+ Luka 1 >

1 Cenimeja Teofile, but džene lelje te pisinen oto događaja save ule maškar amende.
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 On pisinde ađahar sar so vaćerde amenđe okola kola taro anglunipe dikhle adala događaja hem kola inele sluge zako e Devlesoro lafi.
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 Ađahar hem me, palo adava so taro anglunipe šukar ispitujinđum sa adava, mangljum tuće sa palo redo te pisinav,
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 te šaj ove uverime dai čače sa adava so injan sikavdo.
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 Kad o Irod inele caro ani Judeja, nesavo manuš palo anav Zaharija inele svešteniko e izraelconengoro, oto redo e Avijasoro. E Zaharijasiri romni da inele oto pleme e Aaronesoro. Lakoro anav inele Jelisaveta.
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 O Zaharija hem i Jelisaveta inele pravedna anglo Devel, adalese so živinde palo sa o naredbe hem o zakonja e Gospodesere.
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 Olen na ine čhave adalese so i Jelisaveta našti ine te ačhol khamni, a soduj džene već purandile.
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 Jekh dive kad e Zaharijasiri grupa oto sveštenici kandlja ano Hram, tegani hem o Zaharija ćerela ine pli buti sar svešteniko anglo Devel.
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 Ov, palo adeti e sveštenikonengoro, barbuteja inele izabirime te đerdini ko Hram e Gospodesoro hem te kadini.
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 Sar o Zaharija kadini ine ano Hram, sa edobor narodo molini pe ine avri.
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 A ano Hram e Zaharijase mothovđa pe o anđeo e Gospodesoro, kova terdino ki desno strana oto žrtveniko kotar kadinđa pe.
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 Kad o Zaharija dikhlja le, uznemirinđa pe hem but darandilo.
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 A o anđeo phenđa lese: “Ma dara, Zaharija! O Devel šunđa ti molitva. Ti romni i Jelisaveta ka bijani će čhave, i ka de le anav Jovan.
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 Ka ove but radosno zbog leste hem but džene ka radujinen pe so ov ka bijanđol,
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 adalese so ka ovel baro manuš anglo Gospod. Nikad naka pijel mol hem ništa sostar šaj te mačol pe. Ka ovel pherdo e Svetone Duhoja pana pe dajaće ano vođi.
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 Bute Izraelconen ka irini anglo Gospod, anglo lengoro Devel.
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 Ka džal anglo Gospod sar glasniko ano duho hem ano zoralipe e prorokosoro e Ilijasoro. Ka mirini e daden lengere čhavencar hem okolen so na šunena ka irini nakori mudrost e pravednikonengiri. Ka pripremini e narodo te oven spremna zako e Gospodesoro aviba.”
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 I o Zaharija pučlja e anđeo: “Sar me te džanav da čače ka ovel adava so phenđan? Me injum purano hem mli romni da beršali.”
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 A o anđeo phenđa lese: “Me injum o Gavrilo, o anđeo kova terđola anglo Devel. Ov bičhalđa man te vaćerav tuja hem te anav će akava šukar lafi.
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 I ače, ka ove laloro, naka šaj te vaćere sa đi o dive kad adava ka ovel, adalese so na verujinđan mle lafenđe save ka pherđoven ano pravo vreme.”
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 Sar o anđeo vaćeri ine e Zaharijaja, o narodo kova adžićerđa avri čudinđa pe so o Zaharija edobor ačhilo ano Hram.
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 A kad o Zaharija iklilo, našti ine te vaćeri olencar. Ćerela ine nesar te mothoj lenđe vastencar, ali ačhilo laloro. O manuša halile da ole ine vizija ano Hram.
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 Kad pherdile o dive oti lesiri služba ano Hram, o Zaharija irinđa pe čhere.
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 Na nakhlo but, i lesiri romni i Jelisaveta ačhili khamni hem pandž masek na iklili avri taro čher. Phenđa:
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 “O Gospod ćerđa te šaj ačhovav khamni. Akana mothovđa maje pli milost hem cidinđa mli lađ anglo manuša.”
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 Kad i Jelisaveta inele šofto masek khamni, o Devel bičhalđa ple anđeo e Gavrilo ki diz Nazaret ani regija Galileja.
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 Adari valjanđa te legari o lafi e Marijaće koja pana inele čhaj. Oj inele mangli e muršese palo anav Josif, kova inele oto pleme e carosoro e Davidesoro.
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 Kad alo o anđeo, phenđa e Marijaće: “Radujin tut! O Gospodi tuja! Ovi but milostivno premala tute!”
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 A i Marija but uznemirinđa pe zbog e anđeosere lafija, i pučlja pe so šaj te značini adava pozdrav.
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 A o anđeo phenđa laće: “Ma dara, Marije! O Devel mothovđa će pli milost!
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 Ače, ka ačhove khamni hem ka bijane čhave, i ka de le anav Isus.
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 Ov ka ovel baro hem ka vičini pe Čhavo e Najbare Devlesoro. O Devel o Gospod ka del le o presto lesere pradadesoro e Davidesoro.
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 Ka carujini upro pleme e Jakovesoro zauvek; zako lesoro carstvo naka ovel kraj.” (aiōn g165)
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
34 Tegani i Marija pučlja e anđeo: “Sar šaj te ovel adava kad me pana injum čhaj?”
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 A o anđeo phenđa laće: “O Sveto Duho ka huljel upra tute hem o zoralipe e Najbare Devlesoro ka učhari tut. Adalese adava čhavo, kole ka bijane, ka ovel sveto hem ka vičini pe Čhavo e Devlesoro.
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 Eče, ti bibi i Jelisaveta da, ko purane berša, ačhili khamni hem ka bijani murše. I oj, kolaće sare džande da našti te ačhol khamni, akanai šov masek khamni.
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 Adalese so o Devel sa šaj te ćerel!”
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 Tegani i Marija phenđa: “Ače, sluškinja e Gospodesiri injum. Nek ovel maje palo to lafi.” I o anđeo dželo olatar.
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 Adala dive i Marija spreminđa pe hem siđarđa ko bregalo krajo, ki jekh diz ani regija Judeja.
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 Kad resli adari, đerdinđa ko čher e Zaharijasoro hem pozdravinđa e Jelisaveta.
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 I kad i Jelisaveta šunđa e Marijakoro pozdrav, o čhavoro oti radost zorale mrdinđa olaće ano vođi, a oj pherdili e Svetone Duhoja.
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 I bare glasoja phenđa e Marijaće: “Najblagoslovime injan maškaro đuvlja hem blagoslovime o čhavoro kole akhareja ano vođi!
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 Akavai bari čast maje so tu, mle Gospodesiri daj, aljan kora mande.
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 Adalese so, kad šunđum to pozdrav, o čhavoro oti radost zorale mrdinđa maje ano vođi.
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 Blago tuće so verujinđan da ka ovel adava so phenđa će o Gospod!”
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 Tegani i Marija phenđa: “Mli duša barjari e Gospode;
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 Mloi duho radosno ano Devel, ano mlo Spasitelj,
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 so ulo milostivno upri poniznost ple sluškinjakiri. I ače, od akana sa o generacije ka phenen da injum blagoslovime đuvli,
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 adalese so bare šukaripa ćerđa maje o Zoralo Devel kasoroi anav sveto!
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 Ovi milostivno e manušenđe tari generacija ki generacija kola darana olestar.
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 Ple zorale vasteja ćerđa bare buća; rasfrdinđa e manušen kolai barikane ano pumare vile.
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 Peravđa e vladaren taro lengoro prestolje, a vazdinđa e poniznonen.
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 Čaljarđa e bokhalen šukaripnaja, a čučen muklja e barvalen.
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 Pomožinđa e Izraelconenđe, ple slugenđe. Na bisterđa te ovel milostivno
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 e Avraamese hem lesere potomkonenđe zauvek, sar so dinđa plo lafi amare pradadenđe.” (aiōn g165)
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
56 I Marija ačhili e Jelisavetaja đi sar trin masek, i tegani irinđa pe čhere.
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 A kad alo o vreme i Jelisaveta te bijani, bijanđa murše.
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 Kad lakiri familija hem lakere komšije šunde so o Gospod mothovđa laće bari milost, radujinde pe olaja.
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 A kad e čhavore inele ofto dive, koro Zaharija čedinde pe o manuša zako obreziba e čhavoresoro. I mangle te den le lesere dadesoro anav – Zaharija,
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 ali i Jelisaveta phenđa: “Na! Lesoro anav ka ovel Jovan!”
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 A on phende laće: “Niko te familijatar na vičini pe ađahar.”
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 I vastencar pučle e Zaharija savo anav mangela te del ple čhavore.
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 Tegani o Zaharija rodinđa te den le jekh tikori phal zako pisiba hem pisinđa: “Lesoro anavi Jovan.” I sare začudinde pe.
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 I otojekhvar e Zaharijasoro muj phravdilo hem šaj ine palem te vaćeri, i lelja te slavini e Devle.
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 I uklinđa i dar sa lengere komšijen. Ko sa o bregalo krajo e Judejakoro vaćerđa pe adalestar so ulo.
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 I sare kola šunde adava, razmislinde adalestar hem phende: “Akava čhavoro isi te ovel baro manuš. Čačei upro leste o vas e Gospodesoro.”
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 A o Zaharija, e Jovanesoro dad, pherdilo e Svetone Duhoja hem prorokujinđa:
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 “Slava e Gospodese e Izraelesere Devlese, adalese so alo hem otkupinđa ple narodo!
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 Vazdinđa amenđe e zorale Spasitelje oto pleme e carosoro e Davidesoro, ple slugasoro,
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 sar so vaćerđa pana angleder prekalo muja ple svetone prorokonengere. (aiōn g165)
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
71 Vazdinđa amenđe zorale Spasitelje te spasini amen amare neprijateljendar hem sa e manušengere vastendar kola mrzinena amen.
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 Mothovđa milost amare pradadenđe hem ispuninđa plo sveto savez,
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 i sovli savi halja e Avraamese amare pradadese:
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 so ka ikali amen amare neprijateljengere vastendar te šaj služina lese bizi dar
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 ani svetost hem ani pravednost anglo leste sa đikote injam dživde.
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 A tu Jovane, mlo čhavo, ka ove pendžardo sar proroko e Najbare Devlesoro, adalese so ka dža anglo Gospod te pripremine lese o drom.
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 Ka sikave lesere narodo sar te pendžaren o spasenje prekalo oprostiba lengere grehija
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 zbog amare Devlesoro milosrdno vilo palo savo o svetlost odupral ka avel kora amende sar ikljojba e khamesoro,
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 te svetlini okolenđe so bešena ani tomina hem ani senka e meribnasiri, te legari amen ko drom oto mir.”
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 A o čhavoro o Jovan barjola ine hem zoraljola ano duho. Kad barilo, živinđa ani pustinja sa đikote na iklilo anglo Izraelci te propovedini.
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

+ Luka 1 >