< Иеремия 15 >

1 Домнул мь-а зис: „Кяр дакэ Мойсе ши Самуел с-ар ынфэциша ынаинтя Мя, тот н-аш фи биневоитор фацэ де попорул ачеста. Изгонеште-л динаинтя Мя, дукэ-се!
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 Ши дакэ-ць вор зиче: ‘Унде сэ не дучем?’ сэ ле рэспунзь: ‘Аша ворбеште Домнул: «Ла моарте, чей сортиць ла моарте; ла сабие, чей сортиць сабией; ла фоамете, чей сортиць фоаметей; ла робие, чей сортиць робией!»’
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 Кэч вой тримите ымпотрива лор патру фелурь де ненорочирь”, зиче Домнул: „сабия ка сэ-й учидэ, кыний ка сэ-й сфышие, пэсэриле черулуй ши фяреле пэмынтулуй ка сэ-й мэнынче ши сэ-й нимичяскэ.
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 Ый вой фаче де поминэ пентру тоате ымпэрэцииле пэмынтулуй, дин причина луй Манасе, фиул луй Езекия, ымпэратул луй Иуда, ши пентру тот че а фэкут ел ын Иерусалим.
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 Кэч чине сэ айбэ милэ де тине, Иерусалиме, чине сэ те плынгэ? Чине сэ мяргэ сэ те ынтребе де сэнэтате?
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 М-ай пэрэсит”, зиче Домнул, „ай дат ынапой, де ачея Ымь ынтинд мына ымпотрива та ши те нимическ: сунт сэтул де милэ.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Ый вынтур ку лопата ла порциле цэрий; ый липсеск де копий, перд пе попорул Меу, кэч ну с-ау абэтут де ла кэиле лор.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 Вэдувеле лор сунт май мулте декыт боабеле де нисип дин маре; песте мама тынэрулуй, адук ун пустиитор зиуа-н амяза маре; фак сэ кадэ деодатэ песте еа неказул ши гроаза.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 Чя каре нэскусе шапте фий тынжеште, ышь дэ суфлетул; соареле ей апуне кынд есте ынкэ зиуэ: есте рошие, акоперитэ де рушине. Пе чей че май рэмын, ый дау прадэ сабией ынаинтя врэжмашилор лор”, зиче Домнул.
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 Вай де мине, мамэ, кэ м-ай нэскут пе мине, ом де чартэ ши де причинэ пентру тоатэ цара! Ну яу ку ымпрумут, нич ну дау ку ымпрумут, ши тотушь тоць мэ блестемэ!
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 Домнул а рэспунс: „Да, вей авя ун виитор феричит; да, вой сили пе врэжмаш сэ те роаӂе ла време де ненорочире ши ла време де неказ!
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 Поате ферул сэ фрынгэ ферул де ла мязэноапте ши арама?
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Авериле ши комориле тале ле вой да прадэ фэрэ деспэгубире, дин причина тутурор пэкателор тале, пе тот цинутул тэу.
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 Те вой дуче роб ла врэжмашул тэу, ынтр-о царэ пе каре н-о куношть, кэч фокул мынией Меле с-а апринс ши арде песте вой!”
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 Ту штий тот, Доамне! Аду-ць аминте де мине, ну мэ уйта, рэзбунэ-мэ пе пригониторий мей! Ну мэ луа, дупэ ынделунга Та рэбдаре. Гындеште-Те кэ суфэр окара дин причина Та!
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Кынд ам примит кувинтеле Тале, ле-ам ынгицит; кувинтеле Тале ау фост букурия ши веселия инимий меле, кэч дупэ Нумеле Тэу сунт нумит, Доамне, Думнезеул оштирилор!
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Н-ам шезут ын адунаря челор че петрек, ка сэ мэ веселеск ку ей: де фрика путерий Тале, ам стат сингур ла о парте, кэч мэ умплусешь де мыние.
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Пентру че ну май контенеште суферинца мя? Пентру че мэ устурэ рана ши ну вря сэ се виндече? Сэ фий Ту пентру мине ка ун извор ыншелэтор, ка о апэ каре сякэ?
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Де ачея аша ворбеште Домнул: „Дакэ те вей липи ярэшь де Мине, ыць вой рэспунде ярэшь ши вей ста ынаинтя Мя; дакэ вей деспэрци че есте де прец де че есте фэрэ прец, вей фи ка гура Мя. Ей сэ се ынтоаркэ ла тине, ну ту сэ те ынторчь ла ей!
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Те вой фаче пентру попорул ачеста ка ун зид таре де арамэ; ей се вор рэзбои ку тине, дар ну те вор бируи; кэч Еу вой фи ку тине, ка сэ те скап ши сэ те избэвеск”, зиче Домнул.
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 „Те вой избэви дин мына челор рэй ши те вой скэпа дин мына асуприторилор.”
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Иеремия 15 >