< Даниел 11 >
1 Ын анул динтый ал луй Дариус Медул, ерам ши еу ла ел, ка сэ-л ажут ши сэ-л сприжин.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 Акум, ыць вой фаче куноскут адевэрул: Ятэ кэ вор май фи ынкэ трей ымпэраць ын Персия. Чел де-ал патруля ва стрынӂе май мултэ богэцие декыт тоць чейлалць ши, кынд се ва симци путерник прин богэцииле луй, ва рэскула тотул ымпотрива ымпэрэцией Гречией.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Дар се ва ридика ун ымпэрат витяз, каре ва стэпыни ку о маре путере ши ва фаче че ва вои.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 Ши, кум се ва ынтэри, аша се ва ши сфэрыма ымпэрэция луй ши ва фи ымпэрцитэ ын челе патру вынтурь але черурилор, дар ну ынтре урмаший луй ши нич ну ва фи тот атыт де путерникэ пе кыт ера суб ел, кэч ва фи фэкутэ букэцеле ши ва трече ла алций, афарэ де ачештя.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 Ымпэратул де ла мязэзи ва ажунӂе таре. Дар унул дин май-марий луй ва фи ши май таре декыт ел ши ва домни ынтемеинд о маре ымпэрэцие.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Дупэ кыцьва ань, се вор уни, ши фата ымпэратулуй де ла мязэзи ва вени ка невастэ ла ымпэратул де ла мязэноапте, ка сэ факэ о ынвоялэ. Дар ачесте мижлоаче де ажутораре ну вор авя ничо путере ши нич челелалте мижлоаче але ей ну вор путя цине пепт, чи еа ва фи датэ ла моарте ымпреунэ ку алаюл ей, ку татэл ей ши ку чел че с-а легат ку еа.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 Ын время ачея ынсэ се ва ридика ын локул ей ун лэстар дин ачеяшь рэдэчинэ ку еа ши ва вени ымпотрива оштирий Сирией, да, ва интра ын четэцуя ымпэратулуй де ла мязэноапте, ва фаче че ва вои ку еа ши ва фи бируитор.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Ва ридика ши ва стрэмута ын Еӂипт, одатэ ку принший де рэзбой, кяр ши пе думнезеий ши кипуриле лор турнате, ымпреунэ ку васеле лор скумпе де арӂинт ши де аур. Апой ва лэса кыцьва ань ын паче пе ымпэратул де ла мязэноапте.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Ачеста ва порни ымпотрива ымпэрэцией ымпэратулуй де ла мязэзи, дар се ва ынтоарче ярэшь ын цара са.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Тотушь фиий сэй вор ынчепе ярэшь рэзбоюл ши вор стрынӂе о маре мулциме де ошть, каре ва ынаинта, се ва ревэрса ка ун рыу каре есе дин маткэ ши-л вор ымпинӂе ярэшь ынапой пынэ ла четэцуе.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 Ымпэратул де ла мязэзи, мыният де ачаста, ва еши ши се ва лупта ку ымпэратул де ла мязэноапте; ва ридика о маре оштире, дар оштиле ымпэратулуй де ла мязэноапте вор фи дате ын мыниле луй ши нимичите.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 Атунч, инима ымпэратулуй се ва ынгымфа, ва доборы зече мий, дар тот ну ва бируи.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Кэч ымпэратул де ла мязэноапте се ва ынтоарче ши ва стрынӂе о оштире май маре декыт чя динтый ши, дупэ кытэва време, дупэ кыцьва ань, ва порни ын фрунтя уней марь оштирь бине ынармате.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 Ын время ачея, се вор ридика мулць ымпотрива ымпэратулуй де ла мязэзи, ши о чатэ де дербедей дин попорул тэу се вор рэскула, ка сэ ымплиняскэ ведения, дар вор кэдя.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Ымпэратул де ла мязэноапте ва ынаинта, ва ридика ынтэритурь ши ва пуне мына пе четэциле ынтэрите. Оштиле де ла мязэзи, нич кяр флоаря оаменилор ымпэратулуй ну вор путя сэ цинэ пепт, ну вор авя путере сэ се ымпотривяскэ.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 Чел че ва мерӂе ымпотрива луй ва фаче че ва вои ши нимень ну и се ва ымпотриви; ел се ва опри ын цара минунатэ, нимичинд ку десэвыршире тот че-й ва кэдя ын мынэ.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Ышь ва пуне де гынд сэ я ын стэпынире тоатэ ымпэрэция луй ши, фэкынду-се кэ аре гындурь курате ку ел, ый ва да пе фийкэ-са де невастэ ку гынд сэ-л пярдэ, дар лукрул ачеста ну се ва ынтымпла ши ну-й ва избынди.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Апой ышь ва ынтоарче привириле ынспре остроаве ши ва луа пе мулте дин еле, дар о кэпетение ва пуне капэт рушиний пе каре воя ел сэ й-о адукэ ши о ва ынтоарче асупра луй.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 Апой се ва ындрепта спре четэцуиле цэрий луй, дар се ва потикни, ва кэдя ши ну-л вор май гэси.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 Чел че-й ва луа локул ва адуче ун асупритор ын чя май фрумоасэ парте а ымпэрэцией, дар ын кытева зиле ва фи здробит, ши ануме ну прин мыние, нич прин рэзбой.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 Ын локул луй се ва ридика ун ом диспрецуит, фэрэ сэ айбэ путере ымпэрэтяскэ; дар се ва ридика деодатэ ши ва пуне мына пе ымпэрэцие прин унелтире.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Оштиле се вор ревэрса ка ун рыу ынаинтя луй, дар вор фи нимичите ымпреунэ ку о кэпетение а легэмынтулуй.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 Дупэ че се вор уни ку ел, ел ва ынтребуинца о викление; ва порни ши ва бируи ку пуцинэ луме.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 Ва интра пе неаштептате ын локуриле челе май родитоаре але цинутулуй; ва фаче че ну фэкусерэ нич пэринций луй, нич пэринций пэринцилор луй; ва ымпэрци прада, жафуриле ши богэцииле; ва урзи ла планурь ымпотрива четэцуилор, ши ачаста ва цине о време.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Апой ва порни ын фрунтя уней марь оштирь, ку путеря ши мыния луй, ымпотрива ымпэратулуй де ла мязэзи. Ши ымпэратул де ла мязэзи се ва принде ла рэзбой ку о оасте маре ши фоарте путерникэ, дар ну ва путя сэ цинэ пепт, кэч се вор урзи планурь реле ымпотрива луй.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Чей че вор мынка букате де ла маса луй ый вор адуче пеиря; оштиле луй се вор ымпрэштия ка ун рыу ши морций вор кэдя ын маре нумэр.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Чей дой ымпэраць ну вор кэута декыт сэ-шь факэ рэу унул алтуя, вор ста ла ачеяшь масэ ши вор ворби ку викление. Дар ну вор избути, кэч сфыршитул ну ва вени декыт ла время хотэрытэ.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Кынд се ва ынтоарче ын цара луй ку марь богэций, ын инима луй ва фи врэжмаш легэмынтулуй сфынт, ва лукра ымпотрива луй ши апой се ва ынтоарче ын цара луй.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 Ла о време хотэрытэ, ва порни дин ноу ымпотрива ымпэратулуй де ла мязэзи, дар, де дата ачаста, лукруриле ну вор май мерӂе ка май ынаинте.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Чи ниште корэбий дин Китим вор ынаинта ымпотрива луй, яр ел, дезнэдэждуит, се ва ынтоарче ынапой. Апой, мыниос ымпотрива легэмынтулуй сфынт, ну ва ста ку мыниле ын сын, чи, ла ынтоарчере, се ва ынцелеӂе ку чей че вор пэрэси легэмынтул сфынт.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 Ниште ошть тримисе де ел вор вени ши вор спурка Сфынтул Локаш, четэцуя, вор фаче сэ ынчетезе жертфа некурматэ ши вор ашеза урычуня пустииторулуй. Ва адемени прин лингуширь пе чей че руп легэмынтул.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 Дар ачея дин попор каре вор куноаште пе Думнезеул лор вор рэмыне тарь ши вор фаче марь испрэви.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 Ынцелепций попорулуй вор ынвэца пе мулць. Уний вор кэдя, пентру о време, ловиць де сабие ши де флакэрэ, де робие ши де жаф.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Кынд вор кэдя, вор фи ажутаць пуцин, ши мулць се вор уни ку ей дин фэцэрничие.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Кяр ши дин чей ынцелепць, мулць вор кэдя, ка сэ фие ынчеркаць, курэциць ши албиць пынэ ла время сфыршитулуй, кэч сфыршитул ну ва фи декыт ла время хотэрытэ.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 Ымпэратул ва фаче че ва вои; се ва ынэлца, се ва слэви май пресус де тоць думнезеий ши ва спуне лукрурь немайаузите ымпотрива Думнезеулуй думнезеилор ши ва пропэши пынэ ва трече мыния, кэч че есте хотэрыт се ва ымплини.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 Ну ва цине сямэ нич де думнезеий пэринцилор сэй, нич де доринца фемеилор; ку ун кувынт, ну ва цине сямэ де ничун думнезеу, чи се ва слэви пе сине май пресус де тоць.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Ын скимб, ва чинсти пе думнезеул четэцуилор; ачестуй думнезеу, пе каре ну-л куноштяу пэринций сэй, ый ва адуче чинсте ку аур ши арӂинт, ку петре скумпе ши лукрурь де прец.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Ку ажуторул ачестуй думнезеу стрэин ва лукра ымпотрива локурилор ынтэрите; куй ыл ва рекуноаште, ый ва да маре чинсте, ыл ва фаче сэ домняскэ песте мулць ши ле ва ымпэрци моший ка рэсплатэ.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 Ла время сфыршитулуй, ымпэратул де ла мязэзи се ва ымпунӂе ку ел. Ши ымпэратул де ла мязэноапте се ва нэпусти ка о фуртунэ песте ел, ку каре ши кэлэрець ши ку мулте корэбий; ва ынаинта асупра цэрилор луй, се ва ревэрса ка ун рыу ши ле ва ынека.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Ва интра ши ын цара чя минунатэ, ши зечь де мий вор кэдя. Дар Едомул, Моабул ши фрунташий копиилор луй Амон вор скэпа дин мына луй.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Ышь ва ынтинде мына песте фелурите цэрь ши нич цара Еӂиптулуй ну ва скэпа.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Чи се ва фаче стэпын пе вистиерииле де аур ши де арӂинт ши пе тоате лукруриле скумпе але Еӂиптулуй. Либиений ши етиопений вор вени ын алай дупэ ел.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Дар ниште звонурь вените де ла рэсэрит ши де ла мязэноапте ыл вор ынспэймынта ши атунч ва порни ку о маре мыние ка сэ прэпэдяскэ ши сэ нимичяскэ ку десэвыршире пе мулць.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 Ышь ва ынтинде кортуриле палатулуй сэу ынтре маре ши мунтеле чел слэвит ши сфынт. Апой ышь ва ажунӂе сфыршитул ши нимень ну-й ва фи ынтр-ажутор.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”