< МИКА 2 >

1 Вай де чей че куӂетэ нелеӂюиря ши фэуреск реле ын аштернутул лор; кынд се крапэ де зиуэ о ынфэптуеск, дакэ ле стэ ын путере.
Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
2 Дакэ пофтеск огоаре, пун мына пе еле, дакэ дореск касе, ле рэпеск; асупреск пе ом ши каса луй, пе ом ши моштениря луй.
Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
3 Де ачея, аша ворбеште Домнул: „Ятэ, Еу ам де гынд сэ адук о ненорочире ымпотрива ачестуй лят де оамень, де каре ну вэ вець фери грумажий ши ну вець май умбла ку капул атыт де сус, кэч времуриле вор фи реле.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
4 Ын зиуа ачея, вець ажунӂе де поминэ, вець бочи ши вець зиче: ‘С-а испрэвит! Сунтем пустииць ку десэвыршире! Партя де моштенире а попорулуй меу трече ын мына алтуя! Вай, кум мь-о я! Огоареле ноастре ле ымпарте врэжмашулуй…!’”
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
5 Де ачея ну вей авя пе нимень каре сэ ынтиндэ фрынгия де мэсурат пентру сорцул тэу, ын адунаря Домнулуй.
Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
6 „Ну пророчиць!” зик ей. „Сэ ну се пророчаскэ асеменя лукрурь. Кэч алтминтерь окэриле ну май ынчетязэ!”
Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
7 Есте Домнул атыт де грабник ла мыние, каса луй Иаков? Ачеста есте фелул Луй де а лукра? „Да, кувинтеле Меле сунт приелниче челуй че умблэ ку неприхэнире!
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
8 Де мултэ време попорул Меу есте сокотит де Мине ка врэжмаш; вой рэпиць мантауа де пе хайнеле челор че трек лиништиць ши н-ау густ де рэзбой.
Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
9 Вой изгониць дин каселе лор юбите пе фемеиле попорулуй Меу, луаць пентру тотдяуна подоаба Мя де ла копиий лор.
Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
10 Скулаци-вэ ши плекаць, кэч аич ну есте одихнэ пентру вой, кэч, дин причина спуркэчуний, вор фи дурерь, дурерь путерниче.
Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 Да, дакэ ар вени ун ом ку вынт ши минчунь ши ар зиче: ‘Ыць вой пророчи деспре вин ши деспре бэутурь тарь’, ачела ар фи ун пророк пентру попорул ачеста!
Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
12 Те вой стрынӂе ын ынтреӂиме, Иакове! Вой стрынӂе рэмэшица луй Исраел, ый вой адуна ка пе ниште ой динтр-ун стаул, ка пе о турмэ ын пэшуня ей, аша кэ ва фи о маре зарвэ де оамень.
“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 Чел че ва фаче спэртура се ва суи ынаинтя лор; вор фаче спэртура, вор трече пе поартэ ши вор еши пе еа; ымпэратул лор ва мерӂе ынаинтя лор ши Домнул ва фи ын фрунтя лор.”
Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”

< МИКА 2 >