< Иеремия 50 >
1 Ятэ кувынтул ростит де Домнул асупра Бабилонулуй, асупра цэрий халдеенилор, прин пророкул Иеремия:
Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
2 „Даць де штире принтре нямурь, даць де весте ши ынэлцаць ун стяг! Вестиць, н-аскундець нимик! Спунець: ‘Бабилонул есте луат! Бел есте акоперит де рушине, Меродак есте здробит! Идолий луй сунт акопериць де рушине, идолий луй сунт сфэрымаць!’
“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
3 Кэч ымпотрива луй се суе ун ням де ла мязэноапте, каре-й ва префаче цара ынтр-ун пустиу ши ну ва май фи локуитэ; атыт оамений, кыт ши добитоачеле фуг ши се дук.
Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
4 Ын зилеле ачеля, ын времуриле ачеля”, зиче Домнул, „копиий луй Исраел ши копиий луй Иуда се вор ынтоарче ымпреунэ; вор мерӂе плынгынд ши вор кэута пе Домнул Думнезеул лор.
“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
5 Вор ынтреба де друмул Сионулуй, ышь вор ынтоарче привириле спре ел ши вор зиче: ‘Вениць сэ не алипим де Домнул принтр-ун легэмынт вешник, каре сэ ну фие уйтат ничодатэ!’
Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
6 Попорул Меу ера о турмэ де ой пердуте; пэсторий лор ый рэтэчяу, ый фэчяу сэ кутреере мунций; тречяу де пе мунць пе дялурь, уйтынду-шь стаулул.
“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
7 Тоць чей че-й гэсяу ый мынкау ши врэжмаший лор зичяу: ‘Ной ну сунтем виноваць, фииндкэ ау пэкэтуит ымпотрива Домнулуй, Локашул неприхэнирий, ымпотрива Домнулуй, Нэдеждя пэринцилор лор.’
Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
8 Фуӂиць дин Бабилон, ешиць дин цара халдеенилор, ши мерӂець ка ниште цапь ын фрунтя турмей!
“Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
9 Кэч ятэ кэ вой ридика ши вой адуче ымпотрива Бабилонулуй о мулциме де нямурь марь дин цара де ла мязэноапте; се вор ыншируи ын ширурь де бэтае ымпотрива луй ши вор пуне стэпынире пе ел; сэӂециле луй сунт ка але унуй рэзбойник искусит, каре ну се ынтоарче ку мыниле гоале.
Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
10 Астфел ва фи датэ прадэ жафулуй Халдея, ши тоць чей че о вор жефуи се вор сэтура де жаф”, зиче Домнул.
Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
11 „Кэч вой в-аць букурат ши в-аць веселит кынд Мь-аць жефуит моштениря Мя! Да, сэряць ка о жунканэ ын ярбэ, некезаць ка ниште армэсарь фокошь!
“Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
12 Мама воастрэ есте акоперитэ де рушине, чя каре в-а нэскут рошеште де рушине; ятэ, еа есте коада нямурилор, есте ун пустиу, ун пэмынт ускат ши фэрэ апэ!
Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
13 Дин причина мынией Домнулуй ну ва май фи локуитэ ши ва фи о пустиетате. Тоць чей че вор трече пе лынгэ Бабилон се вор мира ши вор флуера пентру тоате рэниле луй.
Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
14 Ыншируици-вэ де бэтае ымпрежурул Бабилонулуй вой, тоць аркаший! Траӂець ымпотрива луй, ну фачець економие де сэӂець! Кэч а пэкэтуит ымпотрива Домнулуй.
“Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
15 Скоатець дин тоате пэрциле ун стригэт де рэзбой ымпотрива луй! Ел ынтинде мыниле; темелииле и се прэбушеск; зидуриле и се сурпэ. Кэч есте рэзбунаря Домнулуй. Рэзбунаци-вэ пе ел! Фачеци-й кум а фэкут ши ел!
Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
16 Нимичиць ку десэвыршире дин Бабилон пе чел че сямэнэ ши пе чел че мынуеште сечера ла время сечеришулуй! Ынаинтя сабией нимичиторулуй, фиекаре сэ се ынтоаркэ ла попорул сэу, фиекаре сэ фугэ спре цара луй.
Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
17 Исраел есте о оае рэтэчитэ пе каре ау гонит-о леий; ымпэратул Асирией а мынкат-о чел динтый ши ачеста дин урмэ й-а здробит оаселе, ачест Небукаднецар, ымпэратул Бабилонулуй.”
“Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
18 Де ачея, аша ворбеште Домнул оштирилор, Думнезеул луй Исраел: „Ятэ, вой педепси пе ымпэратул Бабилонулуй ши цара луй кум ам педепсит пе ымпэратул Асирией.
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 Вой адуче ынапой пе Исраел ын пэшуня луй; ва паште пе Кармел ши пе Басан ши ышь ва потоли фоамя пе мунтеле луй Ефраим ши ын Галаад.
Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 Ын зилеле ачеля, ын время ачея”, зиче Домнул, „се ва кэута нелеӂюиря луй Исраел, ши ну ва май фи, ши пэкатул луй Иуда, ши ну се ва май гэси, кэч вой ерта рэмэшица пе каре о вой лэса.
Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
21 Суе-те ымпотрива цэрий де доуэ орь рэзврэтите, ымпотрива локуиторилор ей ши педепсеште-й! Урмэреште-й, мэчелэреште-й, нимичеште-й”, зиче Домнул, „ши ымплинеште ын тотул порунчиле Меле!
“Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
22 Стригэте де рэзбой рэсунэ ын царэ ши прэпэдул есте маре.
Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
23 Кум с-а рупт ши с-а сфэрымат чоканул ынтрегулуй пэмынт! Бабилонул есте нимичит ын мижлокул нямурилор!
Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
24 Ць-ам ынтинс о курсэ, ши ай фост принс, Бабилонуле, фэрэ сэ те аштепць. Ай фост ажунс, апукат, пентру кэ ай луптат ымпотрива Домнулуй.
Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
25 Домнул Шь-а дескис каса де арме ши а скос дин еа армеле мынией Луй, кэч ачаста есте о лукраре а Домнулуй Думнезеулуй оштирилор ын цара халдеенилор.
Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
26 Пэтрундець дин тоате пэрциле ын Бабилон, дескидеци-й грынареле, фачеци-ле ниште мормане ка ниште грэмезь де снопь ши нимичици-ле. Нимик сэ ну май рэмынэ дин ел!
Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
27 Учидеци-й тоць таурий ши ынжунгияци-й! Вай де ей! Кэч ле-а венит зиуа, время педепсирий лор!
Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
28 Аскултаць стригэтеле фугарилор, але челор че скапэ дин цара Бабилонулуй, ка сэ вестяскэ ын Сион рэзбунаря Домнулуй Думнезеулуй ностру, рэзбунаря пентру Темплул Сэу!
Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
29 Кемаць ымпотрива Бабилонулуй пе аркашь, вой тоць каре ынкордаць аркул! Тэбэрыць ын журул луй, ка нимень сэ ну скапе, рэсплэтици-й дупэ фаптеле луй, фачеци-й ынтокмай кум а фэкут ши ел! Кэч с-а семецит ымпотрива Домнулуй, ымпотрива Сфынтулуй луй Исраел!
“Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
30 Де ачея, тинерий луй вор кэдя пе улице ши тоць оамений луй де рэзбой вор пери ын зиуа ачея”, зиче Домнул.
Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
31 „Ятэ, ам неказ пе тине, ынгымфатуле”, зиче Домнул Думнезеул оштирилор, „кэч ць-а сосит зиуа, время педепсирий тале!
“Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
32 Ынгымфатул ачела се ва потикни ши ва кэдя ши нимень ну-л ва ридика, вой пуне фок четэцилор луй, ши-й ва мистуи тоате ымпрежуримиле.”
Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
33 Аша ворбеште Домнул оштирилор: „Копиий луй Исраел ши копиий луй Иуда сунт апэсаць ымпреунэ; тоць чей че й-ау дус робь ый опреск ши ну вор сэ ле дя друмул.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
34 Дар путерник есте Рэзбунэторул лор, Ел, ал кэруй Нуме есте Домнул оштирилор. Ел ле ва апэра причина, ка сэ дя одихнэ цэрий ши сэ факэ пе локуиторий Бабилонулуй сэ тремуре.
Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
35 Сабия ымпотрива халдеенилор”, зиче Домнул, „ымпотрива локуиторилор Бабилонулуй, ымпотрива кэпетениилор ши ынцелепцилор луй!
Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
36 Сабия ымпотрива пророчилор минчуний, ка сэ ажунгэ ка ниште оамень фэрэ минте! Сабия ымпотрива витежилор луй, ка сэ рэмынэ ынкремениць!
Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
37 Сабия ымпотрива каилор ши карелор луй, ымпотрива оаменилор де тот фелул каре сунт ын мижлокул луй, ка сэ ажунгэ ка фемеиле! Сабия ымпотрива вистиериилор луй, ка сэ фие жефуите!
Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
38 Сечета песте апеле луй, ка сэ сече! Кэч есте о царэ де идоль ши ау ыннебунит ку идолий лор.
Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
39 Де ачея, фяреле пустиулуй се вор ашеза аколо ымпреунэ ку шакалий ши струций вор локуи аколо; ну ва май фи локуит ничодатэ, чи вешник ва рэмыне нелокуит.
“Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
40 Ка ши Содома ши Гомора ши четэциле вечине пе каре ле-а нимичит Думнезеу”, зиче Домнул, „аша ну ва май фи локуит нич ел ши нимень ну се ва май ашеза аколо.
Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
41 Ятэ, вине ун попор де ла мязэноапте ши ун ням маре ши ниште ымпэраць путерничь се ридикэ де ла марӂиниле пэмынтулуй.
“Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
42 Поартэ арк ши сулицэ, сунт некруцэторь ши фэрэ милэ; гласул ле муӂеште ка маря; сунт кэларе пе кай, ка ун ом гата де луптэ ымпотрива та, фийка Бабилонулуй!
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
43 Ымпэратул Бабилонулуй ауде вестя, мыниле и се слэбеск ши ыл апукэ гроаза, ка дуреря пе о фемее каре наште…
Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
44 Ятэ, врэжмашул се суе ка ун леу де пе малуриле ынгымфате але Йорданулуй ымпотрива локуинцей тале тарь; деодатэ ый вой изгони де аколо ши вой пуне песте ей пе ачела пе каре л-ам алес. Кэч чине есте ка Мине? Чине-Мь ва порунчи? Ши каре кэпетение Ымь ва ста ымпотривэ?”
Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
45 Де ачея, аскултаць хотэрыря пе каре а луат-о Домнул ымпотрива Бабилонулуй ши плануриле пе каре ле-а фэкут Ел ымпотрива цэрий халдеенилор: „Ку адевэрат, ый вор тыры ка пе ниште ой слабе, ку адевэрат, ле вор пустии локуинца.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
46 Де стригэтул луэрий Бабилонулуй се кутремурэ пэмынтул ши се ауде ун стригэт де дурере принтре нямурь.”
Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.