< Salmos 94 >

1 Yahweh, seu Deus a quem pertence a vingança, Deus a quem pertence a vingança, resplandece.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Levantem-se, vocês julgam da terra. Retribuir com orgulho o que eles merecem.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Yahweh, por quanto tempo os ímpios vão durar, por quanto tempo os ímpios triunfarão?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Eles despejam palavras arrogantes. Todos os malfeitores se vangloriam.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Eles quebram seu povo em pedaços, Yahweh, e afligir sua herança.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 They matar a viúva e o estrangeiro, e assassinar os órfãos de pai.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Eles dizem: “Yah não vai ver”, nem o Deus de Jacó irá considerar”.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Considere, você não sente nada entre o povo; seus tolos, quando vocês serão sábios?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Aquele que implantou o ouvido, será que ele não ouve? Aquele que formou o olho, ele não verá?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Aquele que disciplina as nações, não castigará ele? Aquele que ensina o homem sabe.
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Yahweh conhece os pensamentos do homem, que eles são fúteis.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Abençoado é o homem a quem você disciplina, Sim, e ensinar a partir de sua lei,
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 que você pode lhe dar descanso dos dias de adversidade, até que o poço seja cavado para os malvados.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Pois Yahweh não rejeitará seu povo, nem renunciará à sua herança.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Para o julgamento voltará à retidão. Todos os retos de coração devem segui-lo.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Quem se levantará por mim contra os ímpios? Quem vai me defender contra os malfeitores?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Unless Yahweh tinha sido minha ajuda, minha alma teria logo vivido em silêncio.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Quando eu disse: “Meu pé está escorregando”! Sua bondade amorosa, Yahweh, me atrasou.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Na multidão de meus pensamentos dentro de mim, seus confortos enchem minha alma.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Shall o trono da maldade tem companheirismo com você, o que traz maldades por lei?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Eles se reúnem contra a alma dos justos, e condenar o sangue inocente.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Mas Yahweh tem sido minha torre alta, meu Deus, a rocha do meu refúgio.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Ele trouxe sobre eles sua própria iniqüidade, e os cortará em sua própria maldade. Yahweh, nosso Deus, vai cortá-los.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Salmos 94 >