайна, кэч с-а пус кезаш пентру алтул, я-л зэлог ын локул уней стрэине!
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 Бинекувынтаря апроапелуй ку глас таре дис-де-диминяцэ есте привитэ ка ун блестем.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 О стряшинэ, каре пикурэ некурмат ынтр-о зи де плоае, ши о невастэ гылчевитоаре сунт тот уна.
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 Чине о опреште паркэ опреште вынтул ши паркэ цине унтделемнул ын мына дряптэ.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Дупэ кум ферул аскуте ферул, тот аша ши омул ацыцэ мыния алтуй ом.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Чине ынгрижеште де ун смокин ва мынка дин родул луй ши чине-шь пэзеште стэпынул ва фи прецуит.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Кум рэспунде ын апэ фаца ла фацэ, аша рэспунде инима омулуй инимий омулуй.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Дупэ кум Локуинца морцилор ши адынкул ну се пот сэтура, тот аша нич окий омулуй ну се пот сэтура. (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
21 Че есте тигая пентру лэмуриря арӂинтулуй ши купторул пентру лэмуриря аурулуй, ачея есте бунул нуме пентру ун ом.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Пе небун, кяр дакэ л-ай писа ку писэлогул ын пиуэ, ын мижлокул грэунцелор, небуния тот н-ар еши дин ел.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Ынгрижеште бине де оиле тале ши я сяма ла турмеле тале!
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 Кэч ничо богэцие ну цине вешник ши нич кунуна ну рэмыне пе вечие.
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 Дупэ че се ридикэ фынул, се аратэ вердяца ноуэ, ши ербуриле де пе мунць сунт стрынсе.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 Меий сунт пентру ымбрэкэминте ши цапий, пентру плата огорулуй;
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 лаптеле капрелор ць-ажунӂе пентру храна та, а касей тале ши пентру ынтрецинеря служничелор тале.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.