< ХАБАКУК 1 >

1 Пророчия дескоперитэ пророкулуй Хабакук.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Пынэ кынд вой стрига кэтре Тине, Доамне, фэрэ с-аскулць? Пынэ кынд мэ вой тынгуи Цие, фэрэ сэ дай ажутор?
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Пентру че мэ лашь сэ вэд нелеӂюиря ши Те уйць ла недрептате? Асуприря ши силничия се фак суб окий мей, се наск чертурь ши се стырнеште гылчавэ.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Де ачея леӂя есте фэрэ путере ши дрептатя ну се веде, кэч чел рэу бируе пе чел неприхэнит, де ачея се фак жудекэць недрепте.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 „Арункаци-вэ окий принтре нямурь ши привиць, уймици-вэ ши ынгрозици-вэ! Кэч ын зилеле воастре вой фаче о лукраре пе каре н-аць креде-о, дакэ в-ар повести-о чинева!
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Ятэ, вой ридика пе халдеень – попор турбат ши юте, каре стрэбате ынтиндерь марь де цэрь, ка сэ пунэ мына пе локуинце каре ну сунт але луй.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Ел есте грозав ши ынфрикошат; нумай дин ел ынсушь ый ес дрептул ши мэриря луй.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Каий луй сунт май юць декыт леопарзий, май спринтень декыт лупий де сярэ, ши кэлэреций луй ынаинтязэ ын галоп де департе, збоарэ ка вултурул каре се репеде асупра прэзий.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 Тот попорул ачеста вине нумай ка сэ жефуяскэ; привириле луй лакоме каутэ ынаинте ши стрынӂе приншь де рэзбой ка нисипул.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 Ышь бате жок де ымпэраць, ши воевозий сунт о нимика пентру ел, рыде де тоате ынтэритуриле, кэч ынгрэмэдеште пэмынт ши ле я.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Апой априндеря и се ындоеште, ынтрече мэсура ши се фаче виноват, кэч путеря луй о я ка думнезеу ал луй!”
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Доамне, ну ешть Ту дин вешничие Думнезеул меу, Сфынтул меу? Ну вом мури! Доамне, Ту ай ридикат пе попорул ачеста ка сэ-Ць ымплинешть жудекэциле Тале; Ту, Стынка мя, л-ай ридикат ка сэ дай прин ел педепселе Тале!
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Окий Тэй сунт аша де кураць кэ ну пот сэ вадэ рэул ши ну поць сэ привешть нелеӂюиря! Кум ай путя приви Ту пе чей мишей ши сэ тачь кынд чел рэу мэнынкэ пе чел май неприхэнит декыт ел?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Вей фаче Ту омулуй ка пештилор мэрий, ка тырытоарей, каре н-аре стэпын?
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Ел ый скоате пе тоць ку ундица, ый траӂе ын мряжа са, ый стрынӂе ын нэводул сэу. Де ачея се букурэ ши се веселеште.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Де ачея адуче жертфе мрежей сале, адуче тэмые нэводулуй сэу, кэч лор ле даторязэ партя луй чя грасэ ши букателе луй густоасе!
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Пентру ачаста ышь ва голи ел ынтруна мряжа ши ва ынжунгия фэрэ милэ пе нямурь?
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< ХАБАКУК 1 >