< Иуда 1 >
1 Иуда, роб ал луй Исус Христос ши фрателе луй Иаков, кэтре чей кемаць, каре сунт юбиць ын Думнезеу Татэл ши пэстраць пентру Исус Христос:
Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo. Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.
2 ындураря, пачя ши драгостя сэ вэ фие ынмулците.
Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.
3 Пряюбицилор, пе кынд кэутам ку тот динадинсул сэ вэ скриу деспре мынтуиря ноастрэ де обште, м-ам вэзут силит сэ вэ скриу ка сэ вэ ындемн сэ луптаць пентру крединца каре а фост датэ сфинцилор о датэ пентру тотдяуна.
Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima.
4 Кэч с-ау стрекурат принтре вой уний оамень скришь демулт пентру осында ачаста, оамень неевлавиошь, каре скимбэ ын десфрынаре харул Думнезеулуй ностру ши тэгэдуеск пе сингурул ностру Стэпын ши Домн, Исус Христос.
Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.
5 Вряу сэ вэ адук аминте, мэкар кэ штиць о датэ пентру тотдяуна тоате ачесте лукрурь, кэ Домнул, дупэ че а избэвит пе попорул Сэу дин цара Еӂиптулуй, ын урмэ а нимичит пе чей че н-ау крезут.
Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire.
6 Ел а пэстрат пентру жудеката зилей челей марь, пушь ын ланцурь вешниче, ын ынтунерик, пе ынӂерий каре ну шь-ау пэстрат вредничия, чи шь-ау пэрэсит локуинца. (aïdios )
Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios )
7 Тот аша, Содома ши Гомора ши четэциле димпрежурул лор, каре се дэдусерэ ка ши еле ла курвие ши ау пофтит дупэ трупул алтуя, не стау ынаинте ка о пилдэ, суферинд педяпса унуй фок вешник. (aiōnios )
Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios )
8 Тотушь оамений ачештя, тырыць де висэриле лор, ышь пынгэреск ла фел трупул, несокотеск стэпыниря ши батжокореск дрегэторииле.
Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba.
9 Архангелул Михаил, кынд се ымпотривя дяволулуй ши се черта ку ел пентру трупул луй Мойсе, н-а ындрэзнит сэ ростяскэ ымпотрива луй о жудекатэ де окарэ, чи доар а зис: „Домнул сэ те мустре!”
Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!”
10 Ачештя, димпотривэ, батжокореск че ну куноск ши се перд сингурь ын чея че штиу дин фире, ка добитоачеле фэрэ минте.
Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.
11 Вай де ей! Кэч ау урмат пе каля луй Каин! С-ау арункат ын рэтэчиря луй Балаам дин доринца де кыштиг! Ау перит ынтр-о рэскоалэ ка а луй Коре!
Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.
12 Сунт ниште стынчь аскунсе ла меселе воастре де драгосте, унде се оспэтязэ фэрэ рушине ымпреунэ ку вой ши се ындоапэ де-а бинеля; ниште норь фэрэ апэ, мынаць ынкоаче ши ынколо де вынтурь, ниште помь томнатичь фэрэ род, де доуэ орь морць, дезрэдэчинаць;
Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu.
13 ниште валурь ынфурияте але мэрий, каре ышь спумегэ рушиниле лор, ниште стеле рэтэчитоаре, кэрора ле есте пэстратэ негура ынтунерикулуй пентру вечие. (aiōn )
Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn )
14 Ши пентру ей а пророчит Енох, ал шаптеля патриарх де ла Адам, кынд а зис: „Ятэ кэ а венит Домнул ку зечиле де мий де сфинць ай Сэй,
Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka
15 ка сэ факэ о жудекатэ ымпотрива тутурор ши сэ ынкрединцезе пе тоць чей нелеӂюиць де тоате фаптеле нелеӂюите, пе каре ле-ау фэкут ын кип нелеӂюит, ши де тоате кувинтеле де окарэ пе каре ле-ау ростит ымпотрива Луй ачешть пэкэтошь нелеӂюиць.”
kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.”
16 Ей сунт ниште кыртиторь, немулцумиць ку соарта лор, трэеск дупэ пофтеле лор, гура ле есте плинэ де ворбе труфаше ши слэвеск пе оамень пентру кыштиг.
Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.
17 Дар вой, пряюбицилор, адучеци-вэ аминте де ворбеле вестите май динаинте де апостолий Домнулуй ностру Исус Христос:
Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu.
18 кум вэ спуняу кэ ын времуриле дин урмэ вор фи батжокориторь, каре вор трэи дупэ пофтеле лор нелеӂюите.
Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.”
19 Ей сунт ачея каре дау наштере ла дезбинэрь, оамень супушь пофтелор фирий, каре н-ау Духул.
Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.
20 Дар вой, пряюбицилор, зидици-вэ суфлетеште пе крединца воастрэ прясфынтэ, ругаци-вэ прин Духул Сфынт,
Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera.
21 цинеци-вэ ын драгостя луй Думнезеу ши аштептаць ындураря Домнулуй ностру Исус Христос пентру вяца вешникэ. (aiōnios )
Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios )
22 Мустраць пе чей че се деспарт де вой;
Muwachitire chifundo amene akukayika.
23 кэутаць сэ мынтуиць пе уний, смулгынду-й дин фок; де алций ярэшь фие-вэ милэ ку фрикэ, урынд пынэ ши кэмаша мынжитэ де карне.
Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.
24 Яр Ачелуя каре поате сэ вэ пэзяскэ де орьче кэдере ши сэ вэ факэ сэ вэ ынфэцишаць фэрэ приханэ ши плинь де букурие ынаинтя славей Сале,
Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa,
25 сингурулуй Думнезеу, Мынтуиторул ностру, прин Исус Христос, Домнул ностру, сэ фие славэ, мэрецие, путере ши стэпынире, май ынаинте де тоць вечий, ши акум, ши ын вечь. Амин. (aiōn )
kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )