< Фаптеле 6 >

1 Ын зилеле ачеля, кынд с-а ынмулцит нумэрул ученичилор, евреий каре ворбяу гречеште кыртяу ымпотрива евреилор, пентру кэ вэдувеле лор ерау трекуте ку ведеря ла ымпэрцяла ажутоарелор де тоате зилеле.
Mʼmasiku amenewo pamene chiwerengero cha ophunzira chinkachuluka, Ayuda a Chihelene pakati pawo anadandaula chifukwa cha Ayuda a Chihebri chifukwa amasiye awo samawagawira chakudya cha tsiku ndi tsiku.
2 Чей дойспрезече ау адунат мулцимя ученичилор ши ау зис: „Ну есте потривит пентру ной сэ лэсэм Кувынтул луй Думнезеу ка сэ служим ла месе.
Tsono Atumwi khumi ndi awiriwo anasonkhanitsa ophunzira onse pamodzi ndipo anati, “Nʼkosayenera kuti ife tisiye kulalikira Mawu a Mulungu ndi kuyangʼanira za chakudya.
3 Де ачея, фрацилор, алеӂець динтре вой шапте бэрбаць ворбиць де бине, плинь де Духул Сфынт ши ынцелепчуне, пе каре ый вом пуне ла служба ачаста.
Choncho abale, sankhani pakati panu anthu asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi anzeru. Ife tidzawapatsa udindo oyangʼanira.
4 Яр ной вом стэруи некурмат ын ругэчуне ши ын проповэдуиря Кувынтулуй.”
Koma ife tidzadzipereka kuti tizipemphera ndi kulalikira mawu.”
5 Ворбиря ачаста а плэкут ынтреӂий адунэрь. Ау алес пе Штефан, бэрбат плин де крединцэ ши де Духул Сфынт, пе Филип, пе Прохор, пе Никанор, пе Тимон, пе Пармена ши пе Николае, ун прозелит дин Антиохия.
Mawu amenewa anakondweretsa gulu lonse la anthu. Iwo anasankha, Stefano, munthu wodzazidwa ndi chikhulupiriro ndiponso Mzimu Woyera; anasankhanso Filipo, Prokoro, Nikanora, Timo, Parmena ndi Nikolao amene anatembenuka mtima ndi kulowa Chiyuda kuchokera kwa Antiokeya.
6 Й-ау адус ынаинтя апостолилор, каре, дупэ че с-ау ругат, шь-ау пус мыниле песте ей.
Iwo anapereka anthuwa kwa atumwi amene anawapempherera ndi kuwasanjika manja.
7 Кувынтул луй Думнезеу се рэспындя тот май мулт, нумэрул ученичилор се ынмулця мулт ын Иерусалим ши о маре мулциме де преоць веняу ла крединцэ.
Ndipo Mawu a Mulungu anapitirira kufalikira. Chiwerengero cha ophunzira mu Yerusalemu chinakula mofulumira ndipo ansembe ochuluka anakhulupirira.
8 Штефан ера плин де хар ши де путере ши фэчя минунь ши семне марь ын нород.
Stefano, munthu wodzazidwa ndi chisomo cha Mulungu ndi mphamvu anachita zodabwitsa ndiponso zizindikiro zazikulu pakati pa anthu.
9 Уний дин синагога нумитэ а Избэвицилор, а Чириненилор ши а Александринилор, ымпреунэ ку ниште иудей дин Чиличия ши дин Асия, ау ынчепут о чартэ де ворбе ку Штефан,
Panauka mtsutso kuchokera kwa anthu a ku Kurene ndi a ku Alekisandriya komanso a ku dera la Silisiya ndi Asiya, otchedwa a Sunagoge ya Mfulu. Anthu amenewa anayamba kutsutsana ndi Stefano.
10 дар ну путяу сэ стя ымпотрива ынцелепчуний ши Духулуй ку каре ворбя ел.
Koma iwo sanathe kumugonjetsa chifukwa iye ankayankhula ndi nzeru zimene Mzimu Woyera anamupatsa.
11 Атунч ау пус ла кале пе ниште оамень сэ зикэ: „Ной л-ам аузит ростинд кувинте де хулэ ымпотрива луй Мойсе ши ымпотрива луй Думнезеу.”
Iwo ananyengerera anthu ena mwamseri kuti anene kuti, “Ife tinamva Stefano akuchitira chipongwe Mose ndiponso Mulungu.”
12 Ау ынтэрытат нородул, пе бэтрынь ши пе кэртурарь, ау нэвэлит асупра луй, ау пус мына пе ел ши л-ау дус ын собор.
Motero anawutsa mitima ya anthu, akulu ndi aphunzitsi amalamulo. Anamugwira Stefano ndi kumubweretsa ku Bwalo Lalikulu.
13 Ау скос ниште марторь минчиношь, каре ау зис: „Омул ачеста ну ынчетязэ сэ спунэ кувинте де хулэ ымпотрива ачестуй локаш сфынт ши ымпотрива Леӂий.
Iwo anabweretsa mboni zonama zimene zinati, “Munthu uyu akupitirirabe kuyankhula mawu onyoza malo oyera ndi malamulo.
14 Ын адевэр, л-ам аузит зикынд кэ ачест Исус дин Назарет ва дэрыма локашул ачеста ши ва скимба обичеюриле пе каре ни ле-а дат Мойсе.”
Pakuti tinamumva akunena kuti Yesu uja wa ku Nazareti adzawononga malo ano ndiponso kusintha miyambo imene Mose anatipatsa.”
15 Тоць чей че шедяу ын собор с-ау уйтат цинтэ ла Штефан, ши фаца луй ли с-а арэтат ка о фацэ де ынӂер.
Onse amene anakhala pansi Mʼbwalo Lalikulu anamuyangʼanitsitsa Stefano, ndipo anaona kuti nkhope yake ikuwala ngati ya mngelo.

< Фаптеле 6 >