< Isaia 53 >

1 Cine a crezut vestea noastră şi cui i s-a arătat braţul DOMNULUI?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Fiindcă el va creşte înaintea lui ca un lăstar şi ca o rădăcină dintr-un pământ uscat, nu va avea nici formă nici frumuseţe; şi când îl vom vedea, nu va avea frumuseţe ca să îl dorim.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 El este dispreţuit şi respins de oameni; un om al întristărilor şi obişnuit cu mâhnirea, şi ne-am ascuns de el cum ne-am ascunde feţele, a fost dispreţuit şi noi nu l-am preţuit.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Cu adevărat el a purtat mâhnirile noastre şi a luat asupra lui întristările noastre, totuşi l-am socotit bătut, lovit de Dumnezeu şi chinuit.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Dar el a fost rănit pentru fărădelegile noastre, zdrobit pentru nelegiuirile noastre, pedeapsa păcii noastre a fost asupra lui; şi prin loviturile lui suntem vindecaţi.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Noi toţi ca oi am rătăcit; ne-am întors fiecare la propria cale; şi DOMNUL a aşezat pe el nelegiuirea noastră a tuturor.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 A fost oprimat şi a fost chinuit, totuşi nu şi-a deschis gura, este adus ca un miel la măcel, ca o oaie mută înaintea tunzătorilor, astfel nu şi-a deschis gura.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 A fost luat de la închisoare şi de la judecată, şi cine va vesti generaţia lui? Fiindcă a fost stârpit din ţara celor vii, pentru fărădelegea poporului meu a fost el lovit.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Şi în moartea lui şi-a rânduit mormântul cu cei stricaţi şi cu cei bogaţi, pentru că nu făcuse nimic violent, nici nu era vreo înşelăciune în gura lui.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Totuşi DOMNULUI i-a plăcut să îl zdrobească; l-a supus suferinţei; când tu îi vei face sufletul o ofrandă pentru păcat, el va vedea sămânţa lui, îşi va prelungi zilele şi plăcerea DOMNULUI va prospera în mâna lui.
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Va vedea din rodul ostenelii sufletului său şi va fi satisfăcut, prin cunoaşterea lui, servitorul meu cel drept va declara drepţi pe cei mulţi; şi el va lua asupra lui nelegiuirile lor.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 De aceea îi voi da partea lui cu cei mari şi va împărţi prada cu cei puternici, pentru că şi-a turnat sufletul până la moarte şi a fost numărat cu călcătorii [de lege]; şi a purtat păcatul multora şi a mijlocit pentru călcătorii [de lege].
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.

< Isaia 53 >