< 2 Петру 1 >
1 Симон Петру, роб ши апостол ал луй Исус Христос, кэтре чей че ау кэпэтат о крединцэ де ачелашь прец ку а ноастрэ, прин дрептатя Думнезеулуй ши Мынтуиторулуй ностру Исус Христос:
Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
2 Харул ши пачя сэ вэ фие ынмулците прин куноаштеря луй Думнезеу ши а Домнулуй ностру Исус Христос!
Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
3 Думнезеяска Луй путере не-а дэруит тот че привеште вяца ши евлавия, прин куноаштеря Челуй че не-а кемат прин слава ши путеря Луй,
Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
4 прин каре Ел не-а дат фэгэдуинцеле Луй неспус де марь ши скумпе, ка прин еле сэ вэ фачець пэрташь фирий думнезеешть, дупэ че аць фуӂит де стрикэчуня каре есте ын луме прин пофте.
Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
5 Де ачея, даци-вэ ши вой тоате силинцеле ка сэ униць ку крединца воастрэ фапта; ку фапта, куноштинца;
Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
6 ку куноштинца, ынфрынаря; ку ынфрынаря, рэбдаря; ку рэбдаря, евлавия;
Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
7 ку евлавия, драгостя де фраць; ку драгостя де фраць, юбиря де оамень.
Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
8 Кэч, дакэ авець дин белшуг ачесте лукрурь ын вой, еле ну вэ вор лэса сэ фиць нич ленешь, нич неродиторь ын чея че привеште деплина куноштинцэ а Домнулуй ностру Исус Христос.
Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
9 Дар чине ну аре ачесте лукрурь есте орб, умблэ ку окий ынкишь ши а уйтат кэ а фост курэцит де векиле луй пэкате.
Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
10 Де ачея, фрацилор, кэутаць ку атыт май мулт сэ вэ ынтэриць кемаря ши алеӂеря воастрэ, кэч, дакэ фачець лукрул ачеста, ну вець алунека ничодатэ.
Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
11 Ын адевэр, ын кипул ачеста ви се ва да дин белшуг интраре ын Ымпэрэция вешникэ а Домнулуй ши Мынтуиторулуй ностру Исус Христос. (aiōnios )
Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios )
12 Де ачея вой фи гата сэ вэ адук тотдяуна аминте де лукруриле ачестя, мэкар кэ ле штиць ши сунтець тарь ын адевэрул пе каре-л авець.
Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
13 Дар сокотеск кэ есте дрепт, кыт вой май фи ын кортул ачеста, сэ вэ цин трежь адукынду-вэ аминте,
Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
14 кэч штиу кэ дезбрэкаря де кортул меу ва вени деодатэ, дупэ кум мь-а арэтат Домнул ностру Исус Христос.
chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
15 Ымь вой да остеняла дар ка, ши дупэ моартя мя, сэ вэ путець адуче тотдяуна аминте де ачесте лукрурь.
Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
16 Ын адевэр, в-ам фэкут куноскуте путеря ши вениря Домнулуй ностру Исус Христос ну ынтемеинду-не пе ниште басме мештешуӂит алкэтуите, чи ка уний каре ам вэзут ной ыншине, ку окий ноштри, мэриря Луй.
Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
17 Кэч Ел а примит де ла Думнезеу Татэл чинсте ши славэ, атунч кынд, дин слава минунатэ, с-а аузит дясупра Луй ун глас каре зичя: „Ачеста есте Фиул Меу пряюбит, ын каре Ымь гэсеск плэчеря.”
Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
18 Ши ной ыншине ам аузит ачест глас венинд дин чер, кынд ерам ку Ел пе мунтеле чел сфынт.
Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
19 Ши авем кувынтул пророчией фэкут ши май таре, ла каре бине фачець кэ луаць аминте, ка ла о луминэ каре стрэлучеште ынтр-ун лок ынтунекос, пынэ се ва крэпа де зиуэ ши ва рэсэри лучяфэрул де диминяцэ ын инимиле воастре.
Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
20 Фииндкэ, май ынтый де тоате, сэ штиць кэ ничо пророчие дин Скриптурэ ну се тылкуеште сингурэ.
Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
21 Кэч ничо пророчие н-а фост адусэ прин воя омулуй; чи оамений ау ворбит де ла Думнезеу, мынаць де Духул Сфынт.
Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.