< Исая 65 >

1 „Ерам гата сэ рэспунд челор че ну ынтребау де Мине, ерам гата сэ фиу гэсит де чей че ну Мэ кэутау. Ам зис: ‘Ятэ-Мэ, ятэ-Мэ!’ кэтре ун ням каре ну кема Нумеле Меу.
“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
2 Мь-ам ынтинс мыниле тоатэ зиуа спре ун попор рэзврэтит, каре умблэ пе о кале ря, ын воя гындурилор луй,
Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
3 спре ун попор каре ну контенеште сэ Мэ мыние ын фацэ, адукынд жертфе ын грэдинь ши арзынд тэмые пе кэрэмизиле де пе акопериш,
Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
4 каре локуеште ын морминте ши петрече ноаптя ын пештерь, мынкынд карне де порк ши авынд ын стрэкинь букате некурате,
Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
5 ши каре тотушь зиче: ‘Дэ-те ынапой, ну те апропия де мине, кэч сунт сфынт!’… Асеменя лукрурь сунт ун фум ын нэриле Меле, ун фок каре арде неконтенит!
Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
6 Ятэ че ам хотэрыт ын Мине: ‘Нич гынд сэ так, чи ый вой педепси; да, ый вой педепси.’
“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
7 Пентру нелеӂюириле воастре”, зиче Домнул, „ши пентру нелеӂюириле пэринцилор воштри, каре ау арс тэмые пе мунць ши М-ау батжокорит пе ынэлцимь, де ачея, ле вой мэсура плата пентру фаптеле лор дин трекут.”
ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
8 Аша ворбеште Домнул: „Дупэ кум, кынд се гэсеште зямэ ынтр-ун стругуре, се зиче: ‘Ну-л нимичи, кэч есте о бинекувынтаре ын ел!’, тот аша ши Еу вой фаче ла фел, дин драгосте пентру робий Мей, ка сэ ну нимическ тотул.
Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
9 Вой скоате о сэмынцэ дин Иаков, ши дин Иуда, ун моштенитор ал мунцилор Мей; алеший Мей вор стэпыни цара ши робий Мей вор локуи ын еа.
Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10 Саронул ва служи ка лок де пэшуне оилор ши валя Акор ва служи де кулкуш боилор пентру попорул Меу каре Мэ ва кэута.
Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
11 Дар пе вой, каре пэрэсиць пе Домнул, каре уйтаць мунтеле Меу чел сфынт, каре пунець о масэ ‘Норокулуй’ ши умплець ун пахар ын чинстя ‘Сорций’,
“Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
12 вэ сортеск сабией ши тоць вець плека ӂенункюл ка сэ фиць ынжунгияць, кэч Еу ам кемат, ши н-аць рэспунс, ам ворбит, ши н-аць аскултат, чи аць фэкут че есте рэу ынаинтя Мя ши аць алес че ну-Мь плаче.”
ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
13 Де ачея, аша ворбеште Домнул Думнезеу: „Ятэ кэ робий Мей вор мынка, яр вой вець фи флэмынзь; ятэ кэ робий Мей вор бя, яр воуэ вэ ва фи сете. Ятэ кэ робий Мей се вор букура ши вой вэ вець рушина.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14 Ятэ кэ робий Мей вор кынта, де веселэ че ле ва фи инима, дар вой вець стрига де дуреря пе каре о вець авя ын суфлет ши вэ вець бочи де мыхнит че вэ ва фи духул.
Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15 Вець лэса нумеле востру ка блестем алешилор Мей, ши ануме Домнул Думнезеу вэ ва оморы ши ва да робилор Сэй ун алт нуме.
Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16 Аша кэ чине се ва бинекувынта ын царэ се ва бинекувынта ын Думнезеул адевэрулуй ши чине ва жура ын царэ ва жура пе Думнезеул адевэрулуй, кэч векиле суферинце вор фи уйтате, вор фи аскунсе де окий Мей.
Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
17 Кэч ятэ, Еу фак черурь ной ши ун пэмынт ноу; аша кэ нимень ну-шь ва май адуче аминте де лукруриле трекуте ши нимэнуй ну-й вор май вени ын минте.
“Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
18 Чи вэ вець букура ши вэ вець весели пе вечие пентру челе че вой фаче. Кэч вой префаче Иерусалимул ын веселие ши пе попорул луй, ын букурие.
Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19 Еу Ынсумь Мэ вой весели асупра Иерусалимулуй ши мэ вой букура де попорул Меу; ну се ва май аузи ын ел де акум нич гласул плынсетелор, нич гласул ципетелор.
Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
20 Ну вор май фи ын ел нич копий ку зиле пуцине, нич бэтрынь каре сэ ну-шь ымплиняскэ зилеле. Кэч чине ва мури ла вырста де о сутэ де ань ва фи ынкэ тынэр ши чел че ва мури ын вырстэ де о сутэ де ань ва фи блестемат ка пэкэтос.
“Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
21 Вор зиди касе ши ле вор локуи; вор сэди вий ши ле вор мынка родул.
Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22 Ну вор зиди касе ка алтул сэ локуяскэ ын еле, ну вор сэди вий пентру ка алтул сэ ле мэнынче родул, кэч зилеле попорулуй Меу вор фи ка зилеле копачилор, ши алеший Мей се вор букура де лукрул мынилор лор.
Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
23 Ну вор мунчи деӂяба ши ну вор авя копий ка сэ-й вадэ перинд, кэч вор алкэтуи о сэмынцэ бинекувынтатэ де Домнул ши копиий лор вор фи ымпреунэ ку ей.
Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24 Ынаинте ка сэ Мэ кеме, ле вой рэспунде; ынаинте ка сэ испрэвяскэ ворба, ый вой аскулта!
Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25 Лупул ши мелул вор паште ымпреунэ, леул ва мынка пае ка боул ши шарпеле се ва хрэни ку цэрынэ. Ничун рэу, ничо вэтэмаре ну се ва фаче пе тот мунтеле Меу чел сфынт”, зиче Домнул.
Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.

< Исая 65 >