< Salmos 29 >
1 Um salmo de David. Atribuam a Yahweh, filhos dos poderosos, atribuem a Yahweh glória e força.
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Atribuir a Yahweh a glória devido a seu nome. Adorar Yahweh em santa disposição.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 A voz de Yahweh está sobre as águas. O Deus da glória troveja, até mesmo Yahweh em muitas águas.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 A voz de Yahweh é poderosa. A voz de Yahweh está cheia de majestade.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 A voz de Yahweh quebra os cedros. Sim, Yahweh quebra em pedaços os cedros do Líbano.
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 Ele também os faz pular como um bezerro; Líbano e Sirion como um boi jovem e selvagem.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 A voz de Yahweh bate com flashes de relâmpagos.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 A voz de Yahweh abala o sertão. Yahweh abala o deserto de Kadesh.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 A voz de Yahweh faz o veado parir, e despoja as florestas. Em seu templo tudo diz: “Glória!”
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Yahweh sentou-se entronizado no Dilúvio. Sim, Yahweh senta-se como Rei para sempre.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Yahweh dará força ao seu povo. Yahweh abençoará seu povo com paz.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.