< Галатень 1 >
1 Павел, апостол ну де ла оамень, нич принтр-ун ом, чи прин Исус Христос ши прин Думнезеу Татэл, каре Л-а ынвият дин морць,
Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
2 ши тоць фраций каре сунт ымпреунэ ку мине, кэтре Бисеричиле Галатией:
pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 Хар ши паче воуэ де ла Думнезеу Татэл ши де ла Домнул ностру Исус Христос!
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
4 Ел С-а дат пе Сине Ынсушь пентру пэкателе ноастре ка сэ не смулгэ дин ачест вяк рэу, дупэ воя Думнезеулуй ностру ши Татэл. (aiōn )
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn )
5 А Луй сэ фие слава ын вечий вечилор! Амин. (aiōn )
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
6 Мэ мир кэ тречець аша де репеде де ла Чел че в-а кемат прин харул луй Христос ла о алтэ евангелие.
Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
7 Ну доар кэ есте о алтэ евангелие, дар сунт уний оамень каре вэ тулбурэ ши воеск сэ рэстоарне Евангелия луй Христос.
umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
8 Дар кяр дакэ ной ыншине сау ун ынӂер дин чер ар вени сэ вэ проповэдуяскэ о евангелие деосебитэ де ачея пе каре в-ам проповэдуит-о ной, сэ фие анатема!
Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
9 Кум ам май спус, о спун ши акум: Дакэ вэ проповэдуеште чинева о евангелие деосебитэ де ачея пе каре аць примит-о, сэ фие анатема!
Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
10 Каут еу оаре, ын клипа ачаста, сэ капэт бунэвоинца оаменилор сау бунэвоинца луй Думнезеу? Сау каут сэ плак оаменилор? Дакэ аш май кэута сэ плак оаменилор, н-аш фи робул луй Христос.
Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
11 Фрацилор, вэ мэртурисеск кэ Евангелия проповэдуитэ де мине ну есте де обыршие оменяскэ,
Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
12 пентру кэ н-ам примит-о, нич н-ам ынвэцат-о де ла вреун ом, чи прин дескопериря луй Исус Христос.
Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
13 Аць аузит, ын адевэр, каре ера пуртаря мя де алтэдатэ, ын релиӂия иудеилор. Кум, адикэ, пригоням песте мэсурэ де мулт Бисерика луй Думнезеу ши фэчям прэпэд ын еа
Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
14 ши кум ерам май ынаинтат ын релиӂия иудеилор декыт мулць дин нямул меу де о вырстэ ку мине. Ерам ынсуфлецит де о рывнэ неспус де маре пентру датиниле стрэмошешть.
Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
15 Дар, кынд Думнезеу, каре м-а пус деопарте дин пынтечеле майчий меле ши м-а кемат прин харул Сэу, а гэсит ку кале
Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
16 сэ дескопере ын мине пе Фиул Сэу, ка сэ-Л вестеск ынтре нямурь, ындатэ, н-ам ынтребат пе ничун ом,
kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 нич ну м-ам суит ла Иерусалим, ла чей че ау фост апостоль ынаинте де мине, чи м-ам дус ын Арабия. Апой м-ам ынторс дин ноу ла Дамаск.
Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
18 Дупэ трей ань, м-ам суит ла Иерусалим сэ фак куноштинцэ ку Кифа ши ам рэмас ла ел чинчспрезече зиле.
Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
19 Дар н-ам вэзут пе ничунул алтул динтре апостоль декыт пе Иаков, фрателе Домнулуй.
Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
20 Ын челе че вэ скриу, ятэ, ынаинтя луй Думнезеу, ну минт.
Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
21 Дупэ ачея м-ам дус ын цинутуриле Сирией ши Чиличией.
Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
22 Ши ерам ынкэ некуноскут ла фацэ Бисеричилор луй Христос, каре сунт ын Иудея.
Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
23 Еле аузяу доар спунынду-се: „Чел че не пригоня одиниоарэ акум проповэдуеште крединца, пе каре кэута с-о нимичяскэ одиниоарэ.”
Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
24 Ши слэвяу пе Думнезеу дин причина мя.
Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.