< Езекиел 38 >

1 Кувынтул Домнулуй мь-а ворбит астфел:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 „Фиул омулуй, ынтоарче-те ку фаца спре Гог, дин цара луй Магог, спре домнул Рошулуй, Мешекулуй ши Тубалулуй, ши пророчеште ымпотрива луй!
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 Ши спуне: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Ятэ, ам неказ пе тине, Гог, домнул Рошулуй, Мешекулуй ши Тубалулуй!
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Те вой тыры ши-ць вой пуне ун кырлиг ын фэлчь; те вой скоате, пе тине ши тоатэ оастя та, кай ши кэлэрець, тоць ымбрэкаць ын кип стрэлучит, чатэ маре де попор, каре поартэ скут ши павэзэ ши каре тоць мынуеск сабия;
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 ымпреунэ ку ей вой скоате пе чей дин Персия, Етиопия ши Пут, тоць ку скут ши койф,
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Гомерул ку тоате оштиле луй, цара Тогармей, дин фундул мязэнопций, ку тоате оштиле сале, попоаре мулте ымпреунэ ку тине!
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Прегэтеште-те дар, фий гата, ту ши тоатэ мулцимя адунатэ ын журул тэу! Фий кэпетения лор!
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Дупэ мулте зиле, вей фи ын фрунтя лор; ын время де апой, вей мерӂе ымпотрива цэрий, ай кэрей локуиторь, скэпаць де сабие, вор фи стрыншь динтре май мулте попоаре пе мунций луй Исраел, каре мултэ време фусесерэ пустий, дар, фиинд скошь дин мижлокул попоарелор, вор фи лиништиць ын локуинцеле лор.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 Яр ту те вей суи, вей ынаинта ка о фуртунэ, вей фи ка ун нор негру каре ва акопери цара, ту ку тоате оштиле тале ши мулте попоаре ку тине.»
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Ын зиуа ачея, мулте гындурь ыць вор вени ын минте ши вей урзи планурь реле.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 Вей зиче: ‹Мэ вой суи ымпотрива цэрий ачестея дескисе, вой нэвэли песте оамений ачештя лиништиць, каре стау фэрэ грижь ын локуинцеле лор, тоць ын локуинце фэрэ зидурь ши неавынд нич зэвоаре, нич порць!
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Мэ вой дуче сэ яу прадэ ши сэ мэ дедау ла жаф, сэ пун мына пе ачесте дэрымэтурь локуите дин ноу, пе попорул ачеста стрынс дин мижлокул нямурилор, каре аре турме ши моший ши локуеште ын мижлокул пэмынтулуй.›
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Себа ши Дедан, негусторий дин Тарс ши тоць пуий лор де лей ыць вор зиче: ‹Вий сэ ей прадэ? Пентру жаф ць-ай адунат оаре мулцимя та, ка сэ ей арӂинт ши аур, ка сэ ей турме ши авуций ши сэ фачь о прадэ маре?›»’
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Де ачея, пророчеште, фиул омулуй, ши спуне луй Гог: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Да, ын зиуа кынд попорул Меу Исраел ва трэи ын линиште, вей порни дин цара та
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 ши вей вени дин фундул мязэнопций, ту ши мулте попоаре ку тине, тоць кэлэрь пе кай, о маре мулциме ши о путерникэ оштире!
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 Вей ынаинта ымпотрива попорулуй Меу Исраел ка ун нор каре ва акопери цара. Ын зилеле де апой, те вой адуче ымпотрива цэрий Меле, ка сэ Мэ куноаскэ нямуриле кынд вой фи сфинцит ын тине суб окий лор, Гог!»
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Ну ешть ту ачела деспре каре ам ворбит одиниоарэ, прин робий Мей, пророчий луй Исраел, каре ау пророчит атунч ань де зиле кэ те вой адуче ымпотрива лор?
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Ын зиуа ачея ынсэ, ын зиуа кынд ва порни Гог ымпотрива пэмынтулуй луй Исраел», зиче Домнул Думнезеу, «Ми се ва суи ын нэрь мыния апринсэ.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 О спун ын ӂелозия ши ын фокул мынией Меле: ‹Ын зиуа ачея, ва фи ун маре кутремур ын цара луй Исраел.
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 Пештий мэрий ши пэсэриле черулуй вор тремура де Мине ши фяреле кымпулуй ши тоате тырытоареле каре се тырэск пе пэмынт ши тоць оамений каре сунт пе фаца пэмынтулуй; мунций се вор рэстурна, переций стынчилор се вор прэбуши ши тоате зидуриле вор кэдя ла пэмынт.›
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Атунч вой кема гроаза ымпотрива луй пе тоць мунций Мей», зиче Домнул Думнезеу; «сабия фиекэруя се ва ынтоарче ымпотрива фрателуй сэу.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 Ыл вой жудека прин чумэ ши сынӂе, принтр-о плоае нэпрасникэ ши прин петре де гриндинэ; вой плоуа фок ши пучоасэ песте ел, песте оштиле луй ши песте попоареле челе мулте каре вор фи ку ел.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Ымь вой арэта астфел мэримя ши сфинцения, Мэ вой фаче куноскут ынаинтя мулцимий нямурилор ши вор шти кэ Еу сунт Домнул.»’
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Езекиел 38 >