< Исая 32 >

1 Атунч ымпэратул ва ымпэрэци ку дрептате ши воевозий вор кырмуи ку непэртинире.
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2 Фиекаре ва фи ка ун адэпост ымпотрива вынтулуй ши ка ун лок де скэпаре ымпотрива фуртуний, ка ниште рыурь де апэ ынтр-ун лок ускат, ка умбра уней стынчь марь ынтр-ун пэмынт арс де сете.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3 Окий челор че вэд ну вор май фи легаць ши урекиле челор че ауд вор луа аминте.
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4 Инима челор ушуратичь ва причепе ши ва ынцелеӂе ши лимба гынгавилор ва ворби юте ши деслушит.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5 Небунул ну се ва май нуми алес ла суфлет, нич мишелул ну се ва май нуми ку инимэ ларгэ.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6 Кэч небунул спуне небуний ши инима луй гындеште рэу, ка сэ лукрезе ын кип нелеӂюит ши сэ спунэ неадевэрурь ымпотрива Домнулуй, ка сэ ласе лихнит суфлетул челуй флэмынд ши сэ я бэутура челуй ынсетат.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7 Армеле мишелулуй сунт нимичитоаре; ел фаче планурь виновате ка сэ пярдэ пе чел ненорочит прин кувинте минчиноасе, кяр кынд причина сэракулуй есте дряптэ.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8 Дар чел алес ла суфлет фаче планурь алесе ши стэруеште ын плануриле луй алесе.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
9 Фемей фэрэ грижэ, скулаци-вэ ши аскултаць гласул меу! Фийче непэсэтоаре, луаць аминте ла кувынтул меу!
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Ынтр-ун ан ши кытева зиле, вець тремура, непэсэтоарелор, кэч се ва дуче кулесул виилор ши стрынӂеря поамелор ну ва май вени.
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Ынгрозици-вэ, вой, челе фэрэ грижэ! Тремураць, непэсэтоарелор! Дезбрэкаци-вэ, дезголици-вэ ши ынчинӂеци-вэ коапселе ку хайне де жале!
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Батеци-вэ пептул, адукынду-вэ аминте де фрумусеця кымпиилор ши де родничия виилор.
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
13 Пе пэмынтул попорулуй меу креск спинь ши мэрэчинь, кяр ши ын тоате каселе де плэчере але четэций челей веселе.
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Каса ымпэрэтяскэ есте пэрэситэ, четатя гэлэӂиоасэ есте лэсатэ; дялул ши турнул вор служи пе вечие ка пештерь; мэгарий сэлбатичь се вор жука ын еле ши турмеле вор паште
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 пынэ кынд се ва турна Духул де сус песте ной; атунч пустиул се ва префаче ын пэмынт ши пометул ва фи привит ка о пэдуре.
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Атунч непэртиниря ва локуи ын пустиу ши неприхэниря ышь ва авя локуинца ын помет.
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 Лукраря неприхэнирий ва фи пачя; роаделе неприхэнирий: одихна ши лиништя пе вечие.
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Попорул меу ва локуи ын локуинца пэчий, ын касе фэрэ грижэ ши ын адэпостурь лиништите.
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 Дар пэдуря ва фи прэбушитэ суб гриндинэ, ши четатя, плекатэ адынк.
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 Фериче де вой, каре семэнаць претутиндень де-а лунгул апелор ши каре даць друмул претутиндень боулуй ши мэгарулуй!
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

< Исая 32 >