< Исая 5 >

1 Вой кынта Пряюбитулуй меу кынтаря Пряюбитулуй меу деспре вия Луй. Пряюбитул меу авя о вие пе о кымпие фоарте мэноасэ.
Ndidzamuyimbira bwenzi langa nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa: Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde.
2 Й-а сэпат пэмынтул, л-а курэцит де петре ши а сэдит ын ел вицеле челе май алесе. А зидит ун турн ын мижлокул ей ши а сэпат ши ун тяск, апой трэӂя нэдежде кэ аре сэ-Й факэ стругурь бунь, дар а фэкут стругурь сэлбатичь.
Anatipula nachotsa miyala yonse ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri. Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo. Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ayi, unabala mphesa zosadya.
3 „Акум дар”, зиче Домнул, „локуиторь ай Иерусалимулуй ши бэрбаць ай луй Иуда, жудекаць вой ынтре Мине ши вия Мя!
“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda, weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
4 Че аш май фи путут фаче вией Меле ши ну й-ам фэкут? Пентру че а фэкут еа стругурь сэлбатичь, кынд Еу мэ аштептам сэ факэ стругурь бунь?
Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa kupambana chomwe ndawuchitira kale? Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji unabala mphesa zosadya?
5 Вэ вой спуне ынсэ акум че вой фаче вией Меле: ый вой смулӂе гардул, ка сэ фие пэскутэ де вите; ый вой сурпа зидул, ка сэ фие кэлкатэ ын пичоаре;
Tsopano ndikuwuzani chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa: ndidzachotsa mpanda wake, ndipo mundawo udzawonongeka; ndidzagwetsa khoma lake, ndipo nyama zidzapondapondamo.
6 о вой пустии; ну ва май фи курэцитэ, нич сэпатэ; спинь ши мэрэчинь вор креште ын еа! Вой порунчи ши норилор сэ ну май плоуэ песте еа.”
Ndidzawusandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pa mundapo.”
7 Вия Домнулуй оштирилор есте каса луй Исраел, ши бэрбаций луй Иуда сунт вица пе каре о юбя. Ел се аштепта ла жудекатэ ши, кынд коло, ятэ сынӂе вэрсат! Се аштепта ла дрептате ши, кынд коло, ятэ стригэте де апэсаре!
Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse ndi Aisraeli, ndipo anthu a ku Yuda ndiwo minda yake yomukondweretsa. Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana; mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.
8 Вай де чей че ынширэ касэ лынгэ касэ ши липеск огор лынгэ огор, пынэ ну май рэмыне лок ши локуеск ын мижлокул цэрий!
Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba, ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda, mpaka mutalanda malo onse kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.
9 Ятэ че мь-а дескоперит Домнул оштирилор: „Хотэрыт, ачесте касе мулте вор фи пустиите, ачесте касе марь ши фрумоасе ну вор май фи локуите.
Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti, “Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja, nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
10 Кяр зече погоане де вие ну вор да декыт ун бат ши ун омер де сэмынцэ ну ва да декыт о ефэ.”
Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi, kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”
11 Вай де чей че дис-де-диминяцэ аляргэ дупэ бэутурь амецитоаре ши шед пынэ ноаптя тырзиу ши се ынфербынтэ де вин!
Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa nathamangira chakumwa choledzeretsa, amene amamwa mpaka usiku kufikira ataledzera kotheratu.
12 Харпа ши алэута, тимпанул, флаутул ши винул ле ынвеселеск оспецеле, дар ну яу сяма ла лукраря Домнулуй ши ну вэд лукрул мынилор Луй.
Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe, matambolini, zitoliro ndi vinyo, ndipo sasamala ntchito za Yehova, salemekeza ntchito za manja ake.
13 Де ачея, попорул меу ва фи дус пе неаштептате ын робие; боеримя луй ва мури де фоаме ши глоата луй се ва уска де сете.
Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo chifukwa cha kusamvetsa zinthu; atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala, ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
14 Де ачея ышь ши дескиде Локуинца морцилор гура ши ышь лэрӂеште песте мэсурэ гытлежул, ка сэ се кобоаре ын еа мэреция ши богэция Сионулуй, ку тоатэ мулцимя луй гэлэӂиоасэ ши веселэ. (Sheol h7585)
Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol h7585)
15 Ши астфел, чей мичь вор фи доборыць, чей марь вор фи смериць ши привириле труфаше вор фи плекате.
Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa, anthu onse adzachepetsedwa, anthu odzikuza adzachita manyazi.
16 Дар Домнул оштирилор ва фи ынэлцат прин жудекатэ ши Думнезеул чел сфынт ва фи сфинцит прин дрептате.
Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama. Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
17 Аколо вор паште меий ка пе имашул лор ши пэсторий прибеӂь вор мынка мошииле прэпэдите але богацилор.
Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo; ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.
18 Вай де чей че траг дупэ ей нелеӂюиря ку фунииле минчуний ши пэкатул, ку шляуриле уней кэруце
Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo, ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
19 ши зик: „Сэ-Шь грэбяскэ, сэ-Шь факэ юте лукраря, ка с-о ведем! Сэ винэ одатэ хотэрыря Сфынтулуй луй Исраел ши сэ се адукэ ла ындеплинире, ка с-о куноаштем!”
amene amanena kuti, “Yehova afulumire, agwire ntchito yake mwamsanga kuti ntchitoyo tiyione. Ntchito zionekere, zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita, zichitike kuti tizione.”
20 Вай де чей че нумеск рэул бине ши бинеле, рэу, каре спун кэ ынтунерикул есте луминэ ши лумина, ынтунерик, каре дау амэрэчуня ын лок де дулчацэ ши дулчаца, ын лок де амэрэчуне!
Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino ndipo zabwino amaziyesa zoyipa, amene mdima amawuyesa kuwala ndipo kuwala amakuyesa mdima, amene zowawasa amaziyesa zotsekemera ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.
21 Вай де чей че се сокотеск ынцелепць ши се кред причепуць!
Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera.
22 Вай де чей тарь кынд есте ворба де бэут вин ши витежь кынд есте ворба де аместекат бэутурь тарь,
Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
23 каре скот ку фаца куратэ пе чел виноват, пентру митэ, ши яу дрептуриле челор невиноваць!
amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
24 Де ачея, кум мистуе о лимбэ де фок мириштя ши кум арде флакэра ярба ускатэ, тот аша ка путрегаюл ле ва фи рэдэчина лор ши флоаря ли се ва рисипи ын вынт ка цэрына, кэч ау несокотит Леӂя Домнулуй оштирилор ши ау диспрецуит Кувынтул Сфынтулуй луй Исраел.
Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
25 Де ачея Се ши апринде Домнул де мыние ымпотрива попорулуй Сэу, Ышь ынтинде мына ымпотрива луй ши-л ловеште де се згудуе мунций ши трупуриле моарте стау ка нороюл ын мижлокул улицелор. Ку тоате ачестя, мыния Луй ну се потолеште ши мына Луй есте ынкэ ынтинсэ.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake; watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha Mapiri akugwedezeka, ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala. Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke, dzanja lake likanali chitambasulire;
26 Ел ридикэ ун стяг попоарелор ындепэртате ши ле флуерэ де ла ун капэт ал пэмынтулуй: ши ятэ-ле, вин репеде ши ушор.
Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali, akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi. Awo akubwera, akubweradi mofulumira kwambiri!
27 Ничунул ну есте обосит, ничунул ну шовэе де обосялэ, ничунул ну дормитязэ, нич ну доарме; ничунуя ну и се десчинӂе брыул де ла мижлок, нич ну и се рупе куряуа де ла ынкэлцэминте.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa, palibe amene akusinza kapena kugona; palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka, palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
28 Сэӂециле лор сунт аскуците ши тоате аркуриле, ынкордате; копителе каилор лор паркэ сунт кремене ши роциле карелор лор паркэ сунт ун выртеж.
Mivi yawo ndi yakuthwa, mauta awo onse ndi okoka, ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi, magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
29 Рэкнеск ка ниште лей, муӂеск ка ниште пуй де лей, сфорэе ши апукэ прада, о яу ку ей, ши нимень ну вине ын ажутор.
Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango, amabangula ngati misona ya mkango; imadzuma pamene ikugwira nyama ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
30 Ын зиуа ачея, ва фи асупра луй Иуда ун муӂет, ка муӂетул уней фуртунь пе маре; уйтынду-се ла пэмынт, ну вор ведя декыт ынтунерик ши стрымтораре, яр лумина се ва ынтунека ын норий луй.
Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja. Ndipo wina akakayangʼana dzikolo adzangoona mdima ndi zovuta; ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.

< Исая 5 >