< Исая 18 >
1 Вай де тине, царэ ын каре рэсунэ зэнгэнит де арме ши каре ешть динколо де рыуриле Етиопией!
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Ту, каре тримиць соль пе маре ын корэбий де папурэ, каре плутеск пе лучиул апелор! Дучеци-вэ, соль юць, ла нямул ачела таре ши путерник, ла попорул ачела ынфрикошат де ла ынчепутул луй, ням путерник каре здробеште тотул ши а кэруй царэ есте тэятэ де рыурь!
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Вой, тоць локуиторь ай лумий, ши вой, локуиторь ай пэмынтулуй, луаць сяма кынд се ыналцэ стягул пе мунць ши аскултаць кынд сунэ трымбица!
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 Кэч аша мь-а ворбит Домнул: „Еу привеск лиништит дин локуинца Мя пе кэлдура арзэтоаре а луминий соарелуй ши пе абурул де роуэ, ын випия сечеришулуй.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Дар, ынаинте де сечериш, кынд каде флоаря ши родул се фаче агуридэ, ел тае ындатэ млэдицеле ку косоаре, ба тае кяр лэстарий ши-й арункэ…”
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 Ши асириений вор фи лэсаць астфел прадэ пэсэрилор рэпитоаре дин мунць ши фярелор пэмынтулуй; пэсэриле де прадэ вор петрече вара пе трупуриле лор моарте, ши фяреле пэмынтулуй вор ерна пе еле.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 Ын время ачея, се вор адуче дарурь де мынкаре Домнулуй оштирилор де попорул чел таре ши путерник, де попорул чел ынфрикошат де ла ынчепутул луй, ням путерник, каре здробеште тотул ши а кэруй царэ есте тэятэ де рыурь: вор фи адусе аколо унде локуеште Нумеле Домнулуй оштирилор, пе мунтеле Сионулуй.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.