< Матей 7 >

1 Ну жудекаць, ка сэ ну фиць жудекаць.
“Musaweruze ena, kuti inunso mungadzaweruzidwe.
2 Кэч ку че жудекатэ жудекаць, вець фи жудекаць; шику че мэсурэ мэсураць, ви се ва мэсура.
Pakuti momwe inu muweruzira ena, inunso mudzaweruzidwa chimodzimodzi, muyeso umene muyesera ena inunso mudzayesedwa ndi womwewo.
3 Дече везь ту паюл дин окюл фрателуй тэу ши ну те уйць ку бэгаре де сямэ ла бырна дин окюл тэу?
“Chifukwa chiyani iwe uyangʼana kachitsotso ka mʼdiso la mʼbale wako koma susamalira chimtengo chili mʼdiso mwako?
4 Сау, кум поць зиче фрателуй тэу: ‘Ласэ-мэ сэ скот паюл дин окюл тэу’ ши, кынд коло, ту ай о бырнэ ынтр-ал тэу?
Kodi unganene bwanji kwa mʼbale wako kuti, ‘Ndikuchotse kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene nthawi zonse chimtengo uli nacho mʼdiso mwako?
5 Фэцарникуле, скоате ынтый бырна дин окюл тэу, ши атунч вей ведя деслушит сэ скоць паюл дин окюл фрателуй тэу.
Wachiphamaso iwe! Yamba wachotsa chimtengo chili mʼdiso mwako ndipo pamenepo udzatha kuona bwino ndi kuchotsa kachitsotso kali mʼdiso mwa mʼbale wako.
6 Сэ нудаць кынилор лукруриле сфинте ши сэ ну арункаць мэргэритареле воастре ынаинтя порчилор, ка ну кумва сэ ле калче ын пичоаре ши сэ се ынтоаркэ сэ вэ рупэ.
“Musapatse agalu zinthu zopatulika; kapena musaponyere nkhumba ngale zanu. Pakuti ngati mutero, zidzaziponda ndipo pomwepo zidzakutembenukirani ndi kukudulani nthulinthuli.
7 Черець, ши ви се ва да; кэутаць, ши вець гэси; батець, ши ви се ва дескиде.
“Pemphani ndipo mudzapatsidwa; funafunani ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsekulirani.
8 Кэч орьчинечере капэтэ; чине каутэ гэсеште; ши челуй че бате, и се дескиде.
Pakuti wopempha aliyense amalandira; ndi wofuna amapeza; ndipo iye amene agogoda, adzamutsekulira.
9 Чинеесте омул ачела динтре вой каре, дакэ-й чере фиул сэу о пыне, сэ-й дя о пятрэ?
“Ndani mwa inu, mwana wake akamupempha buledi amamupatsa mwala?
10 Сау, дакэ-й чере ун пеште, сэ-й дя ун шарпе?
Kapena ngati mwana apempha nsomba, kodi amamupatsa njoka?
11 Деч, дакэ вой, каресунтець рэй, штиць сэ даць дарурь буне копиилор воштри, ку кыт май мулт Татэл востру, каре есте ын черурь, ва да лукрурь буне челор че И ле чер!
Tsono ngati inu woyipitsitsa mumadziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanga Atate anu akumwamba sadzapereka mphatso zabwino kwa iwo amene amupempha?
12 Тот чевоиць сэ вэ факэ воуэ оамений, фачеци-ле ши вой ла фел; кэч ын ачастасунт купринсе Леӂя ши Пророчий.
Nʼchifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu akuchitireni, yambani ndinu kuwachitira, pakuti izi ndi zimene malamulo ndi aneneri amaphunzitsa.
13 Интраць пе поарта чя стрымтэ. Кэч ларгэ есте поарта, латэ есте каля каре дуче ла перзаре ши мулць сунт чей че интрэ пе еа.
“Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo.
14 Дар стрымтэ есте поарта, ынгустэ есте каля каре дуче ла вяцэ ши пуцинь сунт чей че о афлэ.
Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.
15 Пэзици-вэ де пророчь минчиношь. Ейвин ла вой ымбрэкаць ын хайне де ой, дар пе динэунтру сунт ниште лупь рэпиторь.
“Chenjerani nawo aneneri onyenga. Amabwera kwa inu atavala zikopa zankhosa, koma mʼkati mwawo ali mimbulu yolusa.
16 Ый вець куноаште дупэроаделе лор. Кулегоамений стругурь дин спинь сау смокине дин мэрэчинь?
Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula?
17 Тот аша, орьчепом бун фаче роаде буне, дар помул рэу фаче роаде реле.
Chimodzimodzinso mtengo wabwino umabala chipatso chabwino, koma mtengo woyipa umabala chipatso choyipa.
18 Помул бун ну поате фаче роаде реле, нич помул рэу ну поате фаче роаде буне.
Mtengo wabwino sungabale chipatso choyipa, ndi mtengo woyipa sungabale chipatso chabwino.
19 Орьчепом каре ну фаче роаде буне есте тэят ши арункат ын фок.
Mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino umadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
20 Аша кэ дупэ роаделе лор ый вець куноаште.
Momwemonso, ndi zipatso zawo iwo mudzawazindikira.
21 Ну орьчине-Мь зиче: ‘Доамне, Доамне!’ ва интра ын Ымпэрэция черурилор, чи чел че фаче воя Татэлуй Меу, каре есте ын черурь.
“Si munthu aliyense amene amanena kwa Ine, ‘Ambuye, Ambuye,’ adzalowe mu ufumu wakumwamba, koma ndi yekhayo amene amachita chifuniro cha Atate anga amene ali kumwamba.
22 Мулць Ымь вор зиче ын зиуа ачея: ‘Доамне, Доамне! Н-ампророчит ной ын Нумеле Тэу? Н-ам скос ной драчь ын Нумеле Тэу? Ши н-ам фэкут ной мулте минунь ын Нумеле Тэу?’
Ambiri adzati kwa Ine pa tsikulo, ‘Ambuye, Ambuye, kodi sitinkanenera mʼdzina lanu ndi mʼdzina lanunso tinkatulutsa ziwanda ndi kuchita zodabwitsa zambiri?’
23 Атунч, ле вой спуне курат: ‘Ничодатэ ну в-ам куноскут; депэртаци-вэде ла Мине, вой тоць каре лукраць фэрэделеӂе.’
Pamenepo ndidzawawuza momveka bwino kuti, ‘Sindinakudziweni inu. Chokani kwa Ine, inu ochita zoyipa!’
24 Де ачея, пе орьчинеауде ачесте кувинте але Меле ши ле фаче, ыл вой асемэна ку ун ом ку жудекатэ, каре шь-а зидит каса пе стынкэ.
“Nʼchifukwa chake aliyense amene amva mawu anga ndi kuwachita akufanana ndi munthu wanzeru amene anamanga nyumba yake pa thanthwe.
25 А дат плоая, ау венит шувоаеле, ау суфлат вынтуриле ши ау бэтут ын каса ачея, дар еа ну с-а прэбушит, пентру кэ авя темелия зидитэ пе стынкэ.
Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo; koma sinagwe, chifukwa maziko ake anali pa thanthwe.
26 Ынсэ орьчине ауде ачесте кувинте але Меле ши ну ле фаче ва фи асемэнат ку ун ом некибзуит, каре шь-а зидит каса пе нисип.
Koma aliyense amene amva mawu angawa ndi kusawachita ali ngati munthu wopusa amene anamanga nyumba yake pa mchenga.
27 А дат плоая, ау венит шувоаеле, ау суфлат вынтуриле ши ау избит ын каса ачея: еа с-а прэбушит, ши прэбуширя й-а фост маре.”
Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo, ndipo inagwa ndipo kugwa kwake kunali kwakukulu.”
28 Дупэ че а сфыршит Исус кувынтэриле ачестя, нороаделе ау рэмас уймите де ынвэцэтура Луй;
Yesu atamaliza kunena zonsezi, magulu a anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake,
29 кэч Ел ый ынвэца ка унул каре авя путере, ну кум ый ынвэцау кэртурарий лор.
chifukwa anaphunzitsa ngati amene anali ndi ulamuliro osati ngati aphunzitsi amalamulo.

< Матей 7 >