< Езекиел 33 >

1 Кувынтул Домнулуй мь-а ворбит астфел:
Yehova anandiyankhula nati:
2 „Фиул омулуй, ворбеште копиилор попорулуй тэу ши спуне-ле: ‘Кынд вой адуче сабия песте врео царэ, ши попорул цэрий ва луа дин мижлокул луй пе ун ом оарекаре ши-л ва пуне ка стрэжер,
“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
3 дакэ омул ачела ва ведя венинд сабия асупра цэрий, ва суна дин трымбицэ ши ва да де штире попорулуй
Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
4 ши дакэ чел че ва аузи сунетул трымбицей ну се ва фери ши ва вени сабия ши-л ва принде, сынӂеле луй сэ кадэ асупра капулуй луй.
Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
5 Фииндкэ а аузит сунетул трымбицей ши ну с-а ферит, де ачея сынӂеле луй сэ кадэ асупра луй, дар, дакэ се ва фери, ышь ва скэпа вяца.
Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
6 Дакэ ынсэ стрэжерул ва ведя венинд сабия ши ну ва суна дин трымбицэ ши дакэ попорул ну ва фи ынштиинцат ши ва вени сабия ши ва рэпи вяца вреунуй ом, омул ачела ва пери дин причина нелеӂюирий луй, дар вой чере сынӂеле луй дин мына стрэжерулуй.’
Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
7 Акум, фиул омулуй, те-ам пус стрэжер песте каса луй Исраел. Ту требуе сэ аскулць кувынтул каре есе дин гура Мя ши сэ-й ынштиинцезь дин партя Мя.
“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
8 Кынд зик челуй рэу: ‘Рэуле, вей мури негрешит!’ ши ту ну-й спуй ка сэ-л ынторчь де ла каля луй чя ря, рэул ачела ва мури ын нелеӂюиря луй, дар сынӂеле луй ыл вой чере дин мына та.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
9 Дар, дакэ вей ынштиинца пе чел рэу, ка сэ се ынтоаркэ де ла каля луй, ши ел ну се ва ынтоарче, ва мури ын нелеӂюиря луй, дар ту ыць вей мынтуи суфлетул.
Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
10 Спуне дар, фиул омулуй, касей луй Исраел: ‘Вой ку дрепт кувынт зичець: «Фэрэделеӂиле ши пэкателе ноастре сунт асупра ноастрэ ши дин причина лор тынжим – кум ам путя сэ трэим?»’
“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
11 Спуне-ле: ‘Пе вяца Мя’, зиче Домнул Думнезеу, ‘кэ ну дореск моартя пэкэтосулуй, чи сэ се ынтоаркэ де ла каля луй ши сэ трэяскэ. Ынтоарчеци-вэ, ынтоарчеци-вэ де ла каля воастрэ чя ря! Пентру че врець сэ муриць, вой, каса луй Исраел?’
Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
12 Ши ту, фиул омулуй, спуне копиилор попорулуй тэу: ‘Неприхэниря челуй неприхэнит ну-л ва мынтуи ын зиуа фэрэделеӂий луй ши чел рэу ну ва кэдя ловит де рэутатя луй ын зиуа кынд се ва ынтоарче де ла еа, дупэ кум нич чел неприхэнит ну ва путя сэ трэяскэ прин неприхэниря луй ын зиуа кынд ва сэвырши о фэрэделеӂе.’
“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
13 Кынд зик челуй неприхэнит кэ ва трэи негрешит, дакэ се ынкреде ын неприхэниря луй ши сэвыршеште нелеӂюиря, атунч тоатэ неприхэниря луй се ва уйта ши ел ва мури дин причина нелеӂюирий пе каре а сэвыршит-о.
Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
14 Димпотривэ, кынд зик челуй рэу: ‘Вей мури!’, дакэ се ынтоарче де ла пэкатул луй ши фаче че есте бине ши плэкут,
Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
15 дакэ дэ ынапой зэлогул, ынтоарче че а рэпит, урмязэ ынвэцэтуриле каре дау вяца ши ну сэвыршеште ничо нелеӂюире, ва трэи негрешит ши ну ва мури.
monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
16 Тоате пэкателе пе каре ле-а сэвыршит се вор уйта; а фэкут че есте бине ши плэкут, ши ва трэи негрешит!
Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
17 Копиий попорулуй тэу зик: ‘Каля Домнулуй ну есте дряптэ!’ Тотушь май деграбэ каля лор ну есте дряптэ!
“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
18 Дакэ чел неприхэнит се абате де ла неприхэниря луй ши сэвыршеште нелеӂюиря, требуе сэ моарэ дин причина ачаста.
Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
19 Дар, дакэ чел рэу се ынтоарче де ла рэутатя луй ши фаче че есте бине ши плэкут, ва трэи токмай дин причина ачаста!
Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
20 Фииндкэ зичець: ‘Каля Домнулуй ну есте дряптэ!’, вэ вой жудека пе фиекаре дупэ умблетеле луй, каса луй Исраел!”
Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
21 Ын ал дойспрезечеля ан, ын зиуа а чинчя а луний а зечя а робией ноастре, ун ом каре скэпасе дин Иерусалим а венит ла мине ши а зис: „Четатя а фост луатэ!”
Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
22 Дар мына Домнулуй венисе песте мине сяра, ынаинте де вениря фугарулуй ла мине, ши Домнул ымь дескисесе гура пынэ а венит ел ла мине диминяца. Гура ымь ера дескисэ ши ну май ерам мут.
Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
23 Атунч, кувынтул Домнулуй мь-а ворбит астфел:
Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
24 „Фиул омулуй, чей че локуеск ын дэрымэтуриле ачеля ын цара луй Исраел зик: ‘Авраам ера сингур, ши тот а моштенит цара; дар ной сунтем мулць ши цара не-а фост датэ ын стэпынире!’
“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
25 Де ачея спуне-ле: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Вой мынкаць карне ку сынӂе, вэ ридикаць окий спре идолий воштри ши вэрсаць сынӂе. Ши вой сэ стэпыниць цара?
Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
26 Вой вэ бизуиць пе сабия воастрэ, сэвыршиць урычунь, фиекаре дин вой нечинстеште пе неваста апроапелуй сэу. Ши вой сэ стэпыниць цара?»’
Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
27 Де ачея спуне-ле: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Пе вяца Мя кэ чей че локуеск ын ачесте дэрымэтурь вор кэдя учишь де сабие, пе чей че сунт пе кымп ый вой да де мынкаре фярелор, яр чей че сунт ын ынтэритурь ши ын пештерь вор мури де чумэ.
“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
28 Вой префаче цара ынтр-о пустиетате ши ынтр-ун пустиу; мындрия тэрией ей се ва сфырши, мунций луй Исраел вор фи пустииць ши нимень ну ва май трече прин ей.
Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
29 Ши вор шти кэ Еу сунт Домнул кынд вой префаче цара ынтр-о пустиетате ши ынтр-ун пустиу дин причина тутурор урычунилор пе каре ле-ау сэвыршит.»’
Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
30 Фиул омулуй, копиий попорулуй тэу ворбеск де тине пе лынгэ зидурь ши пе ла ушиле каселор ши зик унул алтуя, фиекаре фрателуй сэу: ‘Вениць дар ши аскултаць каре есте кувынтул ешит де ла Домнул!’
“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
31 Ши вин ку грэмада ла тине, стау ынаинтя та ка попор ал Меу, аскултэ кувинтеле тале, дар ну ле ымплинеск, кэч ку гура ворбеск дулче де тот, дар ку инима умблэ тот дупэ пофтеле лор.
Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
32 Ятэ кэ ту ешть пентру ей ка ун кынтэрец плэкут, ку ун глас фрумос ши искусит ла кынтаре пе коарде. Ей ыць аскултэ кувинтеле, дар ну ле ымплинеск делок.
Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
33 Кынд се вор ынтымпла ынсэ ачесте лукрурь – ши ятэ кэ се ынтымплэ! – вор шти кэ ера ун пророк ын мижлокул лор.”
“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

< Езекиел 33 >