< Йов 35 >

1 Елиху а луат дин ноу кувынтул ши а зис:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 „Ыць ынкипуй кэ ай дрептате ши крезь кэ те ындрептэцешть ынаинтя луй Думнезеу
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 кынд зичь: ‘Ла че-мь фолосеште, че кыштиг ам кэ ну пэкэтуеск?’
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Ыць вой рэспунде ши ла ачаста, цие ши приетенилор тэй тотодатэ.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Уйтэ-те спре черурь ши привеште! Везь норий кыт де сус сунт фацэ де тине?
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Дакэ пэкэтуешть, че рэу Ый фачь Луй? Ши кынд пэкателе ци се ынмулцеск, че-Й фачь Луй?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Дакэ ешть дрепт, че-Й дай Луй? Че примеште Ел дин мына та?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Рэутатя та ну поате вэтэма декыт пе семенул тэу, дрептатя та ну фолосеште декыт фиулуй омулуй.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 Оамений стригэ ымпотрива мулцимий апэсэторилор, се плынг де силничия мултора;
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 дар ничунул ну зиче: ‘Унде есте Думнезеу, Фэкэторул меу, каре не инсуфлэ кынтэрь де веселие ноаптя,
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 каре не ынвацэ май мулт декыт пе добитоачеле пэмынтулуй ши не дэ май мултэ причепере декыт пэсэрилор черулуй?’
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Сэ тот стриӂе ей атунч, кэч Думнезеу ну рэспунде дин причина мындрией челор рэй.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Деӂяба стригэ, кэч Думнезеу н-аскултэ, Чел Атотпутерник ну я аминте.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Мэкар кэ зичь кэ ну-Л везь, тотушь причина та есте ынаинтя Луй: аштяптэ-Л!
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Дар, пентру кэ мыния Луй ну педепсеште ынкэ, ну ынсямнэ кэ пуцин Ый пасэ де нелеӂюире.
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Аша кэ Йов ышь дескиде гура деӂяба ши спуне о мулциме де ворбе фэрэ рост.”
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Йов 35 >