< ХАБАКУК 2 >

1 М-ам дус ла локул меу де стражэ ши стэтям пе турн ка сэ вегез ши сэ вэд че аре сэ-мь спунэ Домнул ши че-мь ва рэспунде ла плынӂеря мя.
Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
2 Домнул мь-а рэспунс ши а зис: „Скрие пророчия ши сап-о пе табле, ка сэ се поатэ чити ушор!
Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
3 Кэч есте о пророчие а кэрей време есте хотэрытэ, се апропие де ымплинире ши ну ва минци; дакэ зэбовеште, аштяпт-о, кэч ва вени ши се ва ымплини негрешит.
Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
4 Ятэ, и с-а ынгымфат суфлетул, ну есте фэрэ приханэ ын ел, дар чел неприхэнит ва трэи прин крединца луй.
“Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
5 Ка ши чел бят ши семец, чел мындру ну стэ лиништит, чи ышь лэрӂеште гура ка Локуинца морцилор, есте несэциос ка моартя, аша кэ пе тоате нямуриле вря сэ ле стрынгэ ла ел ши тоате попоареле ле траӂе ла ел. (Sheol h7585)
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
6 Ну ва фи ел де батжокура тутурор ачестора, де рыс ши де поминэ? Се ва зиче: ‘Вай де чел че адунэ че ну есте ал луй! Пынэ кынд се ва ымповэра ку даторий?’
“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
7 Ну се вор ридика деодатэ чей че те-ау ымпрумутат? Ну се вор трези асуприторий тэй ши вей ажунӂе прада лор?
Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
8 Фииндкэ ай жефуит мулте нямурь, тоатэ рэмэшица попоарелор те ва жефуи дин причина вэрсэрий сынӂелуй оаменилор, дин причина силничиилор фэкуте ын царэ, ымпотрива четэций ши ымпотрива тутурор локуиторилор ей.
Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
9 Вай де чел че стрынӂе кыштигурь нелеӂюите пентру каса луй, ка сэ-шь ашезе апой куйбул ынтр-ун лок ыналт ши сэ скапе дин мына ненорочирий!
“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
10 Рушиня касей тале ць-ай кроит нимичинд о мулциме де попоаре ши ымпотрива та ынсуць ай пэкэтуит.
Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
11 Кэч пятра дин мижлокул зидулуй стригэ ши лемнул каре лягэ гринда ый рэспунде.
Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
12 Вай де чел че зидеште о четате ку сынӂе, каре ынтемеязэ о четате ку нелеӂюире!
“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
13 Ятэ, кынд Домнул оштирилор а хотэрыт лукрул ачеста, попоареле се остенеск пентру фок ши нямуриле се трудеск деӂяба.
Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
14 Кэч пэмынтул ва фи плин де куноштинца славей Домнулуй, ка фундул мэрий де апеле каре-л акоперэ.
Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
15 Вай де чел че дэ апроапелуй сэу сэ бя, вай де тине, каре ый торнь бэутурэ спумоасэ ши-л амецешть, ка сэ-й везь голичуня!
“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
16 Те вей сэтура де рушине, ын лок де славэ; бя ши ту ши дезвелеште-те! Ыць ва вени ши цие рындул сэ ей пахарул дин дряпта Домнулуй ши ва вени рушиня песте слава та.
Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
17 Кэч силничииле фэкуте ымпотрива Либанулуй вор кэдя асупра та ши пустиириле фярелор те вор ынгрози, пентру вэрсаря сынӂелуй оаменилор ши силничииле фэкуте ын царэ, ымпотрива четэций ши ымпотрива тутурор локуиторилор ей.
Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
18 Ла че ар путя фолоси ун кип чоплит, пе каре-л чоплеште лукрэторул? Ла че ар путя фолоси ун кип турнат, каре ынвацэ пе оамень минчунь, пентру ка лукрэторул каре л-а фэкут сэ-шь пунэ ынкредеря ын ел, пе кынд ел фэуреште нумай ниште идоль муць?
“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
19 Вай де чел че зиче лемнулуй: ‘Скоалэ-те!’ ши уней петре муте: ‘Трезеште-те!’ Поате еа сэ дя ынвэцэтурэ? Ятэ кэ есте ымподобитэ ку аур ши арӂинт, дар ын еа ну есте ун дух каре с-о ынсуфлецяскэ.
Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
20 Домнул ынсэ есте ын Темплул Луй чел сфынт. Тот пэмынтул сэ такэ ынаинтя Луй!”
Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

< ХАБАКУК 2 >