< Исая 55 >
1 „Вой, тоць чей ынсетаць, вениць ла апе, кяр ши чел че н-аре бань! Вениць ши кумпэраць букате, вениць ши кумпэраць вин ши лапте, фэрэ бань ши фэрэ платэ!
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Де че кынтэриць арӂинт пентру ун лукру каре ну хрэнеште? Де че вэ даць кыштигул мунчий пентру чева каре ну сатурэ? Аскултаци-Мэ дар ши вець мынка че есте бун ши суфлетул востру се ва десфэта ку букате густоасе.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Луаць аминте ши вениць ла Мине, аскултаць, ши суфлетул востру ва трэи, кэч Еу вой ынкея ку вой ун легэмынт вешник, ка сэ ынтэреск ындурэриле Меле фацэ де Давид.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Ятэ, л-ам пус мартор пе лынгэ попоаре, кап ши стэпынитор ал попоарелор.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Ынтр-адевэр, вей кема нямурь пе каре ну ле куношть ши попоаре каре ну те куноск вор алерга ла тине пентру Домнул Думнезеул тэу, пентру Сфынтул луй Исраел, каре те прослэвеште.”
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Кэутаць пе Домнул кытэ време се поате гэси; кемаци-Л кытэ време есте апроапе.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Сэ се ласе чел рэу де каля луй ши омул нелеӂюит сэ се ласе де гындуриле луй, сэ се ынтоаркэ ла Домнул, каре ва авя милэ де ел, ла Думнезеул ностру, каре ну обосеште ертынд.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 „Кэч гындуриле Меле ну сунт гындуриле воастре ши кэиле воастре ну сунт кэиле Меле”, зиче Домнул.
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 „Чи, кыт сунт де сус черуриле фацэ де пэмынт, атыт сунт де сус кэиле Меле фацэ де кэиле воастре ши гындуриле Меле фацэ де гындуриле воастре.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Кэч, дупэ кум плоая ши зэпада се кобоарэ дин черурь ши ну се май ынторк ынапой, чи удэ пэмынтул ши-л фак сэ родяскэ ши сэ одрэсляскэ, пентру ка сэ дя сэмынцэ семэнэторулуй ши пыне челуй че мэнынкэ,
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 тот аша ши Кувынтул Меу каре есе дин гура Мя ну се ынтоарче ла Мине фэрэ род, чи ва фаче воя Мя ши ва ымплини плануриле Меле.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Да, вець еши ку букурие ши вець фи кэлэузиць ын паче. Мунций ши дялуриле вор рэсуна де веселие ынаинтя воастрэ ши тоць копачий дин кымпие вор бате дин палме.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Ын локул спинулуй се ва ынэлца кипаросул, ын локул мэрэчинилор ва креште миртул. Ши лукрул ачеста ва фи о славэ пентру Домнул, ун семн вешник, неперитор.”
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”