< Осея 10 >
1 Исраел ера о вие мэноасэ, каре фэчя мулте роаде. Ку кыт роаделе сале ерау май мулте, ку атыт май мулте алтаре а зидит; ку кыт ый пропэшя цара, ку атыт ынфрумусеца стылпий идолешть.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Инима лор есте ымпэрцитэ, де ачея вор фи педепсиць. Домнул ле ва сурпа алтареле, ле ва нимичи стылпий идолешть.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 Ши курынд вор зиче: „Н-авем ун адевэрат ымпэрат, кэч ну не-ам темут де Домнул, ши ымпэратул пе каре-л авем че ар путя фаче ел пентру ной?”
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 Ей ростеск ворбе дешарте, журэминте минчиноасе кынд ынкее ун легэмынт, де ачея педяпса ва ынколци ка о буруянэ отрэвитоаре дин бразделе кымпией!
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 Локуиторий Самарией се вор уйми де вицеий дин Бет-Авен; попорул ва жели пе идол ши преоций луй вор тремура пентру ел, пентру слава луй каре ва пери дин мижлокул лор.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 Да, ел ынсушь ва фи дус ын Асирия ка дар ымпэратулуй Иареб. Рушиня ва купринде пе Ефраим ши луй Исраел ый ва фи рушине де плануриле сале.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 С-ау дус Самария ши ымпэратул ей, ка о цэплигэ пе фаца апелор.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 Ынэлцимиле дин Бет-Авен, унде а пэкэтуит Исраел, вор фи нимичите; спинь ши мэрэчинь вор креште пе алтареле лор. Ши вор зиче мунцилор: „Акоперици-не!” ши дялурилор: „Кэдець песте ной!”
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 „Дин зилеле Гибеей ай пэкэтуит, Исраеле! Аколо ау стат ей, пентру ка рэзбоюл фэкут ымпотрива челор рэй сэ ну-й апуче ла Гибея.
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Ый вой педепси кынд вой вря ши се вор стрынӂе попоаре ымпотрива лор кынд ый вой педепси пентру ындоита лор нелеӂюире!
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Ефраим есте о мынзатэ ынвэцатэ ла жуг, кэрея ый плаче сэ треере грыул ши й-ам круцат гытул сэу чел фрумос, дар акум вой ынжуга пе Ефраим, Иуда ва ара ши Иаков ый ва грэпа.”
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Семэнаць потривит ку неприхэниря, ши вець сечера потривит ку ындураря. Десцеленици-вэ ун огор ноу! Есте время сэ кэутаць пе Домнул, ка сэ винэ ши сэ вэ плоуэ мынтуире.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 Аць арат рэул, аць сечерат нелеӂюиря ши аць мынкат родул минчуний. Кэч те-ай ынкрезут ын кареле тале де луптэ, ын нумэрул оаменилор тэй витежь.
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 Де ачея се ва стырни о зарвэ ымпотрива попорулуй тэу ши тоате четэцуиле тале вор фи нимичите, кум а нимичит ын луптэ Шалман-Бет-Арбел, кынд мама а фост здробитэ ымпреунэ ку копиий ей.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Ятэ че вэ ва адуче Бетел дин причина рэутэций воастре песте мэсурэ де марь. Ын ревэрсатул зорилор, се ва испрэви ку ымпэратул луй Исраел!
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.