< Исая 21 >
1 Пророчие асупра пустиулуй мэрий: Кум ынаинтязэ вижелия де ла мязэзи, аша вине ел дин пустиу, дин цара ынфрикошатэ.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 О ведение грозавэ ми с-а дескоперит. Асуприторул асупреште, пустииторул пустиеште. „Суе-те, Еламуле! Ымпресоарэ, Медио! Кэч фак сэ ынчетезе тоате офтэриле лор”, зиче Домнул.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Де ачея ми с-а умплут инима де нелиниште, м-апукэ дурериле, ка дурериле уней фемей кынд наште. Звырколириле ну мэ ласэ с-ауд, тремурул мэ ымпедикэ сэ вэд.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Ымь бате инима ку путере, м-апукэ гроаза; ноаптя плэчерилор меле ажунӂе о ноапте де спаймэ.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Ей пун маса, стража вегязэ, ши ей мэнынкэ, бяу… Дар деодатэ се ауде стригынд: „Ын пичоаре, воевозь! Унӂець скутул!”
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Кэч аша мь-а ворбит Домнул: „Ду-те ши пуне ун стрэжер, ка сэ дя де весте деспре че ва ведя.”
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Ел а вэзут кэлэриме, кэлэрець дой кыте дой, кэлэрець пе мэгарь, кэлэрець пе кэмиле, ши аскулта ку луаре аминте, ку чя май маре бэгаре де сямэ.
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Апой а стригат ка ун леу: „Доамне, ам стат мереу ын турнул меу де пазэ ши стэтям де стражэ ын тоате нопциле.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Ши ятэ кэ а венит кэлэриме ши кэлэрець дой кыте дой.” Апой а луат ярэшь кувынтул ши а зис: „А кэзут, а кэзут Бабилонул ши тоате икоанеле думнезеилор луй сунт сфэрымате ла пэмынт!”
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 О, попорул меу, каре ай фост стропшит ка боабеле де грыу дин ария мя, че ам аузит де ла Домнул оштирилор, Думнезеул луй Исраел, ачея вэ вестеск.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 Пророчие асупра Думей: Ми се стригэ дин Сеир: „Стрэжеруле, кыт май есте дин ноапте? Стрэжеруле, май есте мулт дин ноапте?”
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 Стрэжерул рэспунде: „Вине диминяца, ши есте тот ноапте. Дакэ врець сэ ынтребаць, ынтребаць; ынтоарчеци-вэ ши вениць ярэшь!”
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Пророчие асупра Арабией: Вець петрече ноаптя ын туфеле Арабией, чете де негусторь дин Дедан!
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 Дучець апэ челор че ле есте сете; локуиторий цэрий Тема, дучець пыне фугарилор!
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Кэч ей фуг динаинтя сэбиилор, динаинтя сабией скоасе дин тякэ, динаинтя аркулуй ынкордат ши динаинтя уней лупте ынвершунате.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Кэч аша мь-а ворбит Домнул: „Ынкэ ун ан, ка аний унуй симбриаш, ши с-а испрэвит ку тоатэ слава Кедарулуй.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Ну ва май рэмыне декыт ун мик нумэр дин витежий аркашь, фий ай Кедарулуй, кэч Домнул Думнезеул луй Исраел а спус-о.”
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.