< Йов 12 >
1 Йов а луат кувынтул ши а зис:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 „С-ар путя зиче, ын адевэр, кэ нямул оменеск сунтець вой ши кэ одатэ ку вой ва мури ши ынцелепчуня!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Ам ши еу минте ка вой, ну сунт май прежос декыт вой. Ши чине ну штие лукруриле пе каре ле спунець вой?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Еу сунт де батжокура приетенилор мей кынд чер ажуторул луй Думнезеу: дрептул, невиноватул, де батжокурэ!
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 ‘Диспрец ын ненорочире!’ – ятэ зичеря челор феричиць: дэ брынчь куй алунекэ ку пичорул!
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Жефуиторилор ли се ласэ кортуриле ын паче, челор че мыние пе Думнезеу ле мерӂе бине, мэкар кэ Думнезеул лор есте ын пумн.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Ынтрябэ добитоачеле, ши те вор ынвэца; пэсэриле черулуй, ши ыць вор спуне;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 ворбеште пэмынтулуй, ши те ва ынвэца; ши пештий мэрий ыць вор повести.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Чине ну веде ын тоате ачестя довада кэ мына Домнулуй а фэкут асеменя лукрурь?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Ел цине ын мынэ суфлетул а тот че трэеште, суфларя орькэруй труп оменеск.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Ну деосебеште урекя кувинтеле, кум густэ черул гурий мынкэруриле?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Ла бэтрынь се гэсеште ынцелепчуня ши ынтр-о вяцэ лунгэ е причеперя.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Ла Думнезеу есте ынцелепчуня ши путеря; сфатул ши причеперя але Луй сунт.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Че дэрымэ Ел ну ва фи зидит дин ноу; пе чине-л ынкиде Ел, нимень ну-л ва скэпа.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Ел опреште апеле, ши тотул се усукэ; Ел ле дэ друмул, ши пустиеск пэмынтул.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Ел аре путеря ши ынцелепчуня; Ел стэпынеште пе чел че се рэтэчеште сау рэтэчеште пе алций.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Ел я робь пе сфетничь ши тулбурэ минтя жудекэторилор.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Ел дезлягэ легэтура ымпэрацилор ши ле пуне о фрынгие ын журул коапселор.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Ел я робь пе преоць; Ел рэстоарнэ пе чей путерничь.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Ел тае ворба челор мештерь ла ворбэ; Ел я минтя челор бэтрынь.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Ел варсэ диспрецул асупра челор марь; Ел дезлягэ брыул челор тарь.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Ел дескоперэ че есте аскунс ын ынтунерик; Ел адуче ла луминэ умбра морций.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Ел фаче пе нямурь сэ кряскэ ши Ел ле нимичеште; Ел ле ынтинде пынэ департе ши Ел ле адуче ынапой ын хотареле лор.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Ел я минтя кэпетениилор попорулуй; Ел ый фаче сэ рэтэчяскэ ын пустиурь фэрэ друм,
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 унде быжбые прин ынтунерик ши ну вэд деслушит; Ел ый фаче сэ се клатине ка ниште оамень бець.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.