< Еклезиастул 2 >

1 Ам зис инимий меле: „Хайде! Вряу сэ те ынчерк ку веселие ши густэ феричиря.” Дар ятэ кэ ши ачаста есте о дешертэчуне.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake.
2 Ам зис рысулуй: „Ешть о небуние!” ши веселией: „Че те ыншель деӂяба?”
“Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?”
3 Ам хотэрыт ын инима мя сэ-мь веселеск трупул ку вин, ын тимп че инима мэ ва кырмуи ку ынцелепчуне, ши сэ стэруеск астфел ын небуние пынэ вой ведя че есте бине сэ факэ фиий оаменилор суб черурь, ын тот тимпул веций лор.
Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.
4 Ам фэкут лукрурь марь: мь-ам зидит касе, мь-ам сэдит вий,
Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa.
5 мь-ам фэкут грэдинь ши ливезь де помь ши ам сэдит ын еле тот фелул де помь родиторь.
Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse.
6 Мь-ам фэкут язурь ка сэ уд думбрава унде креск копачий.
Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija.
7 Ам кумпэрат робь ши роабе ши ам авут копий де касэ; ам авут чирезь де бой ши турме де ой май мулт декыт тоць чей че фусесерэ ынаинте де мине ын Иерусалим.
Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe.
8 Мь-ам стрынс арӂинт ши аур, ши богэций ка де ымпэраць ши цэрь. Мь-ам адус кынтэрець ши кынтэреце ши десфэтаря фиилор оаменилор: о мулциме де фемей.
Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu.
9 Ам ажунс маре, май маре декыт тоць чей че ерау ынаинтя мя ын Иерусалим. Мь-ам пэстрат кяр ынцелепчуня.
Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.
10 Тот че мь-ау пофтит окий ле-ам дат; ну мь-ам оприт инима де ла ничо веселие, чи ам лэсат-о сэ се букуре де тоатэ труда мя, ши ачаста мь-а фост партя дин тоатэ остеняла мя.
Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna; mtima wanga sindinawumane zokondweretsa. Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse, ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.
11 Апой, кынд м-ам уйтат ку бэгаре де сямэ ла тоате лукрэриле пе каре ле фэкусем ку мыниле меле ши ла труда ку каре ле фэкусем, ам вэзут кэ ын тоате есте нумай дешертэчуне ши гоанэ дупэ вынт ши кэ ну есте нимик трайник суб соаре.
Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga, ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze, zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe, palibe chomwe ndinapindula pansi pano.
12 Атунч мь-ам ынторс привириле спре ынцелепчуне, простие ши небуние. – Кэч че ва фаче омул каре ва вени дупэ ымпэрат? Чея че с-а фэкут ши май ынаинте. –
Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani, komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani. Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani choposa chimene chinachitidwa kale?
13 Ши ам вэзут кэ ынцелепчуня есте ку атыт май де фолос декыт небуния, ку кыт есте май де фолос лумина декыт ынтунерикул.
Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru, monga momwe kuwala kumapambanira mdima.
14 Ынцелептул ышь аре окий ын кап, яр небунул умблэ ын ынтунерик. Дар ам бэгат де сямэ кэ ши унул, ши алтул ау ачеяшь соартэ.
Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo, pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli; koma ndinazindikira kuti chomwe chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.
15 Ши ам зис ын инима мя: „Дакэ ши еу вой авя ачеяшь соартэ ка небунул, атунч пентру че ам фост май ынцелепт?” Ши ам зис ын инима мя: „Ши ачаста есте о дешертэчуне.”
Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga, “Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine. Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?” Ndinati mu mtima mwanga, “Ichinso ndi chopandapake.”
16 Кэч помениря ынцелептулуй ну есте май вешникэ декыт а небунулуй: кяр ын зилеле урмэтоаре, тотул есте уйтат. Ши апой ши ынцелептул моаре, ши небунул!
Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali; mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika. Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!
17 Атунч ам урыт вяца, кэч ну мь-а плэкут че се фаче суб соаре: тотул есте дешертэчуне ши гоанэ дупэ вынт.
Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
18 Мь-ам урыт пынэ ши тоатэ мунка пе каре ам фэкут-о суб соаре, мункэ пе каре о лас омулуй каре вине дупэ мине, ка сэ се букуре де еа.
Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga.
19 Ши чине штие дакэ ва фи ынцелепт сау небун? Ши тотушь ел ва фи стэпын пе тоатэ мунка мя, пе каре ам агонисит-о ку трудэ ши ынцелепчуне суб соаре. Ши ачаста есте о дешертэчуне.
Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake.
20 Ам ажунс пынэ аколо кэ м-а апукат о маре дезнэдежде де тоатэ мунка пе каре ам фэкут-о суб соаре.
Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano.
21 Кэч есте кыте ун ом каре а мунчит ку ынцелепчуне, ку причепере ши ку избындэ, ши ласэ родул мунчий луй унуй ом каре ну с-а остенит делок ку еа. Ши ачаста есте о дешертэчуне ши ун маре рэу.
Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu.
22 Кэч, дрепт ворбинд, че фолос аре омул дин тоатэ мунка луй ши дин тоатэ стрэдуинца инимий луй, ку каре се трудеште суб соаре?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano?
23 Тоате зилеле луй сунт плине де дурере, ши труда луй ну есте декыт неказ: нич мэкар ноаптя н-аре одихнэ инима луй. Ши ачаста есте о дешертэчуне.
Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.
24 Ну есте алтэ феричире пентру ом декыт сэ мэнынче ши сэ бя ши сэ-шь ынвеселяскэ суфлетул ку че есте бун дин агонисяла луй! Дар ам вэзут кэ ши ачаста вине дин мына луй Думнезеу.
Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu,
25 Чине, ын адевэр, поате сэ мэнынче ши сэ се букуре фэрэ Ел?
pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo?
26 Кэч Ел дэ омулуй плэкут Луй ынцелепчуне, штиинцэ ши букурие, дар челуй пэкэтос ый дэ грижа сэ стрынгэ ши с-адуне, ка сэ дя челуй плэкут луй Думнезеу! Ши ачаста есте о дешертэчуне ши гоанэ дупэ вынт.
Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

< Еклезиастул 2 >