< Filipeni 1 >

1 Pavel și Timotei, robi ai lui Isus Cristos, tuturor sfinților în Cristos Isus care sunt în Filipi, împreună cu episcopii și diaconii;
Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
2 Har vouă și pace de la Dumnezeu Tatăl nostru și de la Domnul Isus Cristos.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
3 Mulțumesc Dumnezeului meu la fiecare aducere aminte despre voi,
Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
4 Întotdeauna, în fiecare rugăciune a mea pentru voi toți, făcând cerere cu bucurie,
Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
5 Pentru părtășia voastră în evanghelie, din prima zi până acum;
chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
6 Fiind încredințat de acest lucru, că cel ce a început o bună lucrare în voi, o va termina până în ziua lui Isus Cristos.
Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
7 Așa cum este drept pentru mine să gândesc aceasta despre voi toți, pentru că vă port în inima mea; întrucât, deopotrivă în lanțurile mele și în apărarea și confirmarea evangheliei, voi toți sunteți părtași ai harului meu.
Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
8 Fiindcă Dumnezeu îmi este martor cât de mult tânjesc după voi toți în adâncurile milei lui Isus Cristos.
Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
9 Și aceasta mă rog, ca dragostea voastră să abunde chiar din ce în ce mai mult în cunoaștere și în toată judecata,
Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
10 Ca voi să deosebiți lucrurile alese, ca să fiți sinceri și fără poticnire până în ziua lui Cristos,
kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
11 Fiind umpluți cu roadele dreptății, care sunt prin Isus Cristos, pentru gloria și lauda lui Dumnezeu.
Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
12 Dar voiesc să înțelegeți, fraților, că cele ce mi s-au întâmplat, mai degrabă au ajutat la înaintarea evangheliei;
Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
13 Așa că lanțurile mele în Cristos sunt arătate în tot palatul și în toate celelalte locuri.
Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
14 Și mulți dintre frații în Domnul, încredințați din cauza lanțurilor mele, sunt mult mai cutezători să vorbească fără teamă cuvântul.
Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
15 Unii, într-adevăr, predică pe Cristos chiar din invidie și ceartă; iar alții, de asemenea, din bunăvoință.
Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
16 Unii predică pe Cristos din ceartă, nu sincer, închipuindu-și că adaugă necaz lanțurilor mele;
Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
17 Iar ceilalți, din dragoste, știind că sunt pus pentru apărarea evangheliei.
Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
18 Atunci ce este? Cu toate acestea, în orice fel, fie de ochii lumii, fie în adevăr, Cristos este predicat; și în aceasta mă bucur, da și mă voi bucura.
Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
19 Căci știu că aceasta se va întoarce pentru salvarea mea prin rugăciunea voastră și prin aportul Duhului lui Isus Cristos,
pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
20 Conform anticipării mele arzătoare și speranței mele, că nu voi fi în nimic rușinat, ci cu toată cutezanța, ca întotdeauna, așa și acum Cristos va fi preamărit în trupul meu, fie prin viață, fie prin moarte.
Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
21 Fiindcă pentru mine a trăi este Cristos, și a muri este câștig.
Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
22 Dar dacă trăiesc în carne, aceasta este rodul muncii mele; totuși nu știu ce voi alege.
Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
23 Fiindcă sunt strâmtorat din două părți, având dorință să plec și să fiu cu Cristos, ceea ce este mult mai bine;
Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
24 Totuși, a rămâne în carne este mai necesar pentru voi.
Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
25 Și, având această încredere, știu că voi trăi și voi continua cu voi toți, pentru înaintarea voastră și bucuria credinței,
Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
26 Ca bucuria voastră să fie mai abundentă în Isus Cristos pentru mine, prin venirea mea din nou la voi.
kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
27 Numai purtați-vă cum se cuvine evangheliei lui Cristos, pentru ca, fie că vin și vă văd, fie că sunt absent, să aud despre ale voastre că stați neclintiți într-un singur duh, cu o singură minte, luptând împreună pentru credința evangheliei,
Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
28 Și nefiind înspăimântați în nimic de potrivnicii voștri, ceea ce le este o dovadă a pieirii, dar vouă a salvării, și aceasta de la Dumnezeu.
osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
29 Fiindcă vouă vă este dat, pe partea lui Cristos, nu numai a crede în el, dar și a suferi pentru el.
Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
30 Având același conflict pe care l-ați văzut în mine și acum auziți că este în mine.
Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.

< Filipeni 1 >