< Йов 7 >
1 Соарта омулуй пе пэмынт есте ка а унуй осташ ши зилеле луй сунт ка але унуй мунчитор ку зиуа.
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Кум суспинэ робул дупэ умбрэ, кум ышь аштяптэ мунчиторул плата,
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 аша ам еу парте де лунь де дурере, ши партя мя сунт нопць де суферинцэ.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 Мэ кулк ши зик: ‘Кынд мэ вой скула? Кынд се ва сфырши ноаптя?’ Ши мэ сатур де фрэмынтэрь пынэ ын ревэрсатул зорилор.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 Трупул ми се акоперэ ку вермь ши ку о коажэ пэмынтоасэ, пеля-мь крапэ ши се десфаче.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 Зилеле меле збоарэ май юць декыт сувейка цесэторулуй, се дук ши ну май ам ничо нэдежде!
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Аду-Ць аминте, Думнезеуле, кэ вяца мя есте доар о суфларе! Окий мей ну вор май ведя феричиря.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 Окюл каре мэ привеште ну мэ ва май приви; окюл Тэу мэ ва кэута ши ну вой май фи.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 Кум се рисипеште норул ши трече, аша ну се ва май ридика чел че се кобоарэ ын Локуинца морцилор! (Sheol )
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
10 Ну се ва май ынтоарче ын каса луй ши ну-шь ва май куноаште локул ын каре локуя.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Де ачея ну-мь вой цине гура, чи вой ворби ын нелиништя инимий меле, мэ вой тынгуи ын амэрэчуня суфлетулуй меу.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Оаре о маре сунт еу сау ун балаур де маре, де-ай пус стражэ ын журул меу?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 Кынд зик: ‘Патул мэ ва ушура, кулкушул ымь ва алина дурериле’,
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 атунч мэ ынспэймынць прин висе, мэ ынгрозешть прин ведений.
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 Ах, аш вря май бине гытуиря, май бине моартя декыт ачесте оасе!
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Ле диспрецуеск!… Ну вой трэи ын вечь… Ласэ-мэ, кэч доар о суфларе ми-й вяца!
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 Че есте омул ка сэ-Ць песе атыт де мулт де ел, ка сэ ей сяма ла ел,
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 сэ-л черчетезь ын тоате диминециле ши сэ-л ынчерчь ын тоате клипеле?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Кынд вей ынчета одатэ сэ мэ привешть? Кынд ымь вей да рэгаз сэ-мь ынгит скуйпатул?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Дакэ ам пэкэтуит, че пот сэ-Ць фак, Пэзиторул оаменилор? Пентру че м-ай пус цинтэ сэӂецилор Тале, де ам ажунс о поварэ кяр пентру мине ынсумь?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Пентру че ну-мь ерць пэкатул ши пентру че ну-мь уйць фэрэделеӂя? Кэч вой адорми ын цэрынэ ши, кынд мэ вей кэута, ну вой май фи!”
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”