< Иеремия 23 >

1 „Вай де пэсторий каре нимическ ши рисипеск турма пэшуний Меле”, зиче Домнул.
“Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
2 Де ачея, аша ворбеште Домнул Думнезеул луй Исраел ымпотрива пэсторилор каре паск пе попорул меу: „Пентру кэ Мь-аць рисипит оиле, ле-аць изгонит ши ну в-аць ынгрижит де еле, ятэ кэ вэ вой педепси дин причина рэутэций фаптелор воастре”, зиче Домнул.
Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
3 „Ши Еу Ынсумь вой стрынӂе рэмэшица оилор Меле дин тоате цэриле ын каре ле-ам изгонит; ле вой адуче ынапой ын пэшуня лор ши вор креште ши се вор ынмулци.
“Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
4 Вой пуне песте еле пэсторь каре ле вор паште; ну ле ва май фи тямэ, нич гроазэ ши ну ва май липси ничуна дин еле”, зиче Домнул.
Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
5 „Ятэ вин зиле”, зиче Домнул, „кынд вой ридика луй Давид о Одраслэ неприхэнитэ. Ел ва ымпэрэци, ва лукра ку ынцелепчуне ши ва фаче дрептате ши жудекатэ ын царэ.
Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
6 Ын время Луй, Иуда ва фи мынтуит ши Исраел ва авя линиште ын локуинца луй; ши ятэ Нумеле пе каре и-Л вор да: ‘Домнул, Неприхэниря ноастрэ’!
Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
7 Де ачея ятэ вин зиле”, зиче Домнул, „кынд ну се ва май зиче: ‘Виу есте Домнул, каре а скос дин цара Еӂиптулуй пе копиий луй Исраел!’
Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
8 Чи се ва зиче: ‘Виу есте Домнул, каре а скос ши а адус ынапой сэмынца касей луй Исраел дин цара де ла мязэноапте ши дин тоате цэриле ын каре ый рисиписем!’ Ши вор локуи ын цара лор.”
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
9 Асупра пророчилор. „Инима ымь есте здробитэ ын мине, тоате оаселе ымь тремурэ; сунт ка ун ом бят, ка ун ом амецит де вин, дин причина Домнулуй ши дин причина сфинтелор Луй кувинте.
Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
10 Кэч цара есте плинэ де прякурвий ши цара се желеште дин причина журэминтелор; кымпииле пустиулуй сунт ускате. Тоатэ алергэтура лор цинтеште нумай ла рэу ши тоатэ витежия лор есте пентру нелеӂюире!”
Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
11 „Пророчий ши преоций сунт стрикаць; ле-ам гэсит рэутатя кяр ши ын Каса Мя”, зиче Домнул.
“Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
12 „Де ачея, каля лор ва фи лунекоасэ ши ынтунекоасэ, вор фи ымпиншь ши вор кэдя, кэч вой адуче ненорочиря песте ей ын анул кынд ый вой педепси”, зиче Домнул.
“Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
13 „Ын пророчий Самарией ам вэзут урмэтоаря небуние: ау пророчит пе Баал ши ау рэтэчит пе попорул Меу Исраел!
“Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
14 Дар ын пророчий Иерусалимулуй ам вэзут лукрурь грозаве. Сунт прякурварь, трэеск ын минчунэ, ынтэреск мыниле челор рэй, аша кэ ничунул ну се май ынтоарче де ла рэутатя луй; тоць сунт ынаинтя Мя ка Содома ши локуиторий Иерусалимулуй, ка Гомора.”
Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
15 Де ачея, аша ворбеште Домнул оштирилор деспре пророчь: „Ятэ, ый вой хрэни ку пелин ши ле вой да сэ бя апе отрэвите; кэч прин пророчий Иерусалимулуй с-а рэспындит нелеӂюиря ын тоатэ цара.”
Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
16 Аша ворбеште Домнул оштирилор: „Н-аскултаць кувинтеле пророчилор каре вэ пророческ! Ей вэ лягэнэ ын ынкипуирь задарниче; спун ведений ешите дин инима лор, ну че вине дин гура Домнулуй.
Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
17 Ей спун челор че Мэ несокотеск: ‘Домнул а зис: «Вець авя паче!»’ ши зик тутурор челор че трэеск дупэ аплекэриле инимий лор: ‘Ну ви се ва ынтымпла ничун рэу.’
Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
18 Чине а фост де фацэ ла сфатул Домнулуй ка сэ вадэ ши сэ аскулте кувынтул Луй? Чине а плекат урекя ла кувынтул Луй ши чине л-а аузит?
Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
19 Ятэ кэ фуртуна Домнулуй, урӂия избукнеште, се нэпустеште вижелия ши каде песте капул челор рэй!
Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
20 Мыния Домнулуй ну се ва потоли пынэ ну ва ымплини ши ва ынфэптуи плануриле инимий Луй. Вець ынцелеӂе ын тотул лукрул ачеста ын курсул времурилор.
Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
21 Еу н-ам тримис пе пророчий ачештя, ши тотушь ей ау алергат; ну ле-ам ворбит, ши тотушь ау пророчит.
Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
22 Дакэ ар фи фост де фацэ ла сфатул Меу, ар фи требуит сэ спунэ кувинтеле Меле попорулуй Меу ши сэ-й ынтоаркэ де ла каля лор ря, де ла рэутатя фаптелор лор!
Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
23 Сунт Еу нумай ун Думнезеу де апроапе”, зиче Домнул, „ши ну сунт Еу ши ун Думнезеу де департе?
Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
24 Поате чинева сэ стя ынтр-ун лок аскунс фэрэ сэ-л вэд Еу?”, зиче Домнул. „Ну умплу Еу черуриле ши пэмынтул?”, зиче Домнул.
Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
25 „Ам аузит че спун пророчий каре пророческ минчунь ын Нумеле Меу, зикынд: ‘Ам авут ун вис! Ам висат ун вис!’
“Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
26 Пынэ кынд вор пророчий ачештя сэ пророчаскэ минчунь, сэ пророчаскэ ыншелэторииле инимий лор?
Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
27 Кред ей оаре кэ пот фаче пе попорул Меу сэ уйте Нумеле Меу, прин виселе пе каре ле историсеште фиекаре дин ей, апроапелуй лор, кум Мь-ау уйтат пэринций лор Нумеле дин причина луй Баал?
Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
28 Пророкул каре а авут ун вис сэ историсяскэ висул ачеста ши чине а аузит Кувынтул Меу сэ спунэ ынтокмай Кувынтул Меу! Пентру че сэ аместечь паеле ку грыул?”, зиче Домнул.
Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
29 „Ну есте Кувынтул Меу ка ун фок”, зиче Домнул, „ши ка ун чокан каре сфэрымэ стынка?
Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
30 Де ачея, ятэ”, зиче Домнул, „ам неказ пе пророчий каре ышь аскунд унул алтуя кувинтеле Меле.
Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
31 Ятэ”, зиче Домнул, „ам неказ пе пророчий каре яу кувынтул лор ши-л дау дрепт кувынт ал Меу.
Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
32 Ятэ”, зиче Домнул, „ам неказ пе чей че пророческ висе неадевэрате, каре ле историсеск ши рэтэческ пе попорул Меу ку минчуниле ши ку ындрэзняла лор; ну й-ам тримис Еу, ну Еу ле-ам дат порункэ, ши ну сунт де ничун фолос попорулуй ачестуя”, зиче Домнул.
Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
33 „Дакэ попорул ачеста сау ун пророк, сау ун преот те ва ынтреба: ‘Каре есте аменинцаря Домнулуй?’, сэ ле спуй каре есте ачастэ аменинцаре: ‘«Вэ вой лепэда», зиче Домнул.’
Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
34 Ши пе пророкул, пе преотул сау пе ачела дин попор каре ва зиче: ‘О аменинцаре а Домнулуй’, ыл вой педепси, пе ел ши каса луй!
Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
35 Аша сэ спунець ынсэ, фиекаре апроапелуй сэу, фиекаре фрателуй сэу: ‘Че а рэспунс Домнул?’ сау: ‘Че а зис Домнул?’
Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
36 Дар сэ ну май зичець: ‘О аменинцаре а Домнулуй’, кэч кувынтул фиекэруя ва фи о аменинцаре пентру ел, дакэ вець сучи астфел кувинтеле Думнезеулуй челуй виу, кувинтеле Домнулуй оштирилор, Думнезеулуй ностру!
Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
37 Аша сэ зичь пророкулуй: ‘Че ць-а рэспунс Домнул?’ сау: ‘Че а зис Домнул?’
Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
38 Дар, дакэ вець май зиче: ‘О аменинцаре а Домнулуй’, атунч аша ворбеште Домнул: ‘Пентру кэ спунець кувинтеле ачестя: «О аменинцаре а Домнулуй», мэкар кэ ам тримис сэ вэ спунэ сэ ну май зичець: «О аменинцаре а Домнулуй»,
Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
39 дин причина ачаста, ятэ, вэ вой уйта ши вэ вой лепэда пе вой ши четатя пе каре в-о дэдусем воуэ ши пэринцилор воштри, вэ вой арунка динаинтя Мя
ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
40 ши вой пуне песте вой о вешникэ окарэ ши о вешникэ нечинсте, каре ну се ва уйта.’”
Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”

< Иеремия 23 >