< Провербеле 16 >
1 Плануриле пе каре ле фаче инима атырнэ де ом, дар рэспунсул пе каре-л дэ гура вине де ла Домнул.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Тоате кэиле омулуй сунт курате ын окий луй, дар Чел че черчетязэ духуриле есте Домнул.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Ынкрединцязэ-ць лукрэриле ын мына Домнулуй, ши ыць вор избути плануриле.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Домнул а фэкут тоате пентру о цинтэ, кяр ши пе чел рэу пентру зиуа ненорочирий.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Орьче инимэ труфашэ есте о скырбэ ынаинтя Домнулуй: хотэрыт, еа ну ва рэмыне непедепситэ.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Прин драгосте ши крединчошие, омул испэшеште нелеӂюиря, ши прин фрика де Домнул, се абате де ла рэу.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Кынд сунт плэкуте Домнулуй кэиле куйва, ый фаче приетень кяр ши пе врэжмаший луй.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Май бине пуцин ку дрептате декыт марь венитурь ку стрымбэтате.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Инима омулуй се гындеште пе че кале сэ мяргэ, дар Домнул ый ындряптэ паший.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Хотэрырь думнезеешть сунт пе бузеле ымпэратулуй, гура луй ну требуе сэ факэ грешель кынд жудекэ.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Кынтарул ши кумпэна дряптэ вин де ла Домнул; тоате греутэциле де кынтэрит сунт лукраря Луй.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Ымпэрацилор ле есте скырбэ сэ факэ рэу, кэч прин неприхэнире се ынтэреште ун скаун де домние.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Бузеле неприхэните сунт плэкуте ымпэрацилор, ши ей юбеск пе чел че ворбеште ку неприхэнире.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Мыния ымпэратулуй есте ун веститор ал морций, дар ун ом ынцелепт требуе с-о потоляскэ.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 Сенинэтатя фецей ымпэратулуй есте вяца ши бунэвоинца луй есте ка о плоае де примэварэ.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Ку кыт май мулт фаче кыштигаря ынцелепчуний декыт а аурулуй! Ку кыт есте май де дорит кыштигаря причеперий декыт а арӂинтулуй!
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Каля оаменилор фэрэ приханэ есте сэ се феряскэ де рэу; ачела ышь пэзеште суфлетул, каре вегязэ асупра кэий сале.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Мындрия мерӂе ынаинтя пеирий ши труфия мерӂе ынаинтя кэдерий.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Май бине сэ фий смерит ку чей смериць декыт сэ ымпарць прада ку чей мындри.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Чине куӂетэ ла Кувынтул Домнулуй гэсеште феричиря ши чине се ынкреде ын Домнул есте феричит.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Чине аре о инимэ ынцеляптэ есте нумит причепут, дар дулчаца бузелор мэреште штиинца.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Ынцелепчуня есте ун извор де вяцэ пентру чине о аре, дар педяпса небунилор есте небуния лор.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Чине аре о инимэ ынцеляптэ ышь аратэ ынцелепчуня кынд ворбеште ши мереу се вэд ынвэцэтурь ной пе бузеле луй.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Кувинтеле приетеноасе сунт ка ун фагуре де мьере: дулчь пентру суфлет ши сэнэтоасе пентру оасе.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Мулте кэй и се пар буне омулуй, дар ла урмэ дук ла моарте.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 Чине мунчеште, пентру ел мунчеште, кэч фоамя луй ыл ындямнэ ла лукру.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 Омул стрикат прегэтеште ненорочиря ши пе бузеле луй есте ка ун фок апринс.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Омул неастымпэрат стырнеште чертурь ши пырыторул дезбинэ пе чей май бунь приетень.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 Омул асупритор амэӂеште пе апроапеле сэу ши-л дуче пе о кале каре ну есте бунэ.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Чине ынкиде окий ка сэ се дедя ла гындурь стрикате, чине-шь мушкэ бузеле, а ши сэвыршит рэул.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Перий албь сунт о кунунэ де чинсте, еа се гэсеште пе каля неприхэнирий.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Чел ынчет ла мыние прецуеште май мулт декыт ун витяз ши чине есте стэпын пе сине прецуеште май мулт декыт чине кучереште четэць.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Се арункэ сорцул ын поала хайней, дар орьче хотэрыре вине де ла Домнул.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.