< Иоан 1 >

1 Ла ынчепут ера Кувынтул, ши Кувынтул ера ку Думнезеу, ши Кувынтул ера Думнезеу.
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 Ел ера ла ынчепут ку Думнезеу.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 Тоате лукруриле ау фост фэкуте прин Ел; ши нимик дин че а фост фэкут, н-а фост фэкут фэрэ Ел.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 Ын Ел ера вяца, ши вяца ера лумина оаменилор.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 Лумина луминязэ ын ынтунерик, ши ынтунерикул н-а бируит-о.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 А венит ун ом тримис де Думнезеу: нумеле луй ера Иоан.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 Ел а венит ка мартор, ка сэ мэртурисяскэ деспре Луминэ, пентру ка тоць сэ крядэ прин ел.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 Ну ера ел Лумина, чи ел а венит ка сэ мэртурисяскэ деспре Луминэ.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 Лумина ачаста ера адевэрата Луминэ, каре луминязэ пе орьче ом венинд ын луме.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 Ел ера ын луме, ши лумя а фост фэкутэ прин Ел, дар лумя ну Л-а куноскут.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 А венит ла ай Сэй, ши ай Сэй ну Л-ау примит.
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 Дар тутурор челор че Л-ау примит, адикэ челор че кред ын Нумеле Луй, ле-а дат дрептул сэ се факэ копий ай луй Думнезеу;
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 нэскуць ну дин сынӂе, нич дин воя фирий лор, нич дин воя вреунуй ом, чи дин Думнезеу.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 Ши Кувынтул С-а фэкут труп ши а локуит принтре ной, плин де хар ши де адевэр. Ши ной ам привит слава Луй, о славэ ынтокмай ка слава сингурулуй нэскут дин Татэл.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 Иоан а мэртурисит деспре Ел кынд а стригат: „Ел есте Ачела деспре каре зичям еу: ‘Чел че вине дупэ мине есте ынаинтя мя, пентру кэ ера ынаинте де мине.’”
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 Ши ной тоць ам примит дин плинэтатя Луй ши хар дупэ хар;
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 кэч Леӂя а фост датэ прин Мойсе, дар харул ши адевэрул ау венит прин Исус Христос.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 Нимень н-а вэзут вреодатэ пе Думнезеу; сингурул Луй Фиу, каре есте ын сынул Татэлуй, Ачела Л-а фэкут куноскут.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 Ятэ мэртурисиря фэкутэ де Иоан кынд иудеий ау тримис дин Иерусалим пе ниште преоць ши левиць сэ-л ынтребе: „Ту чине ешть?”
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 Ел а мэртурисит ши н-а тэгэдуит: а мэртурисит кэ ну есте ел Христосул.
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 Ши ей л-ау ынтребат: „Дар чине ешть? Ешть Илие?” Ши ел а зис: „Ну сунт!” „Ешть пророкул?” Ши ел а рэспунс: „Ну!”
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 Атунч й-ау зис: „Дар чине ешть? Ка сэ дэм ун рэспунс челор че не-ау тримис. Че зичь ту деспре тине ынсуць?”
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 „Еу”, а зис ел, „сунт гласул челуй че стригэ ын пустиу: ‘Нетезиць каля Домнулуй’, кум а зис пророкул Исая.”
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 Тримиший ерау дин партя фарисеилор.
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 Ей й-ау май пус урмэтоаря ынтребаре: „Атунч де че ботезь, дакэ ну ешть Христосул, нич Илие, нич пророкул?”
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 Дрепт рэспунс, Иоан ле-а зис: „Еу ботез ку апэ, дар ын мижлокул востру стэ Унул пе каре вой ну-Л куноаштець.
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 Ел есте Ачела каре вине дупэ мине ши каре есте ынаинтя мя; еу ну сунт вредник сэ-Й дезлег куряуа ынкэлцэминтей Луй.”
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 Ачесте лукрурь с-ау петрекут ын Бетабара, динколо де Йордан, унде ботеза Иоан.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 А доуа зи, Иоан а вэзут пе Исус венинд ла ел ши а зис: „Ятэ Мелул луй Думнезеу, каре ридикэ пэкатул лумий!
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 Ел есте Ачела деспре каре зичям: ‘Дупэ мине вине ун Ом, каре есте ынаинтя мя, кэч ера ынаинте де мине.’
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 Еу ну-Л куноштям, дар токмай пентру ачаста ам венит сэ ботез ку апэ: ка Ел сэ фие фэкут куноскут луй Исраел.”
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 Иоан а фэкут урмэтоаря мэртурисире: „Ам вэзут Духул коборынду-Се дин чер ка ун порумбел ши опринду-Се песте Ел.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 Еу ну-Л куноштям, дар Чел че м-а тримис сэ ботез ку апэ мь-а зис: ‘Ачела песте каре вей ведя Духул коборынду-Се ши опринду-Се есте Чел че ботязэ ку Духул Сфынт.’
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 Ши еу ам вэзут лукрул ачеста ши ам мэртурисит кэ Ел есте Фиул луй Думнезеу.”
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 А доуа зи, Иоан стэтя ярэшь ку дой дин ученичий луй.
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 Ши, пе кынд привя пе Исус умблынд, а зис: „Ятэ Мелул луй Думнезеу!”
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 Чей дой ученичь л-ау аузит ростинд ачесте ворбе ши ау мерс дупэ Исус.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 Исус С-а ынторс ши, кынд й-а вэзут кэ мерг дупэ Ел, ле-а зис: „Че кэутаць?” Ей Й-ау рэспунс: „Рабби (каре, тэлмэчит, ынсямнэ: ‘Ынвэцэторуле’), унде локуешть?”
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 „Вениць де ведець”, ле-а зис Ел. С-ау дус де ау вэзут унде локуя ши ын зиуа ачея ау рэмас ла Ел. Ера кам пе ла часул ал зечеля.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 Унул дин чей дой каре аузисерэ кувинтеле луй Иоан ши мерсесерэ дупэ Исус ера Андрей, фрателе луй Симон Петру.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 Ел, чел динтый, а гэсит пе фрателе сэу Симон ши й-а зис: „Ной ам гэсит пе Месия” (каре, тэлмэчит, ынсямнэ: „Христос”).
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 Ши л-а адус ла Исус. Исус л-а привит ши й-а зис: „Ту ешть Симон, фиул луй Иона; туте вей кема Кифа” (каре, тэлмэчит, ынсямнэ: „Петру”).
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 А доуа зи, Исус а врут сэ Се дукэ ын Галилея ши а гэсит пе Филип. Ши й-а зис: „Вино дупэ Мине.”
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 Филип ера дин Бетсаида, четатя луй Андрей ши а луй Петру.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 Филип а гэсит пе Натанаел ши й-а зис: „Ной ам гэсит пе Ачела деспре каре ау скрис Мойсе ын Леӂе ши пророчий: пе Исус дин Назарет, фиул луй Иосиф.”
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 Натанаел й-а зис: „Поате еши чева бун дин Назарет?” „Вино ши везь!” й-а рэспунс Филип.
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 Исус а вэзут пе Натанаел венинд ла Ел ши а зис деспре ел: „Ятэ куадевэрат ун исраелит ын каре ну есте виклешуг.”
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 „Де унде мэ куношть?” Й-а зис Натанаел. Дрепт рэспунс, Исус й-а зис: „Те-ам вэзут май ынаинте ка сэ те кеме Филип, кынд ерай суб смокин.”
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 Натанаел Й-а рэспунс: „Рабби, Ту ешть Фиул луй Думнезеу, Ту ешть Ымпэратул луй Исраел!”
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 Дрепт рэспунс, Исус й-а зис: „Пентру кэ ць-ам спус кэ те-ам вэзут суб смокин, крезь? Лукрурь май марь декыт ачестя вей ведя.”
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 Апой й-а зис: „Адевэрат, адевэрат вэ спун кэ, де акумынколо, вець ведя черул дескис ши пе ынӂерий луй Думнезеу суинду-се ши коборынду-се песте Фиул омулуй.”
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

< Иоан 1 >