< 1 Иоан 4 >
1 Пряюбицилор, сэ ну даць крезаре орькэруй дух, чи сэ черчетаць духуриле дакэ сунт де ла Думнезеу; кэч ын луме ау ешит мулць пророчь минчиношь.
Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi.
2 Духул луй Думнезеу сэ-Л куноаштець дупэ ачаста: Орьче дух каре мэртурисеште кэ Исус Христос а венит ын труп есте де ла Думнезеу;
Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu,
3 ши орьче дух каре ну мэртурисеште пе Исус ну есте де ла Думнезеу, чи есте духул антихристулуй, де а кэруй венире аць аузит. Ел кяр есте ын луме акум.
koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.
4 Вой, копилашилор, сунтець дин Думнезеу ши й-аць бируит, пентру кэ Чел че есте ын вой есте май маре декыт чел че есте ын луме.
Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi.
5 Ей сунт дин луме; де ачея ворбеск ка дин луме ши лумя ый аскултэ.
Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera.
6 Ной ынсэ сунтем дин Думнезеу; чине куноаште пе Думнезеу не аскултэ; чине ну есте дин Думнезеу ну не аскултэ. Прин ачаста куноаштем духул адевэрулуй ши духул рэтэчирий.
Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.
7 Пряюбицилор, сэ не юбим уний пе алций; кэч драгостя есте де ла Думнезеу. Ши орьчине юбеште есте нэскут дин Думнезеу ши куноаште пе Думнезеу.
Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu.
8 Чине ну юбеште н-а куноскут пе Думнезеу, пентру кэ Думнезеу есте драгосте.
Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi.
9 Драгостя луй Думнезеу фацэ де ной с-а арэтат прин фаптул кэ Думнезеу а тримис ын луме пе сингурул Сэу Фиу, ка ной сэ трэим прин Ел.
Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo.
10 Ши драгостя стэ ну ын фаптул кэ ной ам юбит пе Думнезеу, чи ын фаптул кэ Ел не-а юбит пе ной ши а тримис пе Фиул Сэу ка жертфэ де испэшире пентру пэкателе ноастре.
Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu.
11 Пряюбицилор, дакэ астфел не-а юбит Думнезеу пе ной, требуе сэ не юбим ши ной уний пе алций.
Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake.
12 Нимень н-а вэзут вреодатэ пе Думнезеу; дакэ не юбим уний пе алций, Думнезеу рэмыне ын ной ши драгостя Луй а ажунс десэвыршитэ ын ной.
Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.
13 Куноаштем кэ рэмынем ын Ел ши кэ Ел рэмыне ын ной прин фаптул кэ не-а дат дин Духул Сэу.
Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake.
14 Ши ной ам вэзут ши мэртурисим кэ Татэл а тримис пе Фиул ка сэ фие Мынтуиторул лумий.
Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.
15 Чине ва мэртуриси кэ Исус есте Фиул луй Думнезеу, Думнезеу рэмыне ын ел, ши ел, ын Думнезеу.
Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu.
16 Ши ной ам куноскут ши ам крезут драгостя пе каре о аре Думнезеу фацэ де ной. Думнезеу есте драгосте ши чине рэмыне ын драгосте рэмыне ын Думнезеу, ши Думнезеу рэмыне ын ел.
Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye.
17 Кум есте Ел, аша сунтем ши ной ын лумя ачаста, астфел се фаче кэ драгостя есте десэвыршитэ ын ной, пентру ка сэ авем деплинэ ынкредере ын зиуа жудекэций.
Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu.
18 Ын драгосте ну есте фрикэ, чи драгостя десэвыршитэ изгонеште фрика, пентру кэ фрика аре ку еа педяпса; ши чине се теме н-а ажунс десэвыршит ын драгосте.
Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.
19 Ной Ыл юбим пентру кэ Ел не-а юбит ынтый.
Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda.
20 Дакэ зиче чинева: „Еу юбеск пе Думнезеу” ши урэште пе фрателе сэу, есте ун минчинос, кэч чине ну юбеште пе фрателе сэу, пе каре-л веде, кум поате сэ юбяскэ пе Думнезеу, пе каре ну-Л веде?
Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone.
21 Ши ачаста есте порунка пе каре о авем де ла Ел: чине юбеште пе Думнезеу юбеште ши пе фрателе сэу.
Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.