< МИКА 1 >

1 Кувынтул Домнулуй, спус луй Мика, дин Морешет, пе время луй Иотам, Ахаз, Езекия, ымпэраций луй Иуда, пророчие асупра Самарией ши Иерусалимулуй.
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Аскултаць вой, попоаре тоате! Я аминте, пэмынтуле ши че есте пе ел! Домнул Думнезеу сэ фие мартор ымпотрива воастрэ, Домнул каре есте ын Темплул Луй чел сфынт!
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 Кэч ятэ кэ Домнул есе дин локуинца Луй, Се кобоарэ ши умблэ пе ынэлцимиле пэмынтулуй!
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 Суб Ел се топеск мунций, вэиле крапэ ка чара ынаинтя фокулуй, ка апа каре курӂе прин рыпе.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 Ши тоате ачестя дин причина нелеӂюирий луй Иаков, дин причина пэкателор касей луй Исраел! Дар каре есте нелеӂюиря луй Иаков? Ну есте оаре Самария? Ши каре есте пэкатул луй Иуда? Ну есте оаре Иерусалимул?…
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 „Де ачея вой префаче Самария ынтр-ун морман де петре пе кымп, ынтр-ун лок де сэдит вие; ый вой прэвэли петреле ын вале ши-й вой дезголи темелииле.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 Тоате кипуриле ей чоплите вор фи сфэрымате, тоате плэциле ей де курвэ вор фи арсе ын фок ши-й вой пустии тоць идолий, кэч дин плэць де курвэ й-а адунат ши ын плэць де курвэ се вор префаче…”
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 Де ачея плынг, мэ боческ, умблу дескулц ши гол, стриг ка шакалул ши ӂем ка струцул.
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 Кэч рана ей есте фэрэ ляк; се ынтинде пынэ ла Иуда, пэтрунде пынэ ла поарта попорулуй меу, пынэ ла Иерусалим.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Ну спунець лукрул ачеста ын Гат ши ну плынӂець ын Ако; тэвэлици-вэ ын цэрынэ ла Бет-Леафра.
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Тречь, локуитоаре дин Шафир, ку рушиня дескоперитэ; локуитоаря дин Цаанан ну ындрэзнеште сэ ясэ, жаля Бет-Хаецелулуй вэ я густул сэ вэ оприць ын ел.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 Кэч локуитоаря дин Марот тремурэ пентру пердеря феричирий ей, фииндкэ с-а коборыт ненорочиря дин партя Домнулуй пынэ ла поарта Иерусалимулуй.
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Ынхамэ-ць каий чей юць ла кар, локуитоаре дин Лакис; ту ай фост чя динтый причинэ де пэкат пентру фийка Сионулуй, кэч ын тине с-ау гэсит нелеӂюириле луй Исраел.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 Де ачея те вей деспэрци де Морешет-Гат, каселе дин Акзиб вор фи о амэӂире пентру ымпэраций луй Исраел.
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 Ыць вой адуче ун ноу стэпын, локуитоаре дин Мареша; слава луй Исраел ва мерӂе ла Адулам.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Раде-ць, тае-ць пэрул дин причина копиилор тэй юбиць; лэрӂеште-ць плешувия ка вултурул, кэч ей се дук ын робие департе де тине!
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

< МИКА 1 >