< Romani 2 >
1 De aceea, omule, ești de nescuzat, oricine ai fi care judeci; fiindcă în ceea ce judeci pe altul, te condamni pe tine însuți; fiindcă tu care judeci, practici aceleași lucruri.
Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
2 Dar suntem siguri că judecata lui Dumnezeu este conform adevărului împotriva celor ce practică astfel de lucruri.
Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
3 Și gândești aceasta, omule, care judeci pe cei ce practică astfel de lucruri și pe care le faci și tu, că vei scăpa de judecata lui Dumnezeu?
Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
4 Sau disprețuiești bogățiile bunătății lui și a îngăduinței și a îndelungii răbdări, neștiind că bunătatea lui Dumnezeu te conduce la pocăință?
Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
5 Dar după împietrirea ta și inima nepocăită, îți strângi furie pentru ziua furiei și a revelării dreptei judecăți a lui Dumnezeu;
Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
6 Care va întoarce fiecărui om conform faptelor lui;
Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
7 Celor care prin răbdare stăruitoare în facerea binelui caută glorie și onoare și nemurire, viață eternă; (aiōnios )
Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios )
8 Dar celor certăreți și care nu ascultă de adevăr, ci ascultă de nedreptate, indignare și furie,
Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
9 Necaz și chin peste fiecare suflet de om care lucrează răul, întâi al iudeului și de asemenea al neamului.
Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
10 Dar glorie, onoare și pace fiecăruia care lucrează binele, întâi iudeului și de asemenea neamului.
Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
11 Deoarece la Dumnezeu nu este părtinire.
Pajatu Mulungu alibe tsankho.
12 Căci atâți câți au păcătuit fără lege, vor și pieri fără lege; și atâți câți au păcătuit în lege, vor fi judecați prin lege;
Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
13 (Fiindcă nu ascultătorii legii sunt drepți înaintea lui Dumnezeu, ci înfăptuitorii legii vor fi declarați drepți.
Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
14 De aceea când neamurile, care nu au legea, fac prin natură lucrurile cuprinse în lege, aceștia, neavând legea, își sunt lor înșiși lege;
Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
15 Aceștia arată lucrarea legii scrisă în inimile lor, conștiința lor de asemenea aducând mărturie și gândurile lor, în același timp acuzându-se sau scuzându-se unele pe altele),
Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
16 În ziua când Dumnezeu va judeca tainele oamenilor prin Isus Cristos, conform evangheliei mele.
Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
17 Iată, tu, te numești iudeu și te bazezi pe lege și te fălești cu Dumnezeu,
Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
18 Și îi știi voia și deosebești lucruri nespus mai bune, fiind învățat din lege;
ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
19 Și ești sigur că tu însuți ești călăuză orbilor, lumină celor ce sunt în întuneric,
ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
20 Îndrumător al celor fără minte, învățător al pruncilor, având forma cunoașterii și a adevărului în lege.
mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
21 Tu dar, care înveți pe altul, pe tine însuți nu te înveți? Tu care predici: Să nu furi; furi?
tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
22 Tu care spui: Să nu comiți adulter; comiți adulter? Tu care detești idolii, comiți sacrilegiu?
Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
23 Tu care te fălești cu legea, îl dezonorezi pe Dumnezeu prin încălcarea legii?
Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
24 Fiindcă prin voi este blasfemiat numele lui Dumnezeu între neamuri, așa cum este scris.
Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
25 Fiindcă circumcizia, într-adevăr, este de folos, dacă împlinești legea; dar dacă ești călcător de lege, circumcizia ta a devenit necircumcizie.
Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
26 De aceea dacă necircumcizia ține dreptatea legii, necircumcizia lui nu i se va socoti pentru circumcizie?
Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
27 Și necircumcizia care este prin natură, dacă împlinește legea, nu te va judeca pe tine, care prin litera legii și prin circumcizie calci legea?
Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
28 Fiindcă iudeu nu este cel în afară; nici circumcizie cea pe dinafară, în carne;
Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
29 Ci iudeu este cel în lăuntru; și circumcizie este aceea a inimii, în duhul, nu în literă; a cărui laudă nu este de la oameni, ci de la Dumnezeu.
Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.