< Salmos 102 >
1 Uma Oração dos aflitos, quando ele está sobrecarregado e derrama sua reclamação diante de Yahweh. Hear minha oração, Yahweh! Deixem meu choro chegar até vocês.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Don não esconda seu rosto de mim no dia da minha angústia. Vire seu ouvido para mim. Responda-me rapidamente no dia em que eu ligar.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Para meus dias, consumir fora como fumaça. Meus ossos estão queimados como uma tocha.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Meu coração está arruinado como a grama, e murcha, pois esqueci de comer meu pão.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Por causa da voz do meu gemido, meus ossos colam-se à minha pele.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Eu sou como um pelicano do deserto. Eu me tornei como uma coruja dos lugares de desperdício.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Eu assisto, e me tornei como um pardal que está sozinho no topo da casa.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Meus inimigos me censuram o dia todo. Aqueles que estão zangados comigo, usam meu nome como uma maldição.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Pois eu já comi cinzas como pão, e misturei minha bebida com lágrimas,
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 por causa de sua indignação e sua cólera; pois você me pegou e me jogou fora.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Meus dias são como uma longa sombra. Eu murchei como a grama.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Mas você, Yahweh, permanecerá para sempre; sua fama perdura para todas as gerações.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Você se levantará e terá piedade de Zion, pois é hora de ter piedade dela. Sim, chegou a hora estabelecida.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Para seus criados, tenha prazer em suas pedras, e tenha piedade de sua poeira.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Assim as nações temerão o nome de Yahweh, todos os reis da terra, sua glória.
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Pois Yahweh construiu Zion. Ele apareceu em sua glória.
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Ele respondeu à oração dos indigentes, e não desprezou suas orações.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 This será escrito para a geração vindoura. Um povo que será criado elogiará o Yah,
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 pois ele olhou para baixo desde a altura de seu santuário. Do céu, Yahweh viu a terra,
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 para ouvir os gemidos do prisioneiro, para libertar aqueles que estão condenados à morte,
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 para que os homens possam declarar o nome de Yahweh em Zion, e seus elogios em Jerusalém,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 quando os povos estão reunidos, os reinos, para servir a Yahweh.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Ele enfraqueceu minhas forças ao longo do curso. Ele encurtou meus dias.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Eu disse: “Meu Deus, não me leve embora no meio dos meus dias. Seus anos são ao longo de todas as gerações.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 De outrora, você lançou os alicerces da terra. Os céus são o trabalho de suas mãos.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Eles perecerão, mas você perdurará. Sim, todos eles vão se desgastar como uma peça de vestuário. Você os mudará como um manto, e eles serão mudados.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Mas você é o mesmo. Seus anos não terão fim.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Os filhos de seus criados continuarão. Seus descendentes serão estabelecidos diante de você”.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”