< Осея 2 >

1 Зичець фрацилор воштри Ами ши сурорилор воастре Рухама!
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Плынӂеци-вэ, плынӂеци-вэ ымпотрива мамей воастре! Кэч ну есте неваста Мя ши Еу ну сунт бэрбатул ей! Сэ-шь депэртезе курвииле динаинтя ей ши прякурвииле де ла цыцеле ей!
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Алтфел, о дезбрак ын пеля гоалэ, кум ера ын зиуа наштерий е, о фак ка ун пустиу, ка ун пэмынт ускат, ши о лас сэ моарэ де сете!
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 Ну вой авя милэ де копиий ей, кэч сунт копий дин курвие.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 Мама лор а курвит; чя каре й-а нэскут с-а нечинстит, кэч а зис: ‘Вой алерга дупэ ибовничий мей, каре ымь дау пыня ши апа мя, лына ши инул меу, унтделемнул ши бэутуриле меле!’
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Де ачея, ятэ, ый вой аступа друмул ку спинь, и-л вой аступа ку ун зид, ка сэ ну-шь май афле кэрэриле.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 Ва алерга дупэ ибовничий ей, дар ну-й ва ажунӂе; ый ва кэута, дар ну-й ва гэси. Апой ва зиче: ‘Хай сэ мэ ынторк ярэшь ла бэрбатул меу чел динтый, кэч ерам май феричитэ атунч декыт акум!’
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Н-а куноскут кэ Еу ый дэдям грыул, мустул ши унтделемнул ши ау ынкинат службей луй Баал арӂинтул ши аурул чел мулт пе каре и-л дэдям.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Де ачея, Ымь вой луа ярэшь ынапой грыул ла время луй ши мустул ла время луй ши ымь вой ридика ярэшь де ла еа лына ши инул пе каре и ле дэдусем ка сэ-й акопере голичуня.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 Ши акум ый вой дескопери рушиня ынаинтя ибовничилор ей ши ничунул н-о ва скоате дин мына Мя.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 Вой фаче сэ ынчетезе тоатэ букурия ей, сэрбэториле ей, луниле ей челе ной, сабателе ей ши тоате празничеле ей.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 Ый вой пустии ши вииле ши смокиний, деспре каре зичя: ‘Ачаста есте плата пе каре мь-ау дат-о ибовничий мей!’ Ле вой префаче ынтр-о пэдуре ши ле вор мынка фяреле кымпулуй.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 О вой педепси пентру зилеле кынд тэмыя баалилор, кынд се гэтя ку верига де нас, ку салба ей, ши алерга дупэ ибовничий ей, уйтынд де Мине”, зиче Домнул.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 „Де ачея, ятэ, о вой адемени ши о вой дуче ын пустиу ши-й вой ворби пе плакул инимий ей.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Аколо, ый вой да ярэшь вииле ши валя Акор й-о вой префаче ынтр-о ушэ де нэдежде ши аколо ва кынта ка ын время тинереций е ши ка ын зиуа кынд с-а суит дин цара Еӂиптулуй.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 Ын зиуа ачея”, зиче Домнул, „Ымь вей зиче: ‘Бэрбатул меу’ ши ну-Мь вей май зиче: ‘Стэпынул меу’.
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Вой скоате дин гура ей нумеле баалилор, ка сэ ну май фие помениць пе нуме.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 Ын зиуа ачея, вой ынкея пентру ей ун легэмынт ку фяреле кымпулуй, ку пэсэриле черулуй ши ку тырытоареле пэмынтулуй, вой сфэрыма дин царэ аркул, сабия ши орьче унялтэ де рэзбой ши-й вой фаче сэ локуяскэ ын линиште.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 Те вой логоди ку Мине пентру тотдяуна; те вой логоди ку Мине прин неприхэнире, жудекатэ, маре бунэтате ши ындураре;
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 те вой логоди ку Мине прин крединчошие ши вей куноаште пе Домнул!
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 Ын зиуа ачея, вой аскулта, зиче Домнул, вой аскулта черуриле, ши еле вор аскулта пэмынтул;
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 пэмынтул ва аскулта грыул, мустул ши унтделемнул, ши ачестя вор аскулта пе Изреел.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Ымь вой сэди пе Ло-Рухама ын царэ ши-й вой да ындураре; вой зиче луй Ло-Ами: ‘Ту ешть попорул Меу!’ Ши ел ва рэспунде: ‘Думнезеул меу!’”
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Осея 2 >