< Йов 9 >

1 Йов а луат кувынтул ши а зис:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 „Штиу бине кэ есте аша. Ши кум ар путя омул сэ-шь скоатэ дрептате ынаинтя луй Думнезеу?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Дакэ ар вои сэ се черте ку Ел, дин о мие де лукрурь н-ар путя сэ рэспундэ ла унул сингур.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Але Луй сунт ынцелепчуня ши атотпутерничия: чине И с-ар путя ымпотриви фэрэ сэ фие педепсит?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Ел мутэ деодатэ мунций ши-й рэстоарнэ ын мыния Са.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Згудуе пэмынтул дин темелия луй, де и се клатинэ стылпий.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Порунчеште соарелуй, ши соареле ну май рэсаре; ши цине стелеле суб печетя Луй.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 Нумай Ел ынтинде черуриле ши умблэ пе ынэлцимиле мэрий.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 Ел а фэкут Урса-Маре, Лучяфэрул де сярэ ши Ралицеле ши стелеле дин цинутуриле де мязэзи.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 Ел фаче лукрурь марь ши непэтрунсе, минунь фэрэ нумэр.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Ятэ, Ел трече пе лынгэ мине, ши ну-Л вэд, Се дуче, ши ну-Л зэреск.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Дакэ апукэ Ел, чине-Л ва опри? Чине-Й ва зиче: ‘Че фачь?’
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Думнезеу ну-Шь ынтоарче мыния; суб Ел се плякэ тоць сприжиниторий мындрией.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 Ши еу кум сэ-Й рэспунд? Че кувинте сэ алег?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Кяр дакэ аш авя дрептате, ну Й-аш рэспунде. Ну пот декыт сэ мэ рог жудекэторулуй.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Ши кяр дакэ м-ар аскулта кынд Ыл кем, тот н-аш путя креде кэ мь-а аскултат гласул –
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Ел, каре мэ избеште ка ынтр-о фуртунэ, каре ымь ынмулцеште фэрэ причинэ рэниле,
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 каре ну мэ ласэ сэ рэсуфлу, мэ сатурэ де амэрэчуне.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Сэ алерг ла путере? Ел есте атотпутерник. Ла дрептате? Чине мэ ва апэра?
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Орькытэ дрептате аш авя, гура мя мэ ва осынди ши орькыт де невиноват аш фи, Ел мэ ва арэта ка виноват.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 Невиноват! Сунт, дар ну цин ла вяцэ, ымь диспрецуеск вяца.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Че-мь пасэ ла урма урмей? Кэч ындрэзнеск с-о спун: Ел нимичеште пе чел невиноват ка ши пе чел виноват.
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Ши дакэ бичул ар причинуи мэкар ындатэ моартя…! Дар Ел рыде де ынчеркэриле челуй невиноват.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 Пэмынтул есте дат пе мыниле челуй нелеӂюит; Ел акоперэ окий жудекэторилор – де ну Ел, апой чине алтул?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 Зилеле меле аляргэ май юць декыт ун алергэтор; фуг фэрэ сэ фи вэзут феричиря;
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 трек ка ши корэбииле челе юць, ка вултурул каре се репеде асупра прэзий.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Дакэ зик: ‘Вряу сэ-мь уйт суферинцеле, сэ-мь лас ынтристаря ши сэ фиу войос’,
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 сунт ынгрозит де тоате дурериле меле. Штиу кэ ну мэ вей скоате невиноват.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Ши дакэ вой фи жудекат виноват, пентру че сэ мэ май трудеск деӂяба?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 Кяр дакэ м-аш спэла ку зэпадэ, кяр дакэ мь-аш курэци мыниле ку лешие,
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Ту тот м-ай куфунда ын мочирлэ, де с-ар скырби пынэ ши хайнеле де мине!
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 Кэч Ел ну есте ун ом ка мине, ка сэ-Й пот рэспунде ши сэ мерӂем ымпреунэ ла жудекатэ.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Нич ну есте вреун мижлочитор ынтре ной, каре сэ-шь пунэ мына песте ной амындой.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Сэ-Шь трагэ ынсэ варга де дясупра мя ши сэ ну мэ май тулбуре спайма Луй.
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Атунч вой ворби ши ну мэ вой теме де Ел. Алтфел, ну сунт стэпын пе мине.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Йов 9 >